< Amahubo 92 >

1 Ihubo. Ingoma. Elosuku lweSabatha. Kuhle ukudumisa uThixo lokuhlabelela ebizweni lakho, wena oPhezukonke,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 ukumemezela uthando lwakho ekuseni lokuthembeka kwakho ebusuku,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 ukutshaya iziginci ngomhubhe wezintambo ezilitshumi lemvungamo emnandi yechacho.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 Ngoba uyangijabulisa ngezenzo zakho, Oh Thixo; ngihlala ngentokozo ngomsebenzi wezandla zakho.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Mikhulu kangaka imisebenzi yakho, Oh Thixo, izikile imicabango yakho!
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 Umuntu ongelangqondo akazi, iziwula kazizwisisi,
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 ukuthi loba ababi bemila njengotshani lezigangi zonke ziphumelela, zizabhujiswa nini lanini.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 Kodwa wena Thixo, uphakeme laphakade.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Ngoba ngempela izitha zakho, Oh Thixo, ngempela izitha zakho zizabhubha; zonke izigangi zizachithizwa.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Uluphakamisile uphondo lwami njengolwenyathi; ngagcotshwa ngamakha amnandi.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Amehlo ami abonile ukwehlulwa kwezitha zami; indlebe zami zizwile ngokuchithizwa kwezitha zami ezimbi.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 Abalungileyo bazaqhela njengesihlahla selala, bazakhula njengomsedari waseLebhanoni;
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 ngoba behlanyelwe endlini kaThixo, bazaqhela emagumeni kaNkulunkulu wethu.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Bazabe belokhu bethela izithelo lanxa sebebadala, bazahlala belokhu behluma beluhlaza,
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 bememezela besithi, “UThixo uqotho; uliDwala lami, kakukho bubi kuye.”
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Amahubo 92 >