< Amahubo 74 >

1 Ihubo lika-Asafu Kungani ususilahlile kokuphela na, awu Nkulunkulu? Kungani ulaka lwakho luvutha phezu kwezimvu zedlelo lakho na?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Khumbula abantu owabathengayo ekadeni, isizwe selifa lakho owasihlengayo iNtaba iZiyoni, owawuhlala khona.
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Phenduka ungene emanxiweni aphakade la, incithakalo yonke le yenziwe yisitha endlini engcwele.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Izitha zakho zazibhonga endaweni owawuhlangana lathi kuyo; zamisa impawu zazo njengeziboniso.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 Zenza njengabantu abaphakamise amahloka ukuphendla indlela yabo eguswini.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 Zafohloza konke okubaziweyo ngamahloka azo langezando.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 Zatshisa indlu yakho engcwele yaphela nya; zangcolisa indawo ehlala iBizo lakho.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 Zathi ngezinhliziyo zazo, “Sizababhuqa baphele nya!” Zatshisa zonke izindawo zokukhonzela uNkulunkulu elizweni.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 Kasisaboniswa mimangaliso; kakuselabuphrofethi, kakho kithi owaziyo ukuthi kuzaze kube nini kunjalo.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 Koze kube nini isitha sikuklolodela na, awu Nkulunkulu? Izitha zizalithuka kokuphela ibizo lakho na?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Kungani ufinyeza isandla sakho sokunene na? Sikhuphe ezingoxweni zezembatho zakho ubabhubhise.
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Kodwa wena Nkulunkulu uyiNkosi yami kwasekadeni; uletha insindiso emhlabeni.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Kwakunguwe owaqhekeza ulwandle ngamandla akho; wafohloza amakhanda esilo phakathi kwamanzi.
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Kwakunguwe owachoboza amakhanda kaLeviyathani waba yikudla kwezidalwa zasenkangala.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Kwakunguwe owavula imithombo lemifula; womisa qha imifula eyayihlala igeleza.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Imini ngeyakho, ngobakho njalo lobusuku; walimisa ilanga kanye lenyanga.
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Kwakunguwe owamisa imingcele yonke yomhlaba; wenza ihlobo kanye lobusika.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Khumbula ukuthi isitha besikuklolodela, Thixo, ukuthi iziwula bezihlambaza ibizo lakho.
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Ungaqhubeli umphefumulo wejuba lakho ezinyamazaneni; ungaze wakhohlwa kokuphela impilo yabantu bakho abahluphekayo.
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Nanzelela isivumelwano sakho, ngoba izikhundla zobugebenga zigcwele kulolonke ilizwe ezindaweni ezilamathunzi.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Ungayekeli abancindezelweyo babuyele beyangekile; sengathi abayanga labaswelayo bangalidumisa ibizo lakho.
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Phakama, awu Nkulunkulu, vikela okungokwakho; khumbula ukuthi iziwula zikuhleka njani ilanga lonke.
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Ungakulibali ukuvungama kwalabo abalwa lawe, ukuxokozela kwezitha zakho, okuzwakala kokuphela.
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

< Amahubo 74 >