< Amahubo 62 >
1 Kumqondisi wokuhlabela. KuJeduthuni. Ihubo likaDavida. Umphefumulo wami ufumana ukuphumula kuNkulunkulu kuphela; ukusindiswa kwami kuvela kuye.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
2 Yena yedwa uyilo idwala lami lensindiso yami; uyinqaba yami, kangisoze ngihlukunyezwe lanini.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
3 Koze kube nini lilokhu lihlukuluza umuntu na? Lonke lizamlahla phansi na yena ongumduli otshekileyo, oluthango olutebhayo?
Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
4 Bazimisele ukumqethula esikhundleni sakhe esiphezulu; bathokoziswa ngamanga. Ngemilomo yabo bayabusisa, kodwa ezinhliziyweni zabo bayaqalekisa.
Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
5 Fumana ukuphumula, Oh mphefumulo wami, kuNkulunkulu kuphela; ithemba lami livela kuye.
Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
6 Yena yedwa ulidwala lami lensindiso; uyinqaba yami, kangisoze ngihlukunyezwe.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
7 Insindiso yami lodumo lwami kweyeme kuNkulunkulu; ulidwala lami eliqinileyo, isiphephelo sami.
Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
8 Thembani kuye ngezikhathi zonke, lina bantu; likhuphe konke okusezinhliziyweni zenu kuye, ngoba uNkulunkulu uyisiphephelo sethu.
Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
9 Abantukazana bangumoya nje, izikhulu ziyinkohliso nje; aluba belinganiswa esikalini kabasilutho; bonke ndawonye bangumoya kuphela.
Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Lingathembi ukuqilibezela kumbe lizikhukhumeze ngempahla zokwebiwa; kungaze kube inotho yenu iyanda, lingabeki inhliziyo zenu kuyo.
Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
11 Yinye into uNkulunkulu ayikhulumileyo, zimbili izinto engizizwileyo, ukuthi amandla wonke ngawakho wena, Oh Nkulunkulu.
Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12 Lokuthi wena, Thixo, ulothando olojulileyo, umuntu ngamunye uzamupha umvuzo ngalokho akwenzileyo.
komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.