< Amahubo 54 >

1 Kumqondisi wokuhlabela. Kutshaywa iziginci. Ihubo likaDavida. Lapho amaZifi aya kuSawuli afika athi, “Kanti uDavida kacatshanga yini phakathi kwethu?” Ngisindisa, awu Nkulunkulu, ngebizo lakho; ngigeza ecaleni ngamandla akho.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Zwana umkhuleko wami, Oh Nkulunkulu; lalela amazwi omlomo wami.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Ngihlaselwa ngabantu engingabaziyo; izikliwi zifuna impilo yami abantu abangamnanzanga uNkulunkulu.
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Ngeqiniso uNkulunkulu ulusizo lwami; uThixo nguye ongisizayo.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Akuthi ububi bubuyele phezu kwalabo abangigconayo; ngokuthembeka kwakho babhubhise.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Ngizakwenzela umhlatshelo owomnikelo wokuzithandela; ngizalidumisa ibizo lakho, Thixo, ngoba lihle.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 Ngoba ingikhulule kuzozonke inhlupheko zami, lamehlo ami akubonile ukunqotshwa kwezitha zami.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Amahubo 54 >