< Amahubo 32 >

1 Ihubo likaDavida. Ubusisiwe lowo oziphambeko zakhe zithethelelwe, ozono zakhe zisibekelwe.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Ubusisiwe lowo ongasoze abalelwe isono sakhe nguThixo, njalo ongelankohliso emoyeni wakhe.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Ngathi lapho ngithule, amathambo ami ababuthakathaka ngenxa yokububula kwami ilanga lonke.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Ngoba imini lobusuku isandla Sakho sasingelekile, singisinda; amandla ami aphela kwafana lesikhudumezi sehlobo.
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Lapho-ke ngasengisivuma isono sami Kuwe angabe ngisasibekela ububi bami. Ngathi, “Ngizazivuma iziphambeko zami kuThixo,” walithethelela icala lesono sami.
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Ngakho akuthi wonke umuntu othembekileyo akhuleke kuwe usatholakala; ngeqiniso kuzakuthi lapho impophoma seziqubuka, kabayi kumfinyelela.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Uyindawo yami yokuphephela; uzangivikela enkathazweni ungizungeze ngezingoma zensindiso.
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Ngizakutshengisa ngikufundise indlela ofanele uhambe ngayo; ngizakweluleka ngikulinde.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Ungabi njengebhiza loba imbongolo, khona akulakuzwisisa kodwa kumele kukhokhelwa ngamatomu ukuze umuntu kumlalele.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Zinengi izikhalazo zababi, kodwa uthando lukaThixo olungaphuthiyo luyamzungeza umuntu othemba kuye.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Thokozani kuThixo, lithabe lina balungileyo; hlabelelani lonke lina eliqotho enhliziyweni!
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Amahubo 32 >