< Izaga 4 >

1 Zwanini, madodana ami, izeluleko zikayihlo; lalelani lizuze ukuqedisisa.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Ngilipha izifundo ezipheleleyo; ngakho lingalahli imfundiso yami.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Ngathi ngisengumfana emzini kababa, ngisebuthakathaka, ngiyimi ngedwa ingane kamama,
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 wangifundisa ubaba wathi, “Abambe amazwi ami ngenhliziyo yakho yonke; gcina imilayo yami ukuze uphile.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Zuza ukuhlakanipha, zuza ukuqedisisa; ungawakhohlwa amazwi ami, kumbe ugudluke kuwo.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ungafulatheli ukuhlakanipha, kuzakuvikela; kuthande, kuzakulinda.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Ukuhlakanipha kuyinqaba; ngakho zuza ukuhlakanipha. Zuza ukuqedisisa loba kungathatha konke olakho.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Kugogose, kuzakuphakamisa; kugone, kuzakunika udumo.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Kuzakwethesa umqhele wamaluba omusa ekhanda lakho kukwethese umqhele wenkazimulo.”
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Zwana mntanami, yamukela lokho engikutshoyo, ukuze insuku zokuphila kwakho zibe zinengi.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ngiyakukhokhela endleleni yokuhlakanipha, ngikuqondise ezindleleni eziqondileyo.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Nxa uhamba kawuyikuthikaza; nxa ugijima kawuyikukhubeka.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Bambelela iziqondiso, ungayekethisi; zigcine kuhle ngoba ziyikuphila kwakho.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Ungayingeni indlela yababi njalo ungahambi endleleni yezigangi.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Ixwaye, ungahambi ngayo; itshiye uqhubeke ngeyakho indlela.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Phela kabalali bengenzanga ukuganga; badela ubuthongo ukuze baqale balimaze omunye umuntu.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Badla isinkwa sobubi banathe iwayini lobudlwangudlwangu.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Indlela yabalungileyo injengovivi lokusa, kukhule ukukhanya kwalo kuze kuphelele emini.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Kodwa indlela yababi ifana lomnyama omkhulu; kabazi ukuthi kuyini okubakhubayo.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Ndodana yami, zwana lokhu engikutshoyo; lalelisisa amazwi ami.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Ungawasusi emehlweni akho, agcine enhliziyweni yakho;
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 ngoba ayikuphila kulabo abawafumanayo; lokuqina komzimba wonke womuntu.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Phezu kwakho konke, gcina inhliziyo yakho, ngoba ingumthombo wokuphila kwakho.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Lahla izibozi zamazwi emlonyeni wakho; ungakhuphi inkulumo yokuxhwala ezindebeni zakho.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Khangelisa amehlo akho nta phambili, uwathi nhlo amehlo akho kulokho okuphambi kwakho.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Lungisa izindlela ukuze inyawo zakho zinyathele kuhle, uhambe ngezindlela eziqinileyo kuphela.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Ungaphambukeli kwesokunene loba kwesokhohlo; ugcine unyawo lwakho lunganyatheli okubi.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Izaga 4 >