< Izaga 11 >

1 UThixo uyazenyanya izilinganiso zokudlelezela, kodwa uthokoza ngezilinganiso eziqondileyo.
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 Nxa kungena ukuzigqaja kungena lokweyisa, kodwa ukuzithoba kuhamba lenhlakanipho.
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 Ubuqotho kwabaqondileyo buyabakhokhela, kodwa abangathembekanga babulawa yibumenemene babo.
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 Inotho kayisizi lutho ngosuku lweziphithiphithi kodwa ukulunga kuyaphephisa ekufeni.
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 Ukulunga kwabangelacala kuqondisa indlela yabo, kodwa ababi bawiswa yibubi babo.
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 Ukulunga kwabaqondileyo kuyabakhulula, kodwa abangathembekanga bagwenxwa yizinkanuko zabo ezimbi.
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 Umuntu omubi angafa ithemba lakhe liyaphela; konke abesithi uzakuzuza ngamandla akhe kuphelela ezeni.
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 Umuntu olungileyo uyakhululwa enkathazweni, kusuke kuyewela komubi.
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 Ngomlomo wakhe umuntu ongakholwayo uyamchitha umakhelwane, kodwa ngolwazi abalungileyo bayaphepha.
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 Nxa kuphumelela abalungileyo umuzi uyathokoza; nxa kusifa omubi kuba lokujabula.
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 Ngokubusiswa ngabalungileyo omubi ubalodumo, kodwa ngomlomo wezigangi uyachitheka.
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 Umuntu ongelangqondo weyisa umakhelwane wakhe, kodwa umuntu ozwisisayo uthiba ulimi lwakhe.
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 Onyeyayo wehluleka ukuvala isifuba sakhe, kodwa othembekileyo uyayigcina imfihlo.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 Isizwe esingelabukhokheli obuqondileyo siyachitheka, kodwa ngobunengi babeluleki siyanqoba.
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 Lowo okhuphela omunye umuntu isibambiso uzahlupheka, kodwa owalayo ukupha isibambiso uvikelekile.
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 Umfazi olomusa uyahlonitshwa, kodwa amadoda alesihluku azuza inotho kuphela.
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 Umuntu olomusa uyazisiza, kodwa umuntu ololunya uyazilimaza.
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 Umuntu omubi uhola umvuzo wobuqili, kodwa lowo ohlanyela ukulunga uvuna umvuzo omuhle.
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 Lowo omiyo ekulungeni uzuza ukuphila, kodwa oxotshana lobubi uya ekufeni.
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 UThixo uyabazonda abantu abalenhliziyo embi, kodwa uyathokoza ngalabo abandlela zabo zilungile.
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 Kodwa yazi lokhu, ababi bazajeziswa kodwa abalungileyo bazahlala bekhululekile.
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 Njengesongo legolide lifakwe emakhaleni engulube, unjalo umfazi omuhle kodwa ongelambeko.
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 Izifiso zabalungileyo zizuza okuhle kodwa ithemba lababi liphelela osizini.
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 Ophayo ngesihle uyazuza okunengi kulakuqala, lowo ogodlayo ungenelwa yibuyanga.
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 Lowo ophayo uzaphumelela; owonga abanye laye uzakongiwa.
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 Abantu bayamqalekisa lowo ogodla amabele, kodwa izibusiso zingumqhele walowo ovuma ukuwathengisa.
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 Lowo odinga ukulunga uzuza umusa, kodwa okubi kwehlela lowo okudingayo.
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 Othembele enothweni yakhe uzakuwa; kodwa olungileyo uzaphila njengehlamvu eliluhlaza.
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 Olethela abendlu yakhe uhlupho ilifa lakhe yize, lesihawu sizakuba yinceku yohlakaniphileyo.
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 Izithelo zolungileyo ziyisihlahla sokuphila, njalo lowo ozuza imiphefumulo uhlakaniphile.
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 Nxa abalungileyo bezuza ukujeziswa emhlabeni pho kuzakuba njani kwabangakholwayo labayizoni!
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

< Izaga 11 >