< Amanani 32 >

1 AbakoRubheni labakoGadi ababelemihlambi emikhulu yenkomo leyezimvu babona ukuthi amadlelo emangweni weJazeri leGiliyadi ayemahle ezifuyweni.
Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
2 Ngakho baya kuMosi laku-Eliyazari umphristi lakubakhokheli babantu, bathi,
Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
3 “Umhlaba we-Atharothi, leDibhoni, leJazeri, leNimra, leHeshibhoni, le-Eliyale, leSebhami, leNebho kanye leBheyoni,
“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
4 uThixo awunqoba phambi kwabako-Israyeli, ngumhlaba olungele izifuyo, njalo thina nceku zenu silezifuyo.”
dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
5 Basebesithi, “Nxa sifumene umusa emehlweni enu, lelilizwe aliphiwe izinceku zenu libe yisabelo sethu. Lingenzi ukuba sichaphe uJodani.”
Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
6 UMosi wabuza abakoGadi labakoRubheni wathi, “Kambe lingahlala lapha amanye amadoda akini esiya empini na?
Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
7 Kungani lithelela abako-Israyeli ukwesaba ukuchaphela elizweni abaliphiwa nguThixo na?
Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
8 Yikho lokhu okwenziwa ngoyihlo ekubathumeni kwami besuka eKhadeshi Bhaneya ukuyahlola ilizwe.
Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
9 Bathi sebehambe baze bayafika eSigodini sase-Eshikholi balibona ilizwe, bathelela abako-Israyeli ukwesaba ukungena elizweni abaliphiwa nguThixo.
Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
10 Ulaka lukaThixo lwaqubuka ngalolosuku waze wenza lesisifungo.
Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
11 ‘Ngenxa yokuthi abangilandelanga ngezinhliziyo zabo ezipheleleyo, kakho loyedwa emadodeni wonke aleminyaka engamatshumi amabili kusiya phezulu okuzalwa kwabavela eGibhithe ozabona ilizwe engalithembisa u-Abhrahama, u-Isaka loJakhobe ngesifungo,
‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
12 kakho loyedwa ngaphandle kukaKhalebi indodana kaJefune umKhenizi kanye loJoshuwa indodana kaNuni, ngoba laba balandela uThixo ngezinhliziyo ezipheleleyo.’
Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
13 Ulaka lukaThixo lwavutha wabazondela abako-Israyeli njalo wabenza bantula enkangala okweminyaka engamatshumi amane, kwaze kwaphela bonke abentanga yalabo ababonile phambi kukaThixo.
Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 Khathesi nanku-ke lina, nzalo yezoni, selimi endaweni yaboyihlo libangela ukuthi uThixo athukuthelele abako-Israyeli ngamandla.
“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
15 Nxa lingala ukumlandela, uThixo uzaphinde atshiye bonke lababantu bakhe enkangala, njalo kuzabe kuyini elibangele incithakalo yabo.”
Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 Ngakho beza kuye bathi, “Sifuna ukwakha izibaya zezifuyo zethu njalo sakhele omkethu labantwabethu amadolobho.
Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
17 Kodwa thina sesilungele ukuzihlomisa ukuze sikhokhele abako-Israyeli size siyebafikisa endaweni yabo. Kunjalo-nje omkethu labantwabethu bazasala emadolobheni avikelekileyo, ukuze bangahlaselwa ngabanikazi balelolizwe.
Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
18 Kasiyikubuyela kweyethu imizi wonke owako-Israyeli aze azuze isabelo sakhe.
Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
19 Thina kasiyikuzuza isabelo kanye labo ngale kweJodani, ngoba esethu isabelo sisithole ngapha ngempumalanga kweJodani.”
Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 Ngakho uMosi wathi kubo, “Nxa lizakwenza lokhu, lizihlomisele ukuhlasela phambi kukaThixo,
Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
21 njalo nxa lonke lizahamba lihlomile ngale kweJodani phambi kukaThixo aze adudule izitha phambi kwakhe,
ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
22 kuthi nxa ilizwe selinqotshiwe phambi kukaThixo selingaphenduka njalo liyabe selikhululekile emlandwini wenu kuThixo laku-Israyeli. Ngalokho-ke lelilizwe lizakuba yisabelo senu phambi kukaThixo.
dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 Kodwa lingehluleka ukwenza lokhu, lizabe lonile phambi kukaThixo; njalo yazini ukuthi isono senu sizalifumana.
“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
24 Yakhelani abesifazane benu labantwabenu amadolobho, njalo lakhele izifuyo zenu izibaya, kodwa yenzani lokho elikuthembisileyo.”
Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 AbakoGadi labakoRubheni bathi kuMosi, “Thina izinceku zakho sizakwenza njengokulaya kwenkosi yethu.
Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
26 Abantwabethu labomkethu, imihlambi yezimvu zethu leyenkomo zethu kuzasala lapha emadolobheni aseGiliyadi.
Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
27 Kodwa thina zinceku zakho, yonke indoda ehlomele ukuhlasela, izachapha iyekulwa phambi kukaThixo, njengokutsho kwenkosi yethu.”
koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 UMosi wasekhupha ilizwi lesiqondiso ngabo ku-Eliyazari umphristi lakuJoshuwa indodana kaNuni kanye lakulabo abazinhloko zezimuli zezizwana zako-Israyeli.
Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
29 Wathi kubo, “Nxa abakoGadi labakoRubheni, wonke amadoda ayabe ehlomele ukuhlasela, angachaphela ngale kweJodani kunye lani phambi kukaThixo, kube sekusithi nxa ilizwe selinqotshiwe phambi kwenu banikeni ilizwe laseGiliyadi libe yisabelo sabo.
Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
30 Kodwa nxa bengachaphanga lani behlomile, kumele bemukele isabelo sabo kunye lani eKhenani.”
Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 AbakoGadi labakoRubheni baphendula bathi, “Izinceku zakho zizakwenza okutshiwo nguThixo.
Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
32 Sizachaphela ngale phambi kukaThixo singene eKhenani sihlomile, kodwa ilifa eliyisabelo sethu lizakuba nganeno kweJodani.”
Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 Ngakho uMosi wasenika abakoGadi, labakoRubheni kanye lengxenye yesizwana sakoManase indodana kaJosefa umbuso kaSihoni inkosi yama-Amori kanye lombuso ka-Ogi inkosi yaseBhashani, ilizwe lonke kanye lamadolobho alo kanye lamazwe ayebagqagqele.
Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 AbakoGadi bakha iDibhoni, i-Atharothi, i-Aroweri,
Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
35 i-Athirothi-Shofani, iJazeri, iJogibheha,
Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
36 iBhethi-Nimra kanye leBhethi-Harani aba ngamadolobho ahonqolozelwe ngemithangala, njalo bakha lezibaya zemihlambi yezifuyo zabo.
Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
37 Kanti-ke abakoRubheni bakha kakutsha iHeshibhoni, i-Eliyale kanye leKhiriyathayimi,
Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
38 kanye lokwakha iNebho kanye leBhali-Meyoni (la amabizo aguqulwa) leSibhima. Betha amadolobho abawakha kutsha amabizo.
Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 Izizukulwane zikaMakhiri indodana kaManase zaya eGiliyadi, zalithumba njalo zaxotsha ama-Amori ayekulelolizwe.
Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
40 Ngakho uMosi wapha elaseGiliyadi kumaMakhiri, izizukulwane zikaManase, basebehlala khona.
Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
41 UJayiri, umzukulu kaManase, wathumba imizi yabo wayibiza ngokuthi yiHarothi Jayiri.
Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
42 Kanti uNobha wathumba iKhenathi kanye lemizi eyigqagqeleyo njalo wayetha ibizo lakhe wathi yiNobha.
Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.

< Amanani 32 >