< Izililo 5 >
1 Oh Thixo, khumbula okusehleleyo khangela ubone ukuyangeka kwethu.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Ilifa lethu seliphiwe abezizweni, imizi yethu yathathwa ngabemzini.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Sesizintandane ezingelaboyise, omama sebenjengabafelokazi.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Amanzi okunatha siyawathenga; inkuni zethu zikhutshelwa imali.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Labo abasixotshayo basihlezi ezithende; sikhathele asilakuphumula.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Sazinikela kwabeGibhithe labe-Asiriya ukuze sizuze isinkwa.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Okhokho benza isono kodwa kabasekho, thina yithi esesijeziswa.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Sibuswa yizigqili, kakho osikhululayo ezandleni zazo.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Isinkwa sisithola ngendlela eyingozi ngenxa yenkemba ekhona enkangala.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Isikhumba sethu sitshisa njengeziko, silomkhuhlane wendlala.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Abesifazane bayahlukuluzwa eZiyoni kanye lezintombi ezigcweleyo emadolobheni akoJuda.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Amakhosi alengisiwe ngezandla zawo; abadala abasahlonitshwa.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Izinsizwa ziyahoqiswa ematsheni okuchola; abafana babhensiswa yimithwalo yenkuni.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Abadala sebesukile esangweni lomuzi; izinsizwa sezithule ukuhlabelela.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Ukuthokoza akusekho ezinhliziyweni zethu; ukugida kwethu sekuphenduke ukukhala.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Umqhele usuwile ekhanda lethu. Maye thina, ngoba sonile!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Ngenxa yalokhu inhliziyo zethu zibuthakathaka; ngenxa yalezizinto amehlo ethu ayafiphala,
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 ngoba intaba iZiyoni silugwadule, sekucathama amakhanka kuyo.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Wena, Oh Thixo, busa nini lanini; ubukhosi bakho buhlezi kuzozonke izizukulwane.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Kungani uhlezi usikhohlwa? Usifulathelelani isikhathi eside kangaka na?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Sibuyisele kuwe, Oh Thixo, ukuze siphenduke; buyisa kabutsha insuku zethu njengezakudala,
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 ngaphandle kokuba nxa ususilahle kokuphela wasizondela ngokungalinganisekiyo.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.