< Abahluleli 3 >

1 Nanzi izizwe ezatshiywa nguThixo ukuze abahlole bonke abako-Israyeli ababengazibonanga izimpi eKhenani
Iyi ndi mitundu ya anthu yomwe Yehova anayisiya kuti ayese nayo Aisraeli amene sanadziwe kumenya nkhondo mu Kanaani
2 (wenza lokhu ukuba azifundise izizukulwane zako-Israyeli ukulwiwa kwezimpi lezo ezazingazange zikubone ukulwa ngaphambilini):
(Yehova anachita izi kuti Aisraeli onse aphunzire kumenya nkhondo; makamaka amene nʼkale lonse sanadziwe kumenya nkhondo.
3 ababusi abahlanu bamaFilistiya, amaKhenani wonke, amaSidoni, lamaHivi ahlala ezintabeni zaseLebhanoni kusukela eNtabeni iBhali-Hemoni kusiya eLebho Hamathi.
Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
4 Babetshiyelwe ukuhlola abako-Israyeli ukuba kubonakale ukuthi bayayilalela na imilayo kaThixo, ayeyinike okhokho babo ngoMosi.
Iwowa Yehova anawasiya kuti aziyesa nawo Aisraeli kuti aone ngati angamvere malamulo a Yehova, amene anapatsa makolo awo kudzera mwa Mose.
5 Abako-Israyeli babehlala phakathi kwamaKhenani, lamaHithi, lama-Amori, lamaPherizi, lamaHivi kanye lamaJebusi.
Choncho Aisraeli anakhala pakati pa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
6 Bathatha amadodakazi awo aba ngomkabo njalo bendisela amadodakazi abo emadodaneni awo, bakhonza labonkulunkulu bawo.
Tsono Aisraeli aja amalola ana awo aamuna ndi aakazi kuti azikwatira ndi kukwatiwa ndi anthu amitundu ina. Kenaka anayamba kupembedza milungu yawo.
7 Abako-Israyeli benza okubi emehlweni kaThixo; bamkhohlwa uThixo uNkulunkulu wabo bakhonza oBhali labo-Ashera.
Aisraeli anachita zinthu zoyipira Yehova. Iwowa anayiwala Yehova Mulungu wawo ndi kumatumikira Abaala ndi Asera.
8 Ulaka lukaThixo lwavuthela abako-Israyeli waze wabanikela ezandleni zikaKhushani-Rishathayimi inkosi yase-Aramu Naharayimu, lapho abantu bako-Israyeli ababangaphansi kombuso wayo iminyaka eyisificaminwembili.
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeliwo ndipo anawagulitsa kwa Kusani-Risataimu mfumu ya ku Mesopotamiya. Choncho Aisraeli anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zisanu ndi zitatu.
9 Kodwa ekukhaleni kwabo kuThixo, wabalethela umhlengi, u-Othiniyeli indodana kaKhenazi, umnawakhe kaKhalebi, owabakhululayo.
Koma pamene Aisraeliwo analirira kwa Yehova, Iye anawawutsira mpulumutsi, Otanieli mwana wamwamuna wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe. Iyeyu ndiye anawapulumutsa.
10 Umoya kaThixo wehlela kuye, wasesiba ngumahluleli wako-Israyeli waya empini. UThixo wanikela uKhushani-Rishathayimi inkosi ye-Aramu ezandleni zika-Othiniyeli, wamnqoba.
Mzimu wa Yehova unatsika pa iye, choncho anasanduka mtsogoleri wa Israeli. Iye anapita kukamenya nkhondo, ndipo Yehova anapereka Kusani-Risataimu mfumu ya Aaramu mʼmanja mwake. Choncho anayigonjetsa.
11 Ngakho ilizwe laba lokuthula iminyaka engamatshumi amane, u-Othiniyeli indodana kaKhenazi waze wafa.
Ndipo mʼdzikomo munakhala mtendere zaka makumi anayi. Kenaka Otanieli mwana wa Kenazi anamwalira.
12 Abako-Israyeli baphinda benza okubi emehlweni kaThixo, kwathi ngenxa yokuthi babenze lobububi uThixo wanika u-Egiloni inkosi yaseMowabi amandla phezu kuka-Israyeli.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Tsono Yehova anapatsa mphamvu Egiloni, mfumu ya Mowabu kuti alimbane ndi Aisraeli aja popeza anachita zinthu zoyipira Yehova.
13 Esenze ama-Amoni lama-Amaleki amanyana laye, u-Egiloni wayahlasela u-Israyeli, basebethumba idolobho laMalala.
Egiloniyo anamemeza Aamori ndi Aamaleki kupita kukamenyana ndi Israeli, ndipo analanda Yeriko, mzinda wa migwalangwa.
14 Abako-Israyeli babangaphansi kombuso ka-Egiloni inkosi yaseMowabi iminyaka elitshumi layisificaminwembili.
Aisraeli anatumikira ngati akapolo Egiloni mfumu ya Mowabu kwa zaka 18.
15 Abako-Israyeli bakhala futhi kuThixo, wasebapha umhlengi u-Ehudi, indoda eyayilinxele indodana kaGera owakoBhenjamini. Abako-Israyeli bamthuma lesipho ku-Egiloni inkosi yaseMowabi.
Aisraeli analiranso kwa Yehova, ndipo Iye anawawutsira mpulumutsi, Ehudi. Iyeyu anali mwana wa Gera, munthu wamanzere, wa fuko la Benjamini. Aisraeli ankatumiza msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, kudzera kwa Ehudi.
16 U-Ehudi wayenze inkemba esika inxa zombili eyayingaba yingalo lengxenye ubude bayo, ayibophela ethangazini lakhe lwesokudla ngaphansi kwezigqoko zakhe.
Ndipo Ehudi anapanga lupanga lakuthwa kuwiri lotalika masentimita makumi asanu, ndipo anamangirira lupangalo pa ntchafu yake ya kumanja mʼkati mwa zovala zake.
17 Wasethula isipho ku-Egiloni inkosi yaseMowabi, owayengumuntu oqatha kakhulu.
Iye anakapereka msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, amene anali munthu wonenepa kwambiri.
18 Emva kokuba u-Ehudi esesethule isipho, walaya abantu ababesithwele ukuba bazihambele.
Ehudi atapereka msonkhowo, anawuza anthu amene ananyamula msonkhowo kuti azipita.
19 Ezithombeni eduze leGiligali yena uqobo wabuyela emuva, wathi, “Oh nkosi, ngilelizwi lakho eliyimfihlo.” Inkosi yathi, “Thula!” Zonke izikhonzi zayo zasuka kuyo.
Iye mwini anabwerera pamalo a miyala yozokotedwa ku Giligala ndipo anati, “Zikomo mfumu, ine ndili ndi mawu achinsinsi kuti ndikuwuzeni.” Mfumuyo inawuza onse amene amayitumikira kuti akhale chete, ndipo kenaka anawatulutsa.
20 U-Ehudi wayilanda isihlezi yodwa ekamelweni langaphezulu elipholileyo endlini yayo yobukhosi wathi, “Ngilelizwi lakho elivela kuNkulunkulu.” Kwathi inkosi isukuma esihlalweni sayo,
Kenaka Ehudi anayandikira pafupi ndi mfumuyo, ndipo iyo inakhala yokha mʼchipinda chapamwamba, mozizira bwino. Tsono Ehudi anati, “Ndili ndi mawu ochokera kwa Mulungu woti ndikuwuzeni.” Mfumuyo itadzuka pa mpando wake waufumu,
21 u-Ehudi wafinyelela ngesandla sakhe senxele, wahwatsha inkemba ethangazini lakhe kwesokudla wayithela esiswini senkosi.
Ehudi ndi dzanja lake lamanzere, anasolola lupanga pa ntchafu yake ya kumanja ndi kubaya nalo mfumuyo pa mimba.
22 Inkemba yatshona yasala ngesilanda, amathumbu akhe agcwala phansi. U-Ehudi kayingcothulanga inkemba, idanga layemboza.
Lupanga linalowa mʼmimba pamodzi ndi chogwirira chake. Mafuta anaphimba lupangalo popeza silinatulutsidwe mʼmimbamo. Ndiponso matumbo anatuluka.
23 U-Ehudi waphuma phandle, wavala iminyango yekamelo langaphezulu wayihluthulela.
Kenaka Ehudi anatuluka panja pa khonde, atatseka ndi kukhoma zitseko za chipinda chapamwambacho.
24 Esehambile kweza izinceku zathola iminyango yekamelo langaphezulu ihluthulelwe. Zathi, “Kutsho ukuthi iye ngaphandle ekamelweni elingaphakathi kwendlu.”
Ehudi atachoka, atumiki a mfumu aja anabwera, ndipo ataona kuti zitseko za chipinda chapamwamba zinali zokhoma anaganiza kuti mwina mfumu ikudzithandiza mʼkatimo.
25 Zalinda zaze zakhathazeka, kodwa ngoba ingasavulanga iminyango yekamelo lelo, zathatha ikhiye zayivula. Lapho-ke zabona inkosi yazo iwele phansi, isifile.
Iwo anadikira nthawi yayitali koma popanda chochitika. Koma ataona kuti mfumuyo sikutsekulabe zitseko za chipindacho, iwo anatenga makiyi ndi kutsekula zitsekozo, ndipo anangoona mbuye wawo atagwera pansi, ali wakufa.
26 Zisalindile, u-Ehudi wasuka wahamba. Wedlula eduzane lezithombe wabalekela eSeyira.
Ehudi anathawa pamene iwo ankadikira. Iye anadzera ku malo a miyala yozokotedwa kuja ndi kuthawa kupita ku Seiri.
27 Esefike lapho wakhalisa icilongo elizweni lezintaba lako-Efrayimi, abako-Israyeli basebesehla laye ezintabeni, yena ebakhokhele.
Atafika kumeneko, anayimba lipenga ku dziko la ku mapiri la Efereimu. Iye akutsogolera, Aisraeli onse anatsika naye pamodzi kuchoka ku mapiriko.
28 Wabalaya wathi, “Ngilandelani, ngoba uThixo usenikele uMowabi, isitha senu, ezandleni zenu.” Ngakho behlela laye phansi bemlandela, kwathi sebethumbe amazibuko eJodani ayewelela eMowabi, kabaze bavumela muntu ukuba achaphele ngaphetsheya.
Iye anawawuza kuti, “Nditsatireni, chifukwa Yehova wapereka Amowabu, adani anu mʼmanja mwanu.” Choncho anthuwo anamutsatira, nalanda madooko a Yorodani opita ku Mowabu. Iwo sanalole kuti wina aliyense awoloke.
29 Ngalesosikhathi babulala amaMowabi ayengaba zinkulungwane ezilitshumi, wonke ayeqinile elamandla; akukho muntu owaphunyukayo.
Nthawi imeneyo anapha Amowabu pafupifupi 10,000. Ophedwawo anali anthu amphamvu komanso odziwa kumenya nkhondo, ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anathawa.
30 Ngalolosuku iMowabi yanqotshwa yi-Israyeli, ilizwe laselisiba lokuthula iminyaka engamatshumi ayisificaminwembili.
Tsiku limenelo Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Israeli, ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 80.
31 Emva kuka-Ehudi kwaba loShamigari indodana ka-Anathi owabulala amaFilistiya angamakhulu ayisithupha ngesijujo senkabi. Laye wamkhulula u-Israyeli.
Ehudi atamwalira, panabwera Samugara mwana wa Anati. Iye anapha Afilisti 600 ndi ndodo yomenyera ngʼombe. Nayenso anapulumutsa Israeli.

< Abahluleli 3 >