< UJuda 1 >

1 UJuda, inceku kaJesu Khristu lomfowabo kaJakhobe, Kulabo ababiziweyo, abathandwa nguNkulunkulu uBaba belondolozwa nguJesu Khristu:
Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo. Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.
2 Isihawu, lokuthula kanye lothando kakube ngokwenu ngokwandileyo.
Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.
3 Bangane abathandekayo, lanxa kade ngitshisekela kakhulu ukulilobela mayelana lensindiso esilayo, kodwa ngibone kufanele ukuthi ngilobele ukulikhuthaza ukuba lilwele ukholo lolu olwaphiwa abangcwele bakaNkulunkulu
Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima.
4 Ngoba abantu abathile abokulahlwa kwabo okwalotshwa ngakho endulo sebengene phakathi kwenu ngasese. Bangabantu abangamesabiyo uNkulunkulu abaguqulela umusa kaNkulunkulu ukuthi ubeyimvumo yokuganga bamphike loJesu Khristu onguye kuphela iNkosi yethu Yobukhosi.
Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.
5 Lanxa likwazi konke lokhu, ngithanda ukulikhumbuza ukuthi iNkosi yakhupha abantu bayo eGibhithe, kodwa muva yababhubhisa labo abangakholwanga.
Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire.
6 Lezingilosi ezingagcinanga izikhundla zazo zamandla, kodwa zadela ikhaya lazo, lezi wazigcina ebumnyameni, zibotshwe ngamaketane angaqamukiyo zilindele ukwahlulelwa ngoSuku olukhulu. (aïdios g126)
Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios g126)
7 Ngokunjalo, iSodoma leGomora lamadolobho aseduzane azinikela ekuxhwaleni kobufebe lokonakala. Ayisibonelo salabo abezwa isijeziso somlilo waphakade. (aiōnios g166)
Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios g166)
8 Ngokunjalo, ngamandla okuphupha kwabo lababantu abangalunganga bangcolisa imizimba yabo, baphike ubukhokheli, bachothoze lezidalwa zasezulwini.
Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba.
9 Kodwa lengilosi enkulu uMikhayeli lapho ephikisana loSathane ngesidumbu sikaMosi kazange alokothe ukumthuka ngenhlamba, kodwa wathi, “INkosi kayikukhuze!”
Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!”
10 Kodwa abantu laba bakhuluma behlambaza lokho abangakuzwisisiyo; njalo lezozinto abazizwisisayo ngokwemvelo njengezinyamazana ezingacabangiyo, lezi yizo kanye izinto ezizababhubhisa.
Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.
11 Maye kubo! Balandela indlela kaKhayini; baphuthuma inzuzo besona njengoBhalamu; babhujiswa emvukeleni kaKhora.
Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.
12 Abantu laba bayisinengiso emadilini enu abantu abathetheneyo besidla lani bengelanhloni lakancane, abelusi abazitika ngokudla bona bodwa. Bangamayezi angelazulu, aphetshulwa ngumoya; izihlahla zasekwindla ezingelazithelo njalo ezisitshuniweyo, ezife kabili.
Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu.
13 Bangamagagasi olwandle alamandla, bebhubhudla ihlazo labo; izinkanyezi ezintulayo, ezilobumnyama obukhulu obugcinelwe zona kuze kube nininini. (aiōn g165)
Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn g165)
14 U-Enoki, owesikhombisa kusukela ku-Adamu waphrofitha ngabantu laba wathi: “Khangelani, iNkosi iza lezinkulungwane lezinye izinkulungwane zabangcwele bayo
Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka
15 ukwahlulela abantu bonke, lokubalahla ngenxa yamacala abawenzayo ebubini babo, langenxa yamazwi wonke okudelela, izoni ezingamesabiyo uNkulunkulu ezawakhuluma ngaye.”
kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.”
16 Abantu laba bangabakhononi labachothozi; balandela izinkanuko zabo ezimbi; bayazikhukhumeza, bancome abanye ngamanga ukuze bazitholele inzuzo.
Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.
17 Kodwa-ke, bangane abathandekayo, khumbulani okwatshiwo ngaphambilini ngabapostoli beNkosi yethu uJesu Khristu.
Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu.
18 Bathi kini, “Ngezikhathi zokucina kuzakuba labaklolodayo, belandela izinkanuko zabo zokungalungi.”
Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.”
19 Laba yibo abantu abalehlukanisayo, abalandela isazela semvelo nje bengelawo uMoya.
Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.
20 Kodwa lina, bangane abathandekayo, zakheni ekukholweni kwenu okungcwele kakhulu likhuleke kuMoya oNgcwele,
Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera.
21 lizigcine lisothandweni lukaNkulunkulu lisalindele isihawu seNkosi yethu uJesu Khristu ukuba ilingenise ekuphileni okulaphakade. (aiōnios g166)
Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios g166)
22 Yibani lesihawu kulabo abathandabuzayo;
Muwachitire chifundo amene akukayika.
23 lenyule abanye emlilweni libasilise; kwabanye bonakalisani isihawu, kuhlangene lokwesaba, lizonde lezigqoko ezingcoliswe yimizimba exhwalileyo.
Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.
24 Kuye olamandla okuligcina ukuba lingawi, lokulibeka phambi kwenkazimulo yobukhona bakhe kungelasici njalo ngentokozo enkulu,
Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa,
25 kuye yedwa uNkulunkulu onguMsindisi wethu, kakube lodumo, ubukhosi kanye lamandla ngoJesu Khristu iNkosi yethu, mandulo kwezikhathi zonke, khathesi kanye lanininini! Ameni. (aiōn g165)
kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)

< UJuda 1 >