< UJoshuwa 10 >
1 U-Adoni-Zedekhi inkosi yaseJerusalema wezwa ukuthi uJoshuwa wayesethumbe i-Ayi wayitshabalalisa, njengalokho akwenza eJerikho lenkosini yayo, lokuthi abantu baseGibhiyoni babenze isivumelwano sokuthula labako-Israyeli njalo sebehlala labo.
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 Yena labantu bakhe besaba kakhulu ngalokhu, ngenxa yokuthi iGibhiyoni kwakulidolobho eliqakatheke kakhulu, njengelinye lamadolobho esikhosini; lalilikhulu kule-Ayi, njalo amadoda alo wonke ayezingwazi ezilamandla.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 Ngakho u-Adoni-Zedekhi inkosi yaseJerusalema wakhalaza kuHohamu inkosi yaseHebhroni, kuPhiramu inkosi yaseJamuthi, kuJafiya inkosi yaseLakhishi lakuDebhiri inkosi yase-Egiloni.
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Wathi kubo, “Wozani lizongincedisa ukuhlasela iGibhiyoni ngenxa yokuthi yenze isivumelwano sokuthula loJoshuwa labako-Israyeli.”
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 Ngakho amakhosi womahlanu ama-Amori, aseJerusalema, eHebhroni, eJamuthi, eLakhishi lase-Egiloni abambana. Aphuma lamabutho awo wonke ayihonqolozela iGibhiyoni ayihlasela.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 AmaGibhiyoni athumela ilizwi kuJoshuwa ezihonqweni zaseGiligali athi: “Ungalahli izinceku zakho. Woza ngapha kithi ngokuphangisa uzosisiza! Sincede, ngoba wonke amakhosi ama-Amori abusa emazweni asemaqaqeni asebambene ukuze alwisane lathi.”
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 Ngakho uJoshuwa wasuka eGiligali, wenyuka kanye lebutho lakhe lonke, elaligoqela wonke amadoda ayekwazi ukulwa.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 UThixo wathi kuJoshuwa, “Ungabesabi; sengibanikele esandleni sakho. Kakho loyedwa ozakwenelisa ukumelana lawe.”
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 Ngemva kokuhamba okobusuku bonke besuka eGiligali, uJoshuwa wabajuma.
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 UThixo wenza ukuthi basanganiseke phambi kuka-Israyeli, wabehlula ngokunqoba okukhulu eGibhiyoni. Abako-Israyeli baxotshana labo emgwaqweni oya eBhethi-Horoni, baxhumana labo baze bayafika e-Azekha leMakheda.
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 Lapho bebalekela abako-Israyeli emgwaqweni osuka eBhethi-Horoni usiya e-Azekha, uThixo wehlisa isiqhotho esikhulu sivela emkhathini, njalo inengi labo lafa libulawa yisiqhotho ukwedlula ababulawa zinkemba zabako-Israyeli.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 Ngalelolanga uThixo wanikela ngalo ama-Amori kwabako-Israyeli, uJoshuwa wathi kuThixo phambi kwabako-Israyeli: “We langa, mana uthi mpo ngaphezu kweGibhiyoni, lawe nyanga, mana ngaphezu kweSigodi se-Ayijaloni.”
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 Ngakho ilanga lema lathi mpo, lenyanga yema, isizwe saze saphindisela ngokupheleleyo ezitheni zaso, njengoba kulotshiwe oGwalweni lukaJasha. Ilanga lema phakathi laphakathi kwesibhakabhaka laphuza ukutshona okosuku lonke.
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 Kakuzange kube losuku olwafana lalo ngaphambili kumbe kuze kube lamhlanje, usuku lapho uThixo alalela khona umuntu. Ngeqiniso uThixo wayelwela u-Israyeli!
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 Ngakho uJoshuwa waphindela labo bonke abako-Israyeli ezihonqweni zaseGiligali.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 Amakhosi lawo womahlanu abaleka ayacatsha ebhalwini lwaseMakheda.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 Kwathi uJoshuwa esetshelwe ukuthi amakhosi womahlanu ayetholakale ecatshile ebhalwini lweMakheda,
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 wathi, “Giqani amatshe amakhulu liwafake emlonyeni wobhalu, beselisithi amanye amadoda alinde.
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 Kodwa lingemi! Xotshani izitha zenu, lingazivumeli ukuthi zifike emadolobheni azo, ngoba uThixo uNkulunkulu wenu esezinikele ezandleni zenu.”
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Ngakho uJoshuwa labako-Israyeli bababhubhisa baphosa baphela bonke kodwa abalutshwana abasalayo banelisa ukufika emadolobheni abo ayezinqaba.
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 Ibutho lonke lenelisa ukuphenduka ngokuthula kuJoshuwa esihonqweni seMakheda, njalo kakho owake wakhuluma okubi ngabako-Israyeli.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 UJoshuwa wathi, “Vulani umlomo wobhalu beseliletha amakhosi womahlanu eze kimi.”
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 Ngakho bakhupha amakhosi womahlanu ebhalwini, inkosi yaseJerusalema, eyeHebhroni, yeJamuthi, eyeLakhishi kanye leyase-Egiloni.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 Bathi sebelethe amakhosi la kuJoshuwa, wabiza wonke amadoda ako-Israyeli wasesithi kubo bonke abalawuli bamabutho ababeze laye, “Wozani lapha lizofaka inyawo zenu entanyeni zala amakhosi.” Ngakho beza phambili basebefaka inyawo zabo entanyeni zawo.
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 UJoshuwa wathi kubo, “Lingesabi; lingadangali qinani libe lezibindi. Lokhu yikho okuzakwenziwa nguThixo kuzozonke izitha elizalwisana lazo.”
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Ngakho uJoshuwa wawabulala amakhosi la wawalengisa ensikeni ezinhlanu, alenga lapho kwaze kwahlwa.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 Ekutshoneni kwelanga uJoshuwa walaya ukuthi bawethule bawaphose ebhalwini lapho ayekade ecatshe khona. Emlonyeni wobhalu bafaka amatshe amakhulu alokhu ekhona lanamhlanje.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 Ngalelolanga uJoshuwa wathumba iMakheda. Wahlasela idolobho kanye lenkosi yalo ngenkemba, wabhubhisa wonke umuntu owayephakathi kwalo. Kakho owatshiywa ephila. Wenza enkosini yeMakheda lokho ayekwenze enkosini yaseJerikho.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 Ngakho uJoshuwa labo bonke abako-Israyeli ababelaye basuka eMakheda baya eLibhina balihlasela.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 UThixo waphinda wanikela lelodolobho lenkosi yalo esandleni sika-Israyeli. UJoshuwa wahlasela ngenkemba idolobho laye wonke umuntu owayephakathi kwalo. Kakho owatshiywa ephila lapho. Wenza enkosini yalo lokho ayekwenze enkosini yeJerikho.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 Ngakho uJoshuwa labo bonke abako-Israyeli ayelabo bahamba besuka eLibhina besiya eLakhishi; balihanqa basebelihlasela.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 UThixo wanikela iLakhishi ku-Israyeli, uJoshuwa wayithatha ngelanga lesibili. Idolobho laye wonke umuntu owayephakathi kwalo wakuhlasela ngenkemba, njengalokho ayekwenze eLibhina.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 Kunjalo-nje uHoramu inkosi yaseGezeri yayize ukuzoncedisa iLakhishi kodwa uJoshuwa wayehlula ndawonye lebutho layo, kakho owatshiywa ephila.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 Ngakho uJoshuwa labo bonke abako-Israyeli ababelaye basuka eLakhishi baya edolobheni le-Egiloni; basebelihanqa balihlasela.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 Balithumba ngalelolanga, balihlakaza ngenkemba basebebhubhisa wonke umuntu owayephakathi kwalo, njengalokho ababekwenze eLakhishi.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 Ngakho uJoshuwa labo bonke abako-Israyeli ababelaye bahamba besuka e-Egiloni baya eHebhroni bayihlasela.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 Balithumba lelodolobho ngenkemba ndawonye lamakhosi alo, imizana yalo laye wonke umuntu owayephakathi kwalo, kakho owatshiywa ephila. Njengalokho abakwenza e-Egiloni, balitshabalalisa laye wonke umuntu owayephakathi kwalo.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
38 Ngakho uJoshuwa labo bonke abako-Israyeli ayelabo baphenduka bahlasela iDebhiri.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 Bathumba lelidolobho, inkosi lemizi yalo, bayihlasela ngenkemba. Bonke abantu ababephakathi kwalo babhujiswa baphela. Kakho owatshiywa ephila. Benza eDebhiri lenkosini yakhona lokho abakwenza eLibhina lenkosini yakhona kanye leHebhroni.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 Ngakho uJoshuwa wasinqoba sonke isabelo, okugoqela ilizwe lamaqaqa, iNegebi, emawatheni ezintaba entshonalanga lemithezukweni yezintaba ndawonye lamakhosi alapho wonke. Kakho owatshiywa ephila. Wabhubhisa bonke abebephefumula, njengoba uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli wayebalayile.
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 UJoshuwa wabanqoba kusukela eKhadeshi Bhaneya kusiya eGaza lakuso sonke isabelo seGosheni kusiya eGibhiyoni.
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 Wonke amakhosi la lamazwe awo athunjwa nguJoshuwa ekuhlaseleni kunye, ngenxa yokuthi uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, walwela u-Israyeli.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 Ngakho uJoshuwa waphindela laye wonke u-Israyeli ezihonqweni zaseGiligali.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.