< UJona 2 >

1 Ephakathi kwenhlanzi uJona wakhuleka kuThixo uNkulunkulu wakhe.
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 Wathi: “Ekuhluphekeni kwami ngambiza uThixo, wangiphendula. Ngisekujuleni kwengcwaba ngacela uncedo, wena wakulalela ukukhala kwami. (Sheol h7585)
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
3 Wangiphosela ezinzikini, phakathi emathunjini enlwandle, amagagasi agubhazela emaceleni wonke; wonke amagagasi akho lezimpophoma zawo kwangisibekela.
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Ngathi, ‘Sengixotshiwe ebusweni bakho; kodwa ngizakhangela njalo ethempelini lakho elingcwele.’
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Indonga zamanzi zaziqonde ukungimbokotha, ngangihanqwe yinziki; inkunkuma yotshani bolwandle yangithandela ekhanda.
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Ngagalula ngatshona empandeni zezintaba; umhlaba ongaphansi wangivalela okwaphakade. Kodwa wena wayikhupha impilo yami egodini, wena Thixo, Nkulunkulu wami.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 Lapho impilo yami yayisincipha, ngakhumbula wena, Thixo, umkhuleko wami waphakamela kuwe, ethempelini lakho elingcwele.
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 Labo ababambelela ezithombeni ezingelamsebenzi balahlekelwa ngumusa ongaba ngowabo.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Kodwa mina, ngizakuthi ngihlabela ingoma yokubonga ngenze umhlatshelo kuwe. Engikufungileyo ngizakugcwalisa. Insindiso ivela kuThixo.”
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 UThixo walaya inhlanzi, yona yase imhlanza uJona emhlabathini owomileyo.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

< UJona 2 >