< UJohane 7 >

1 Ngemva kwalokhu uJesu wahambahamba eGalile, kazathanda ukuya eJudiya ngoba amaJuda alapho ayefuna indlela yokumbulala.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Kwathi uMkhosi wamaJuda weziHonqo ususondele
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 abafowabo bakaJesu bathi kuye, “Sekumele usuke lapha uye eJudiya ukuze abafundi bakho babone imimangaliso oyenzayo.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 Kakho umuntu othi efuna ukuba lodumo asebenzele ensitha. Njengoba usenza izinto lezi ziveze emhlabeni.”
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 Ngoba labafowabo babengakholwa kuye.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Ngakho uJesu wabatshela wathi, “Kasikafiki isikhathi sami salokho; kini loba yisiphi isikhathi sililungele.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 Umhlaba ngeke ulizonde, kodwa mina uyangizonda ngoba ngiveza ukuthi lokho okwenzayo kubi.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Hambani lina emkhosini. Mina kangikayi emkhosini lowo ngoba kimi kasikafiki isikhathi esifaneleyo.”
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 Esetsho lokhu wazihlalela eGalile.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 Kodwa ngemva kokuba abafowabo sebehambile emkhosini laye waya khona, hatshi obala kodwa wahamba ensitha.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 Khonapho emkhosini amaJuda ayemlindele ebuza esithi, “Ingaphi indoda leyana?”
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 Phakathi kwamaxuku abantu kwakulokunyenyezelana ngaye. Abanye bathi, “Ungumuntu olungileyo.” Abanye baphendula bathi, “Hatshi, ukhohlisa abantu.”
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Kodwa kakho owakhuluma ngaye obala ngokwesaba amaJuda.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 Kwathi isikhathi somkhosi sesiphakathi laphakathi uJesu wasesiya egumeni lethempeli waqalisa ukufundisa.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 AmaJuda amangala, abuza athi, “Indoda le yaluzuza kanjani ulwazi olungaka yona ingafundanga?”
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 UJesu waphendula wathi, “Imfundiso yami kayisiyami. Ivela kulowo ongithumileyo.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 Nxa umuntu ekhetha ukwenza intando kaNkulunkulu uzabona ingabe imfundiso yami ivela kuNkulunkulu loba ngiyazikhulumela.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 Lowo ozikhulumelayo wenzela ukuzizuzela udumo, kodwa lowo osebenzela udumo lwalowo omthumileyo ngumuntu weqiniso; kakulankohliso kuye.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 UMosi kalinikanga yini umthetho? Kodwa kakho lamunye kini owugcinayo umthetho. Kungani lifuna ukungibulala na?”
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 Ixuku labantu laphendula lathi, “Ulamadimoni wena. Ngubani ofuna ukukubulala?”
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 UJesu wathi kubo, “Ngenza umangaliso owodwa lamangala kakhulu lonke.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Kodwa ngoba uMosi walipha ukusoka (loba iqiniso liyikuthi kakuvelanga kuMosi kodwa kubokhokho), liyamsoka umntwana ngeSabatha.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 Manje-ke, nxa umntwana engasokwa ngeSabatha kungabi yikuwephula umthetho kaMosi, pho mina lingizondelani ngokuthi ngisilise umuntu ngokupheleleyo ngeSabatha na?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Khawulani ukusola ngokubona kwamehlo kodwa yahlulelani ngokuqondileyo.”
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Ngalesosikhathi abanye abantu baseJerusalema babuza bathi, “Kanti kasuye yini umuntu lo abafuna ukumbulala na?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 Nangu phela ekhuluma egcekeni kodwa kabatsho lutho kuye. Kambe iziphathamandla zingabe sezibone ukuthi nguye uKhristu na?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Kodwa siyakwazi thina lapha indoda le edabuka khona; nxa uKhristu esefika, kakho ozakwazi lapho avela khona.”
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Kwathi uJesu elokhu esafundisa egumeni lethempeli, wamemeza wathi, “Yebo, liyangazi njalo liyakwazi lapho engivela khona. Kangizibuyelanga lapha kodwa lowo ongithumileyo uqinisile. Kalimazi
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 kodwa mina ngiyamazi ngoba ngivela kuye, nguye ongithumileyo.”
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 Besizwa lokhu bazama ukumbamba kodwa kakho owambeka isandla ngoba isikhathi sakhe sasingakafiki.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 Loba kunjalo, abanengi exukwini labantu bakholwa kuye. Bathi, “Nxa uKhristu angafika, kambe uzakwenza imimangaliso okwedlula umuntu lo?”
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 AbaFarisi bezwa abantu benyenyeza izinto ezinjalo ngaye. AbaFarisi labaphristi abakhulu basebethuma amanxusa ethempelini ukuba ayembopha.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 UJesu wathi, “Ngilani okwesikhathi esifitshane, besengihamba ngisiya kuye ongithumileyo.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Lizangidinga kodwa lingangifumani; lalapho engikhona lingeke lifike.”
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 AmaJuda abuzana athi, “Umuntu lo ufuna ukuya ngaphi lapho esingeke samfumana khona na? Uzakuya ebantwini bakithi abahlakazekileyo abahlala phakathi kwamaGrikhi, afundise amaGrikhi na?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 Ubesitshoni esithi, ‘Lizangidinga, kodwa lingangifumani,’ njalo wathi, ‘Lapho engikhona lingeke lifike’?”
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 Ngelanga lokucina elaliqakatheke kakhulu emkhosini, uJesu wasukuma wakhuluma ngelizwi elikhulu wathi, “Nxa ekhona owomileyo keze kimi azonatha.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 Loba ngubani okholwa kimi njengoba uMbhalo utshilo, imifula yamanzi aphilayo izageleza ngaphakathi kwakhe.”
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 Ngalokhu wayesitsho uMoya, okwakuzakuthi labo abakholwa kuye bamamukele ngesikhathi esizayo. Kuze kube yilesosikhathi uMoya wawungakathelwa ebantwini, njengoba uJesu wayengakakhazimuliswa.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Sebewazwile amazwi akhe abanye bathi, “Ngeqiniso umuntu lo nguye umphrofethi.”
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Abanye bathi, “Nguye uKhristu.” Abanye njalo babuza bathi, “Kungenzeka kanjani ukuthi uKhristu avele eGalile na?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 UMbhalo kawutsho yini ukuthi uKhristu uzavela kusendo lukaDavida, eBhethilehema, umuzi lapho uDavida ayehlala khona.”
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 Kanjalo abantu badabukana phakathi ngenxa kaJesu.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 Abanye babefuna ukumbamba, kodwa kakho owambeka isandla.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 Amanxusa ethempelini acina esebuyela kubaphristi abakhulu labaFarisi athi, “Kungani lingezanga laye?”
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 Amanxusa afakaza athi, “Kakho osewake wakhuluma njengaloyamuntu.”
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 AbaFarisi bakhwaza bathi, “Litsho ukuthi lani uselikhohlisile?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Ukhona na kubabusi loba kubaFarisi osebeke ithemba lakhe kuye?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 Hatshi! Kodwa inkunkuma yabantu le engazilutho ngezomthetho, iqalekisiwe.”
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 UNikhodimasi owayeye kuJesu mandulo, owayengomunye wabo wabuza wathi,
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 “Kanti umthetho wakithi uyamlahla na umuntu engaqalanga wabuzwa ukuthi yena uthini ngokwakhe?”
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 Baphendula bathi, “Lawe uvela eGalile yini? Ake ukudingisise, uzabona ukuthi kakulamphrofethi ongaphuma eGalile.” [
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 Ngakho bonke basuka baya emizini yabo.
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

< UJohane 7 >