< UJobe 28 >
1 Kulomgodi wesiliva lendawo lapho okucengwa khona igolide.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Insimbi ithathwa emhlabathini, lethusi lincibilikiswa emanyeleni.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Umuntu uyawuxotsha umnyama; uguduza ezingoxweni eziphansi kude edinga amanyele emnyameni othe bhuqe.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Khatshana kwezindawo zabantu ugebha umgodi, ezindaweni lapho okungafiki nyawo lwamuntu; khatshana kwabantu uyalenga, azunguzeke.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Umhlaba, okuphuma kuwo ukudla, uyaguquka ngaphansi ingathi utshiswe ngomlilo;
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 amasafire amatshe amahle ayaphuma emadwaleni, uthuli lwawo lugcwele igolide.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 Kakukho nyoni edla inyama eyaziyo leyondlela efihlekileyo, kakulalihlo laluphi ukhozi oselwake lwayibona.
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Izilo ezizithembileyo kazilubeki unyawo kuyo, njalo kakulasilwane esizingela khona.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 Isandla somuntu yiso esihlasela idwala eliyinsengetshe siveze obala impande zezintaba.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Uyaligubha idwala angene; ilihlo lakhe liwabone wonke amagugu alo.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Uyathungatha lapho okudabuka khona imifula aveze obala izinto ezifihlekileyo.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Kodwa ukuhlakanipha kungafunyanwa ngaphi na? Kuhlala ngaphi na ukuzwisisa?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Umuntu kakuzwisisi ukuqakatheka kwakho; kakufunyanwa elizweni labaphilayo.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Phansi ekujuleni kuthi, “Kakukho kimi”; ulwandle luthi, “Kangilakho mina.”
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Kungeke kwathengwa ngegolide elicolekileyo, njalo lentengo yakho ingeke yalinganiswa ngesiliva.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 Kungeke kwathengwa ngegolide lase-Ofiri, loba nge-onikisi kumbe isafire.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Kungazake kulinganiswe legolide loba amatshe akhazimulayo, njalo kakuzuzwa ngemiceciso yegolide.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Amatshe amahle ekhorali lejaspa lawo kawabalwa lapha; intengo yokuhlakanipha ingaphezulu kwamarubhi.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Ithophazi yaseKhushi ngeke ilinganiswe lakho; ngeke kuthengwe langegolide elicolekileyo.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Pho kuvela ngaphi ukuhlakanipha na? Kuhlala ngaphi ukuzwisisa?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Kufihliwe emehlweni ento yonke ephilayo, kucatshisiwe lakuzo izinyoni zasemoyeni.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 INcithakalo loKufa kuthi, “Amahungahunga akho yiwo kuphela esiwezwayo.”
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 UNkulunkulu uyayizwisisa indlela yakho njalo nguye yedwa okwaziyo lapho okuhlala khona,
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 ngoba uyayikhangela imikhawulo yomhlaba akubone konke okungaphansi kwamazulu.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Wathi emisa umfutho womoya, elinganisa isimo samanzi,
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 wathi ebeka umthetho wezulu elinayo lendlela yezulu elilesiphepho,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 wasekukhangela ukuhlakanipha wakuhlola butsha; wakukholwa wakuqinisa, wakulinga ukuthi kuqinile.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Wathi emuntwini, “Ukumesaba uThixo yikho ukuhlakanipha, lokuxwaya ububi yikho ukuzwisisa.”
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”