< UJobe 27 >

1 UJobe waqhubeka ngenkulumo yakhe wathi:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 “Ngifunga ngoNkulunkulu ophilayo, ngubani ongithathele ilungelo lami lokwahlulelwa ngokulunga, uSomandla, ongizwise ubuhlungu bomphefumulo,
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 nxa ngilokhu ngiselempilo ngaphakathi kwami, umphefumulo kaNkulunkulu usemakhaleni ami,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 izindebe zami kazisoze zikhulume ububi, lolimi lwami kaluyikukhuluma inkohliso.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Kangisoze ngivume ukuthi lina lilungile ngelikutshoyo; ngizaze ngiyekufa ngingabulandulanga ubuqotho bami.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Ngizakugcina ukulunga kwami ngingakuyekeli; umzwangedwa wami kawuyikungihlupha empilweni yami.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Sengathi izitha zami zingaba njengababi, abaxabana lami babe njengabangaqondanga!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Ngoba ulethemba bani ongakholwayo nxa esefile, uNkulunkulu angathatha impilo yakhe na?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 UNkulunkulu uyakulalela yini ukukhala kwakhe nxa usizi lumehlela na?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Uzakuthola yini ukuthokoza kuSomandla? Uzacela kuNkulunkulu sonke isikhathi na?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Ngizalifundisa mayelana lamandla kaNkulunkulu; izindlela zikaSomandla kangiyikuzifihla.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Lonke lizibonele lokhu ngokwenu. Pho, ngeyani inkulumo yonke le eyize na?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Nansi isabelo uNkulunkulu asiqumela ababi, ilifa elemukelwa ngumuntu olesihluku sivela kuSomandla:
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Loba bebanengi njani abantwabakhe, isabelo sabo yinkemba; lenzalo yakhe kayisoze lanini izuze ukudla okwaneleyo.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Isifo esibi sizabangcwaba labo abatshiywa nguye besaphila, labafelokazi babo kabayikubalilela.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Lokuba angaze abuthelele isiliva njengothuli lezigqoko zibe yinqwaba njengodaka,
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 lokho akubuthelelayo abalungileyo bazakugqokela, labangelacala bazakwaba isiliva sakhe.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Indlu ayakhayo injengesidleke sobulembu, njengedumba elenziwe ngumlindi.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Uthi esiyalala enothile, kodwa kasayikuphinda njalo; uthi esevula amehlo, konke sekuphelile.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Utshaywa luvalo kungathi ufuqwa yisikhukhula; isiphepho siyamhwitha ebusuku.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Umoya wempumalanga udlula laye, anyamalale; uyamkhukhula endaweni yakhe.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Utshaya phezu kwakhe ngesihluku esithi uyabaleka ecambalele evika amandla awo.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Utshaya izandla umhleka ulunya uvunguza laye umsusa endaweni yakhe.”
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< UJobe 27 >