< UJobe 16 >

1 UJobe wasephendula wathi:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Sengezwa izinto ezinengi ezifana lalezi; lingabaduduzi ababi lina lonke!
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Zizaphela nini inkulumo zokubhuda kwenu lokhu? Kuyini okulihluphayo laphikelela nje lidaza inkani?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Lami bengingakhuluma njengani aluba yini elisesikhundleni sami; ngabe ngikhupha inkulumo ezimnandi ngilisola ngize nginikine ikhanda lami.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Kodwa umlomo wami ngabe uyaliqinisa; induduzo yezindebe zami idedise inhlungu zenu.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Kodwa nxa ngikhuluma, ubuhlungu obukimi kabudedi; loba ngingaze ngithule, kabupheli.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Ngeqiniso, Nkulunkulu, usungiqede amandla; usuyitshabalalisile yonke imuli yami.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Usungibophile sekuyibo ubufakazi balokho; lokucikizeka kwami kuyakhula kungilahla.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 UNkulunkulu uyanginxwanela angidlikize ngolaka lwakhe, angigedlele amazinyo; isitha sami singinyonkoloze ngamehlo ahlabayo.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Abantu bavula imilomo yabo bengihoza; bangimakala esihlathini bengihlambaza babambane bangihlanganyele.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 UNkulunkulu usenginikele ebantwini ababi wangiphosela ezandleni zezigangi.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Konke kwakukuhle kimi, kodwa wangibhidliza; wangixhakalaza ngentamo wangichoboza. Usengenze ngaba yinto yakhe yokunenjwa;
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 abacibi bemtshoko bakhe bangihanqile. Ungiciba izinso zami engelazwelo achithele inyongo yami phansi.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Ungisukela njalonjalo; angidumele njengebutho.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Sengithungele isembatho sesaka emzimbeni wami ngathukuza ibunzi lami othulini.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Ubuso bami sebubomvu ngokukhala, amathunzi anzima ahonqolozela amehlo ami;
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 kodwa izandla zami kaziluqhelanga udlakela, lomkhuleko wami uhlanzekile.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 Awu mhlaba, ungaligqibeli igazi lami; sengathi lokukhala kwami kungaze kwacitshwa lanini!
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Lakhathesi ufakazi wami usezulwini; umeli wami uphezulu khonale.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Umeli wami ngumngane wami nxa amehlo ami empompoza inyembezi kuNkulunkulu;
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 uyamncengela umuntu kuNkulunkulu njengomuntu encengela umngane wakhe.
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Kusasele iminyakana engemingaki andubana ngiye lapho kungabuywa khona.”
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< UJobe 16 >