< UJobe 11 >

1 UZofari umNahama wasephendula wathi:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 “Uthi amazwi wonke la angayekelwa ukuphendulwa na? Uwawane lolu luyekelwe nje lubheda?
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Umbhedo wakho lo ungenza abantu bathule na? Uthi ungangakhuzwa muntu wena ukhulumela eceleni?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 Uthi kuNkulunkulu, ‘Inkolo yami kayilansolo njalo ngimsulwa phambi kwakho.’
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 Oh, ngize ngifise ukuthi ngabe uNkulunkulu uyakhuluma, avule izindebe zakhe ekusola
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 akuvulele imfihlo zokuhlakanipha, ngoba inhlakanipho yeqiniso ikabili. Yazi lokhu: UNkulunkulu uvele usezikhohliwe ezinye izono zakho.
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 Kambe ungayifinyelela yini imfihlakalo kaNkulunkulu? Ungaziphenya iziphetho zikaSomandla na?
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 Ziqongile ngaphezu kwamazulu, ungenzani kambe? Zizikile kulokujula kolwandle, kuyini ongakwazi pho? (Sheol h7585)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
9 Ukulinganiswa kwazo kude kulomhlaba njalo kubanzi kulolwandle.
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 Nxa engeza lapha akuphosele entolongweni abize inkundla, ngubani ongamphikisa na?
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Liqiniso ukuthi uyababona abantu abakhohlisayo; njalo nxa ebona okubi, kananzeleli na?
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Kodwa umuntu oyisithutha ngeke ahlakaniphe njengoba ubabhemi weganga engeke azalwa ngumuntu.
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 Kodwa nxa ugxilisa inhliziyo yakho kuye uphakamisele izandla zakho kuye,
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 nxa ulahla isono esisesandleni sakho ungavumeli bubi buhlale ethenteni lakho,
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 lapho-ke uzabuveza ubuso bakho ungelanhloni; uzakuma uqine ungesabi.
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Uzalukhohlwa ngempela uhlupho lwakho, lufike nje engqondweni njengezikhukhula ezadlulayo.
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 Impilo izakhanya kulemini enkulu, lobumnyama buzakuba njengasekuseni.
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 Uzavikeleka, ngoba ithemba likhona; uzakhangela ofuna khona uzuze ukuphumula uvikelekile.
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Uzazilalela, kungekho okwethusayo, njalo abanengi bazabe sebezisondeza kuwe.
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 Kodwa amehlo ababi azafiphala, behluleke lokubaleka; ithemba labo libe yikuhotsha umoya wokufa.”
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

< UJobe 11 >