< UJeremiya 9 >

1 Awu, sengathi ngabe ikhanda lami lingumthombo wamanzi, lamehlo ami angumthombo wezinyembezi! Kade ngizakhala emini lebusuku ngikhalela abantu bami ababuleweyo.
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Awu, sengathi ngabe enkangala ngilendawo engahlala izihambi, ukuba ngisuke ebantwini bami ngisuke kubo, ngoba bonke bayizifebe, ixuku labantu abangathembekanga.
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 “Benza izindimi zabo zilunge njengesavutha ukuba batshoke amanga, ukuthi bayanqoba elizweni akusikho ngeqiniso. Basuka kokunye ukona baye kokunye; kabangamukeli,” kutsho uThixo.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 “Qaphela abangane bakho, ungabathembi abafowenu. Ngoba wonke umfowenu ungumkhohlisi, njalo wonke umngane ungumhlebi.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Umngane ukhohlisa umngane, njalo kakho okhuluma iqiniso. Sebafundisa izindimi zabo ukuqamba amanga, bayazidinisa ngokona.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Lihlala phakathi kwenkohliso, ngenkohliso yabo bayala ukungamukela,” kutsho uThixo.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Ngakho uThixo uSomandla uthi: “Khangelani, ngizabacolisa ngibahlole, ngoba kuyini okunye engingakwenza ngenxa yesono sabantu bami?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Ulimi lwabo lungumtshoko olobuthi, lukhuluma inkohliso. Lowo lalowo ukhuluma kuhle kubomakhelwane bakhe, kodwa enhliziyweni zabo bebathiya ngemijibila.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Kakufanele ngibajezisele lokhu na?” kubuza uThixo. “Kakufanele ngiphindisele esizweni esinjengalesi na?”
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 Ngizakhala ngililele izintaba ngibuye ngililele lamadlelo asenkangala. Atshabalele njalo kakho ohambela kuwo, lokubhonsa kwezinkomo akuzwakali. Izinyoni zasemoyeni sezibalekile, lezinyamazana kazisekho.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 “IJerusalema ngizalenza libe yinqumbi yonxiwa, isikhundla samakhanka, njalo ngizawadiliza amadolobho akoJuda ukuze kungabikhona ohlala kuwo.”
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Nguphi umuntu ohlakaniphileyo ukuba akuzwisise lokhu? Ngubani ofundiswe nguThixo ongakuchaza? Kungani ilizwe litshabalalisiwe lachithwa njengenkangala ukuze kungadluli muntu kulo?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 UThixo wathi, “Kungenxa yokuthi sebelahle umthetho wami engababekela wona; kabangilalelanga, lomthetho wami kabawulandelanga.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Esikhundleni salokho, bona balandele ubulukhuni bezinhliziyo zabo; balandele oBhali, njengokufundiswa kwabo ngoyise.”
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Ngakho-ke, uThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: “Khangelani, abantu laba ngizabadlisa ukudla okubabayo ngibanathise lamanzi alobuthi.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Ngizabahlakazela ezizweni bona kanye laboyise abangazange bazazi, njalo ngizabalandela ngenkemba ngize ngibaqede du.”
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 UThixo uSomandla uthi: “Cabangani khathesi! Bizani abesifazane abalilayo beze, libize labo abalobuciko obumangalisayo.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Kabeze ngokuphangisa, bazesililela amehlo ethu aze ehlise inyembezi lempophoma zamanzi zigeleze, ziphuma enkopheni zethu.”
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Ilizwi lokukhala liyezwakala livela eZiyoni: “Yeka kunganani ukuchithakala kwethu! Yeka ubukhulu behlazo lethu! Kumele sisuke elizweni lethu ngoba izindlu zethu zidiliziwe.”
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Khathesi, lina abesifazane, zwanini ilizwi likaThixo, vulani indlebe zenu lizwe amazwi omlomo wakhe. Fundisani amadodakazi enu ukulila, lifundisane amazwi okukhala.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Ukufa kukhwele kwangena ngamafastela ethu, njalo kungenile lasezinqabeni zethu, sekususe abantwana emigwaqweni kanye lamajaha ezindaweni zikazulu.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Tshono uthi, uThixo uthi, “‘izidumbu zabafileyo zizalala njengezibi egangeni, njengamabele aqunywe ngemva kovunayo, okungekho ozawabutha.’”
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 UThixo uthi: “Ohlakaniphileyo kangazincomi ngokuhlakanipha kwakhe, loba indoda elamandla izincome ngamandla ayo, loba indoda enothileyo izincome ngenotho yayo,
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 kodwa lowo ozincomayo, kazincome ngokuthi uyaqedisisa njalo uyangazi, ukuthi mina nginguThixo, osebenzisa umusa, imfanelo lokulunga emhlabeni, ngoba lezizinto ziyangithokozisa,” kutsho uThixo.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 UThixo uthi, “Insuku ziyeza, lapho engizabajezisa khona bonke abasoke enyameni kuphela,
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 iGibhithe, loJuda, lo-Edomi, lo-Amoni loMowabi labo bonke abahlala enkangala ezindaweni ezikhatshana. Ngoba izizwe zonke lezi kazisokanga, njalo lendlu yonke ka-Israyeli kayisokanga enhliziyweni.”
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< UJeremiya 9 >