< U-Isaya 49 >
1 Ngilalelani lina zihlenge; zwanini lokhu lina zizwe ezikude: uThixo wangibiza ngingakazalwa; kusukela ekuzalweni kwami ubelitsho ibizo lami.
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 Wenza umlomo wami waba njengenkemba eloliweyo, wangifihla emthunzini wesandla sakhe. Wangenza ngaba ngumtshoko ololiweyo, wangifihla emxhakeni wakhe wemitshoko.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
3 Wathi kimi, “Wena Israyeli uyinceku yami, engizabonakalisa inkazimulo yami ngayo.”
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 Kodwa mina ngathi, “Mina ngisebenzele ize; amandla ami ngiwachithele ize lobala, ikanti okufanele mina kusesandleni sikaThixo, lomvuzo wami ukuNkulunkulu.”
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 Khathesi uThixo uthi, yena owangibumbayo esiswini ukuba ngibe yinceku yakhe ukuze ngibuyisele uJakhobe kuye lokuqoqela u-Israyeli kuye, ngoba ngiphakanyisiwe emehlweni kaThixo njalo uNkulunkulu wami ubengamandla ami
Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 uthi: “Kuyinto encane kakhulu kuwe ukuba yinceku yami ukuze uvuselele izizwe zikaJakhobe ubuyise labako-Israyeli engibalondolozileyo. Ngizakwenza ube yikukhanya kwabeZizwe, ukuze ufikise usindiso lwami emikhawulweni yomhlaba.”
Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Nanku okutshiwo nguThixo, uMhlengi loNgcwele ka-Israyeli, utsho kuye oweyiswa, wenyanywa yisizwe, kuyo inceku yababusi: “Amakhosi azakubona asukume, amakhosana azakubona akhothame, ngenxa kaThixo othembekileyo, oNgcwele ka-Israyeli okukhethileyo.”
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
8 Nanku okutshiwo nguThixo: “Ngesikhathi esifaneleyo kimi ngizakuphendula, langosuku lwensindiso ngizakusiza. Ngizakulondoloza ngikwenze ube yisivumelwano sabantu, ukubuyisela ilizwe lokwaba kutsha amafa abo achithekayo,
Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 uthi kwabathunjiweyo, ‘Phumani,’ kulabo abasemnyameni uthi, ‘Khululekani!’ Bazadlela emaceleni emigwaqo bathole amadlelo kuwo wonke amaqaqa alugwadule.
Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Kabayikulamba kumbe bome, lokutshisa kwasenkangala kumbe okwelanga kabayikukuzwa. Lowo obazwela isihawu uzabakhokhela abase emithonjeni yamanzi.
Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 Izintaba zami zonke ngizazenza zibe yizindlela, imigwaqo yami izaphakamela phezulu.
Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Khangelani, bazakuza bevela khatshana, abanye bevela enyakatho, abanye bevela entshonalanga labanye bevela emangweni wase-Asiwani.”
Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Hlabelelani ngentokozo lina mazulu; jabula lawe mhlaba; tshayani ingoma lina zintaba. Ngoba uThixo uyabaduduza abantu bakhe njalo uzakuba lesihawu kwabahluphekayo bakhe.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 Kodwa iZiyoni yathi, “UThixo ungilahlile, uThixo usengikhohliwe.”
Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
15 “Owesifazane angamkhohlwa umntanakhe omunyayo na, angabi lesihelo emntwaneni amzeleyo na? Lanxa engamkhohlwa, mina angiyikukukhohlwa!”
“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Khangela, sengikudwebe ezintendeni zezandla zami; imiduli yakho ihlezi iphambi kwami.
Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Amadodana akho aphanga emuva, lalabo abakuchithayo bayasuka kuwe.
Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Phakamisa amehlo akho ukhangele emaceleni wonke, wonke amadodana akho ayaqoqana eze kuwe. UThixo uthi, “Ngeqiniso elinjengoba ngiphila, bonke uzabagqiza njengezigqizo, ucece ngabo njengomlobokazi.
Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 Lanxa nje wadilizwa waba lunxiwa lelizwe lakho lachithwa, khathesi uzakuba mncane kakhulu ebantwini bakho; lalabo abakuchithayo bazakuba khatshana.
“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 Abantwana abazalwa ngesikhathi sokufelwa kwakho bazakutsho lawe usizwa bathi, ‘Indawo le incinyane kakhulu kithi; siphe enye njalo indawo yokuhlala.’
Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 Lapho-ke uzakuthi enhliziyweni yakho, ‘Ngubani owangizalela laba na? Ngafelwa njalo ngaba njengongazalanga; ngaxotshwa elizweni, ngalahlwa. Laba bondliwa ngubani? Mina ngangisele ngedwa, kodwa laba-ke, bavele ngaphi?’”
Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
22 Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: “Khangela, ngizaqhweba abeZizwe. Ngizaphakamisela uphawu lwami ebantwini; bazaletha amadodana akho bewagonile, amadodakazi akho bewathwele ngamahlombe abo.
Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 Amakhosi azakuba ngoyihlo bokukukhulisa, amakhosikazi awo abe ngonyoko bokukondla. Bazakhothama phambi kwakho ubuso babo buphansi, emhlabathini, bazakhotha uthuli ezinyaweni zakho. Lapho-ke uzakwazi ukuthi mina nginguThixo; labo abangithembayo abayikudaniswa.”
Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 Amabutho angemukwa impango na, kumbe abathunjiweyo bahlengwe kwabesabekayo na?
Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 Kodwa nanku okutshiwo nguThixo: “Yebo, abathunjiweyo bazathathwa emabuthweni lempango izahluthunwa futhi kwabesabekayo, ngoba ngizamelana lalabo abamelana lawe, abantwabakho ngizabahlenga.
Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 Ngizakwenza abancindezeli bakho badle inyama yemizimba yabo; bazadakwa ngelabo igazi njengewayini. Lapho-ke izizwe zonke zizakwazi ukuthi mina Thixo, nginguMsindisi wakho, uMhlengi wakho, uMninimandla kaJakhobe.”
Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”