< U-Isaya 36 >
1 Ngomnyaka wetshumi lane wokubusa kwenkosi uHezekhiya, uSenakheribhi inkosi yase-Asiriya wahlasela wonke amadolobho avikelweyo akoJuda wawathumba.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 Emva kwalokho inkosi yase-Asiriya yathuma umlawuli wayo lebutho elikhulu lisuka eLakhishi lisiya enkosini uHezekhiya eJerusalema. Kwathi umlawuli webutho esemi emgelweni wechibi elingaphezulu, elisendleleni eya eNsimini yoMgezisi,
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 u-Eliyakhimu indodana kaHilikhiya umgcini wesigodlo, loShebhina umabhalane kanye loJowa indodana ka-Asafi umbhali, baya kuye.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 Umlawuli webutho wathi kubo, “Tshelani uHezekhiya ukuthi, ‘Nanku okutshiwo yinkosi enkulu, inkosi yase-Asiriya ithi: Uthembeni ngalesisibindi sakho na?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 Uthi ulamaqhinga lamandla ebutho kodwa ukhuluma amazwi ayize. Uthembe bani uze ungihlamukele nje?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Khangela, ngiyazi uthembe iGibhithe, yona enjengomhlanga ozimvava osika isandla somuntu umlimaze nxa eweyamile. Unjalo uFaro inkosi yaseGibhithe kubo bonke abathembele kuye.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 Njalo nxa lisithi kimi, “Thina sithembe uThixo uNkulunkulu wethu,” kasuye yini uHezekhiya asusa izindawo zakhe eziphakemeyo lama-alithare akhe, esithi kuJuda leJerusalema, “Kumele likhonzele phambi kwaleli i-alithari”?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Khathesi woza wenze isivumelwano lenkosi yami, inkosi yase-Asiriya: Ngizakunika amabhiza azinkulungwane ezimbili nxa bekhona abazawagada!
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 Pho ungayehlula njani induna eyodwa yezikhulu ezincane zenkosi yami, lanxa uthembele eGibhithe ekutholeni izinqola zempi labagadi bamabhiza na?
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Phezu kwalokho, kanti ngizehlasela lokuzochitha ilizwe leli kungatshongo uThixo na? UThixo uqobo nguye othe ngizohlasela ilizwe leli ngilichithe.’”
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Ngakho u-Eliyakhimu loShebhina loJowa bathi kumlawuli webutho, “Ake ukhulume ezincekwini zakho ngesi-Aramayikhi ngoba siyasizwa. Ungasikhulumisi ngesiHebheru lababantu abasemdulini besizwa.”
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Kodwa umlawuli webutho waphendula esithi, “Inkosi yami ingithume ukuba izinto lezi ngizitsho kuphela enkosini yenu lakini, hatshi ebantwini abahlezi emdulini okuzakuthi labo njengani badle ubulongwe babo banathe lomchamo wabo na?”
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 Umlawuli webutho wasukuma wasememeza ngesiHebheru esithi, “Zwanini amazwi enkosi enkulu, inkosi yase-Asiriya!
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 Lokhu yikho okutshiwo yinkosi: Lingamvumeli uHezekhiya ukuba alikhohlise. Angeke alikhulule.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 Lingamvumeli uHezekhiya elincenga ukuba lithembele kuThixo lapho esithi ‘Ngempela uThixo uzasikhulula; idolobho leli kaliyikuphiwa esandleni senkosi yase-Asiriya.’”
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Lingamlaleli uHezekhiya. Nanku okutshiwo yinkosi yase-Asiriya: Yenza isivumelwano sokuthula lami, uphume uze kimi. Lapho-ke omunye lomunye uzakudla esivinini sakhe lasemikhiweni yakhe, anathe lamanzi emthonjeni wakhe,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 ngize ngifike ngilithathe, ngilise elizweni elifanana lelakini, ilizwe lamabele lewayini elitsha, ilizwe lesinkwa lezivini.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 “Lingavumeli uHezekhiya ukuthi alikhohlise esithi, ‘UThixo uzasikhulula.’ Kulonkulunkulu wesinye isizwe osewake wakhulula ilizwe lakhe esandleni senkosi yase-Asiriya na?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Bangaphi onkulunkulu baseHamathi le-Ariphadi na? Bangaphi onkulunkulu baseSefavayimi na? Bayikhululile iSamariya esandleni sami na?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Nguphi kubo bonke onkulunkulu bamazwe la oke wenelisa ukukhulula ilizwe lakhe kimi na? Pho uThixo angayikhulula njani iJerusalema esandleni sami na?”
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Kodwa abantu bathula kabazange batsho lutho, ngoba inkosi yayilaye yathi, “Lingamphenduli.”
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 U-Eliyakhimu indodana kaHilikhiya umgcini wesigodlo loShebhina umabhalane loJowa indodana ka-Asafi umbhali, baya kuHezekhiya izigqoko zabo zidabukile bamtshela okwakutshiwo ngumlawuli webutho.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.