< U-Isaya 25 >
1 Oh Thixo, wena unguNkulunkulu wami; ngizakudumisa ngibabaza ibizo lakho ngoba ngokuthembeka okupheleleyo, wenze izinto ezimangalisayo, izinto ezamiswa endulo.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 Wenze idolobho laba yinqwaba yemfucuza; idolobho elivikelweyo laba lunxiwa, inqaba yabezizweni kayiseyilo dolobho; kayiyikwakhiwa futhi.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Ngakho-ke abantu abalamandla bazakudumisa, amadolobho ezizwe ezilolunya azakwesaba.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Ubuyisiphephelo sabayanga, isiphephelo soswelayo osizini lwakhe, isivikelo phakathi kwesiphepho lomthunzi ekutshiseni kwelanga. Ngoba umoya wabalesihluku unjengesiphepho sitshayeka emdulini,
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 lanjengokutshisa kwasenkangala. Wena uthulisa umsindo wabezizweni; njengokutshisa kusehliswa ngumthunzi weyezi, ithuliswa kanjalo lengoma yaba lesihluku.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 Phezu kwale intaba uThixo uSomandla uzakwenzela abantu bonke idili lokudla okumnandi, idili lewayini elidala, inyama enhle kakhulu lewayini elihle kakhulu.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 Phezu kwale intaba uzadiliza isembeso esimboze abantu bonke, ilembu elembese izizwe zonke;
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 uzakuginya kokuphela ukufa. UThixo Wobukhosi uzakwesula inyembezi ebusweni babantu bonke; uzasusa ihlazo labantu bakhe emhlabeni wonke. UThixo usekhulumile.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 Ngalolosuku bazakuthi, “Ngempela lo nguNkulunkulu wethu; sethemba kuye, wasikhulula. Lo nguThixo, sethemba kuye; kasithokozeni sithabe ngokusisindisa kwakhe.”
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Isandla sikaThixo sizahlala phezu kwalintaba; kodwa uMowabi uzanyathelelwa ngaphansi ezweni lakhe njengotshani bunyathelelwa phansi emqubeni.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 Bazakwelulela izandla zabo kuye, njengenhlambi iselula izandla zayo ukuba intsheze. UNkulunkulu uzakuqeda ukuzigqaja kwabo phezu kokuhlakanipha kwezandla zabo.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 Uzadiliza izinqaba zenu eziphakemeyo azibhidlizele phansi; uzazidilizela phansi emhlabathini, kulo kanye uthuli.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.