< UHoseya 4 >
1 Zwanini ilizwi likaThixo, lina bako-Israyeli ngoba kulecala uThixo alethesa lina elihlala elizweni: “Akulakwethembeka, akulathando, akukho ukumamukela uNkulunkulu elizweni.
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Kulokuthuka kuphela, lokuqamba amanga lokubulala, lokuntshontsha kanye lobufebe; benza ububi bonke, njalo ukuchithwa kwegazi kulandela ukuchithwa kwegazi.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 Ilizwe liyalila ngenxa yalokhu, njalo bonke abahlala kulo bayacikizeka; izinyamazana zeganga lezinyoni zasemoyeni kanye lenhlanzi zasolwandle kuyafa.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Kodwa akungabi lamuntu omangalayo, akungabi lomuntu owethesa omunye icala ngoba abantu bakho bafana lalabo abamangalela umphristi.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 Liyakhubeka emini lebusuku, labaphrofethi bakhubeka kanye lani. Ngakho unyoko ngizamchitha,
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 abantu bami bachithwa yikungabi lolwazi. Njengoba likwalile ukwazi, lami ngiyalala njengabaphristi bami; ngoba kaliwunakanga umthetho kaNkulunkulu wenu, lami angiyikubanaka abantwana benu.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 Ngokwanda kwabaphristi, kwanda kanjalo lokona kwabo kimi, benanisa uDumo lwabo ngento elihlazo.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 Badla izono zabantu bami bajabuliswe yikuxhwala kwabo.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 Njalo kuzakuba kanje: Njengabantu, njengabaphristi. Bonke ngizabajezisela izindlela zabo, ngiphindisele kubo lezenzo zabo.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 Bazakudla kodwa bangasuthi; bazakwenza ubufebe kodwa bangandi, ngoba bamdelile uThixo ukuba bazinikele
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 ebufebeni, lewayini elidala kanye lelitsha elisusa ukuqedisisa kwabantu bami.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 Badinga izeluleko esithombeni sesigodo baphendulwe yiluthi lwesigodo. Umoya wobufebe uyabedukisa; kabathembekanga kuNkulunkulu wabo.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Banikela imihlatshelo ezingqongweni zezintaba batshise iminikelo phezu kwamaqaqa, ngaphansi komʼokhi, lomphophila kanye lomtherebhinti, lapho okulomthunzi omnandi. Ngakho amadodakazi enu enza ubuwule, labomalukazana benu benze ubufebe.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 Angiyikuwajezisa amadodakazi enu lapho esenza ubuwule loba omalukazana benu lapho besenza ubufebe, ngoba amadoda uqobo azwana lezifebe anikele imihlatshelo lezifebe ezisezindaweni zokukhonzela abantu abangelakuqedisisa bazabhubha.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 Lanxa ufeba, we Israyeli, uJuda kangabi lecala. Lingayi eGiligali; lingayi eBhethi-Aveni. Njalo lingafungi lisithi, ‘Ngeqiniso njengoba uThixo ekhona!’
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Abako-Israyeli bayiziqholo, njengethokazi eliyisiqholo. Pho uThixo angabelusela njani emadlelweni njengezimvu na?
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 U-Efrayimi uhlangene lezithombe; myekeleni enjalo!
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 Lalapho okunathwayo kwabo sekuphelile, bayaqhubeka ngobufebe babo; ababusi babo bazithanda kakhulu izindlela ezilihlazo.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Isavunguzane sizabakhukhula, lemihlatshelo yabo izabalethela ihlazo.”
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.