< UHoseya 11 >
1 “U-Israyeli esesengumntwana, ngangimthanda njalo indodana yami ngayikhupha eGibhithe.
“Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
2 Kodwa kwathi lapho u-Israyeli ngimbiza kanengi kwayikhona ehlehlela khatshana lami. Banikela imihlatshelo kuboBhali, batshisela lezifanekiso impepha.
Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
3 Yimi engafundisa u-Efrayimi ukuhamba, ngibabambe ngezingalo; kodwa kababonanga ukuthi yimi engabelaphayo.
Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
4 Ngabakhokhela ngentambo zomusa woluntu, ngezibopho zothando; ngaba njengomuntu osusa amajogwe entanyeni zabo, ngakhothamela phansi ukuba angiphe ukudla.
Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
5 Kabayikubuyela eGibhithe na, njalo i-Asiriya kayiyikubabusa na njengoba besala ukuphenduka?
“Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
6 Izinkemba zizaphazima emadolobheni abo, zizachitha imigoqo yamasango abo ziqede amacebo abo.
Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
7 Abantu bami bazimisele ukungihlamukela. Lanxa bekhuleka koPhezukonke kasoze abaphakamise.
Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
8 Ngingakukhalela kanjani, Efrayimi? Ngingakunikela kanjani, Israyeli? Ngingakuphatha kanjani njengo-Adima na? Ngingakwenza kanjani, njengoZebhoyimi na? Inhliziyo yami iguqukile phakathi kwami; isihawu sami sonke siqubukile.
“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
9 Kangiyikwenza okwentukuthelo yami eyesabekayo, kumbe ngiphenduke ngimqothule u-Efrayimi. Ngoba nginguNkulunkulu, hatshi umuntu, oNgcwele phakathi kwenu. Kangiyikuza ngolaka.
Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
10 Bazamlandela uThixo; uzabhonga njengesilwane. Lapho esebhonga, abantwana bakhe bazakuza beqhaqhazela bevela entshonalanga.
Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 Bazakuza bevela eGibhithe beqhaqhazela njengezinyoni bevela e-Asiriya bephaphazela njengamajuba. Ngizabahlalisa emakhaya abo,” kutsho uThixo.
Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
12 “U-Efrayimi usengizingeleze ngamanga, lendlu ka-Israyeli ngenkohliso. LoJuda uluhlaza kuNkulunkulu, kanye lakuye othembekileyo oNgcwele.”
Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.