< UGenesisi 32 >
1 UJakhobe laye wahamba ngeyakhe indlela, wasehlangabezwa yizingilosi zikaNkulunkulu.
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 Wathi ezibona uJakhobe wathi, “Leli libandla likaNkulunkulu!” Indawo leyo waseyibiza ngokuthi yiMahanayimi.
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 UJakhobe wathuma izithunywa ukuba zihambe phambili kwakhe kumnewabo u-Esawu elizweni laseSeyiri, ilizwe lika-Edomi.
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 Wazilaya wathi, “Nanku okumele likutsho enkosini yami u-Esawu, ‘Inceku yakho uJakhobe uthi bengihlezi loLabhani njalo ngihlale khona kwaze kwaba khathesi.
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 Ngilenkomo labobabhemi, ngilezimvu, lembuzi, njalo ngilezinceku lezincekukazi. Khathesi-ke sengithumela lelilizwi enkosini yami, ukuze ngithole umusa emehlweni akho.’”
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 Kwathi izithunywa sezibuya kuJakhobe zathi, “Sihambile kumfowenu u-Esawu, okwamanje uyeza ukuzokuhlangabeza, ulamadoda angamakhulu amane eza lawo.”
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 UJakhobe wafikelwa yikwesaba lokukhathazeka okukhulu wasesehlukanisa phakathi abantu ayelabo baba ngamaqembu amabili, wenzenjalo lemihlambini yezimvu leyenkomo lamakamela lawo.
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 Wakhumbula wathi, “Nxa u-Esawu angafika ahlasele elinye iqembu, leloqembu eliseleyo lingahle libaleke.”
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 UJakhobe wasekhuleka wathi, “Oh Nkulunkulu kababa u-Abhrahama, Nkulunkulu kababa u-Isaka, Thixo, wena owathi kimi, ‘Buyela elizweni lakini lasezihlotsheni zakho, ngizakwenza uphumelele,’
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 mina kangiwufanelanga wonke umusa lokuthembeka okutshengise inceku yakho. Ngangiphethe intonga yami zwi mhla ngichapha iJodani leli, kodwa khathesi sengingamaqembu amabili.
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 Ngiyakhuleka ngithi ngisindise esandleni somfowethu u-Esawu, ngoba ngiyesaba ukuthi uzakuza angihlasele, kanye labesifazane labantwababo.
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 Kodwa wena uthe, ‘Ngempela ngizakwenza uphumelele ngenze lezizukulwane zakho zibe njengetshebetshebe lolwandle elingeke labalwa.’”
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 Wahlala khonapho ngalobobusuku, kwathi kulokho ayelakho wakhetha isipho sikamnewabo u-Esawu:
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
14 imbuzikazi ezingamakhulu amabili lempongo ezingamatshumi amabili; izimvu ezinsikazi ezingamakhulu amabili lenqama ezingamatshumi amabili;
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
15 amakamela amasikazi angamatshumi amathathu lamathole awo; amankomokazi angamatshumi amane lenkunzi ezilitshumi; kanye labobabhemi abasikazi abangamatshumi amabili lemiduna yawo elitshumi.
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 Wakugcinisa izisebenzi zakhe konke, umhlambi munye wema wodwa, wathi kuzo izisebenzi zakhe, “Hambani phambi kwami, njalo litshiye ibanga phakathi kwemihlambi.”
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 Lowo owayephambili wamlaya wathi, “Nxa umnewethu u-Esawu ekuhlangabeza afike abuze athi, ‘Ungokabani wena, njalo uya ngaphi, njalo ngezikabani zonke lezizifuyo eziphambi kwakho?’
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 Ubokuthi, ‘Ngezenceku yakho uJakhobe. Ziyisipho esithunyelwe inkosi yami u-Esawu, laye uyeza nje emuva kwethu.’”
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 Walaya njalo isisebenzi sesibili, lesesithathu lazozonke ezinye ezaziqhuba imihlambi wathi: “Kumele likhulume into efanayo ku-Esawu nxa lihlangana laye.
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 Njalo lingakhohlwa ukuthi, ‘Inceku yakho uJakhobe iyeza ngemva kwethu.’” Ngoba wacabanga wathi: “Ngizamthoba ngezipho lezi engizithumela phambili; nxa sengimbona muva mhlawumbe uzangamukela.”
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
21 Ngakho izipho zikaJakhobe zahanjiswa, zamandulela, kodwa yena wasala ezihonqweni ubusuku bonke.
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 Ngalobobusuku uJakhobe waphakama wathatha omkakhe bobabili, lezincekukazi zakhe zombili kanye lamadodana akhe alitshumi lamunye wawela izibuko likaJabhoki.
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
23 Esebachaphisile wabuye wachaphisa yonke imfuyo yakhe.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 Ngakho uJakhobe wasala yedwa, indoda ethile yabindana laye kwaze kwaba semathathakusa.
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 Leyondoda yathi ngokubona ukuthi kayimehluli uJakhobe, yambamba inyonga, inyonga yakhe yakhumuka elokhu ebindana laleyondoda.
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 Indoda yasisithi, “Ngiyekela ngihambe ngoba sokusile.” Kodwa uJakhobe wamphendula wathi, “Kangisoze ngikwekele uhambe ngaphandle kokuthi ungibusise.”
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 Indoda yambuza yathi, “Ungubani ibizo lakho na?” Wathi, “NginguJakhobe.”
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 Indoda yasisithi, “Ibizo lakho kalisayikuba nguJakhobe, kodwa u-Israyeli, ngoba ulwe loNkulunkulu kanye labantu wanqoba.”
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 UJakhobe wathi, “Akungitshele ibizo lakho.” Kodwa waphendula wathi “Ulibuzelani ibizo lami na?” Wasembusisa khonapho.
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 Ngakho uJakhobe wabiza indawo leyo ngokuthi yiPheniyeli esithi, “Kungoba ngimbonile uNkulunkulu ubuso ngobuso, kodwa impilo yami kayilinyazwanga.”
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 Ilanga lamphumela esedlula ePheniweli, ehamba eqhugezela ngenxa yenyonga yakhe.
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 Ngakho-ke kuze kube lamuhla abako-Israyeli kabayidli inyama elomsipha osuka enyongeni, ngoba inyonga kaJakhobe yenyela eduze lomsipha.
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.