< UGenesisi 26 >

1 Kwasekusiba lendlala elizweni, ngaphandle kwendlala yakuqala eyayikhona ngesikhathi sika-Abhrahama, u-Isaka waya ku-Abhimelekhi inkosi yamaFilistiya eGerari.
Tsono kunagwa njala ina mʼdzikomo kuwonjezera pa ija ya poyamba ya nthawi ya Abrahamu ndipo Isake anapita kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.
2 UThixo wabonakala ku-Isaka wathi, “Ungehleli eGibhithe; hlala elizweni engithi hlala khona.
Yehova anadza kwa Isake nati, “Usapite ku Igupto; koma ukhale mʼdziko limene ndidzakuwuza kuti ukakhalemo.
3 Ake uhlale kulelilizwe okwesikhatshana, mina ngizakuba lawe ngikubusise. Ngoba wena lezizukulwane zakho ngizalinika wonke amazwe la njalo ngiqinise isifungo engasifunga kuyihlo u-Abhrahama.
Khala mʼdziko lino ndipo ndidzakhala nawe ndi kukudalitsa. Pakuti kwa iwe ndi zidzukulu zako ndidzapereka mayiko onsewa. Choncho ndidzakwaniritsa pangano limene ndinalumbira kwa Abrahamu, abambo ako.
4 Ngizakwenza izizukulwane zakho zibe zinengi njengezinkanyezi emkhathini, ngizinike wonke lamazwe, njalo kuthi ngenzalo yakho zonke izizwe emhlabeni zizabusiswa,
Zidzukulu zako ndidzazichulukitsa ngati nyenyezi za mu mlengalenga ndi kuzipatsa mayiko onsewa. Ndiponso anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako,
5 ngoba u-Abhrahama wangilalela, wagcina izimiso zami, lemilayo yami, kanye lemithetho yami.”
chifukwa Abrahamu anandimvera, nasunga malamulo anga onse.”
6 Ngakho u-Isaka wahlala eGerari.
Choncho Isake anakhala ku Gerari.
7 Kwathi lapho abantu baleyondawo bembuza ngomkakhe wathi, “Ngudadewethu,” ngoba wayesesaba ukuthi, “Ngumkami.” Wacabanga wathi, “Amadoda alapha angangibulala ngenxa kaRabheka, ngoba muhle kakhulu.”
Anthu akumaloko atafunsa Isake za mkazi wake, iye anati, “Ndi mlongo wanga ameneyu.” Iye anaopa kunena kuti, “Ndi mkazi wanga ameneyu,” popeza ankaganiza kuti anthu akumeneku akhoza kumupha ndi kukwatira mkazi wake popeza Rebeka anali wokongola.
8 Kwathi u-Isaka esehlale khona okwesikhathi eside, u-Abhimelekhi inkosi yamaFilistiya wakhangela ngefasitela wabona u-Isaka egone umkakhe uRabheka.
Isake atakhalako kumeneko nthawi yayitali, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anasuzumira pa zenera kuyangʼana kunja, ndipo anaona Isake akugwiragwira Rebeka, mkazi wake.
9 Ngakho wasebiza u-Isaka wathi, “Kanti ngumkakho ngeqiniso! Kungani uthe ungudadewenu?” U-Isaka wamphendula wathi, “Ngoba ngakhumbula ukuthi ngingalahlekelwa yimpilo yami ngenxa yakhe.”
Choncho Abimeleki anamuyitanitsa Isake nati, “Uyu ndi mkazi wako ndithu! Nanga bwanji umati, ‘Ndi mlongo wanga’?” Ndipo Isake anamuyankha kuti, “Ine ndimaganiza kuti ndingataye moyo wanga chifukwa cha iyeyu.”
10 U-Abhimelekhi wasesithi, “Kuyini lokhu okwenzileyo kithi? Omunye wamadoda ubezaqabuka elala laye umkakho, ubususibangela icala.”
Tsono Abimeleki anati, “Nʼchiyani chimene watichitira? Mmodzi mwa anthuwa anatsala pangʼono kugona ndi mkazi wako ndipo ukanatisandutsa ife kukhala olakwa.”
11 Ngakho u-Abhimelekhi wasekhupha umlayo ebantwini bonke wathi, “Lowo ozake ayithinte indoda le loba umkayo ngempela uzabulawa.”
Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”
12 U-Isaka walima amabele kulelolizwe, ngalowomnyaka wavuna okuphindwe ngekhulu, ngoba uThixo wambusisa.
Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa.
13 Umuntu lo wanotha kakhulu, lemfuyo yakhe yanda kakhulukazi.
Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri.
14 Waba lemihlambi yezimvu lenkomo emikhulu kakhulu, kanye lezisebenzi ezinengi, amaFilistiya aze aba lomona ngaye.
Anali ndi nkhosa, ngʼombe ndi antchito ambiri mwakuti Afilisti anamuchitira nsanje.
15 Kwasekusithi yonke imithombo eyayigejwe yizisebenzi ngesikhathi sikayise u-Abhrahama, amaFilistiya ayivala ngokuyigqibela ngenhlabathi.
Nthawi iyi nʼkuti Afilisti atakwirira ndi dothi zitsime zonse zimene antchito abambo ake Abrahamu anakumba mu nthawi ya abambo akewo.
16 U-Abhimelekhi wasesithi ku-Isaka, “Suka kithi; ususuke waba lamandla kakhulu kulathi.”
Ndipo Abimeleki anati kwa Isake, “Muchoke pakati pathu chifukwa mwasanduka wamphamvu kuposa ife.”
17 Ngakho u-Isaka wasuka lapho wayakuma eSigodini saseGerari, wahle wakha khona.
Choncho Isake anachokako kumeneko nakakhala ku chigwa cha Gerari kumene anakhazikikako.
18 U-Isaka wayiphanda imithombo eyayigejwe ngesikhathi sikayise u-Abhrahama, eyayigqitshelwe ngamaFilistiya ngemva kokuba u-Abhrahama esefile, wayibiza ngalawo mabizo uyise ayeyibiza ngawo.
Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.
19 Izisebenzi zika-Isaka zagebha esigodini zafumana umthombo olamanzi amahle khonapho.
Antchito a Isake anakumba mʼchigwamo ndipo anapezamo kasupe wa madzi.
20 Kodwa abelusi baseGerari baxabana labelusi baka-Isaka bathi, “Amanzi la ngawethu!” Ngakho umthombo lowo wawuthi yi-Eseki, ngoba bawubanga laye.
Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye.
21 Ngakho basebesimba omunye umthombo, kodwa lawo bawubanga njalo; wasewubiza ngokuthi yiSithina.
Kenaka iwo anakumba chitsime china, koma anakangananso chifukwa cha chitsimecho. Choncho anachitcha dzina lakuti Chidani.
22 Wasuka lapho wayagebha omunye umthombo, akwabe kusaba khona owubangayo. Wawuthi yiRehobhothi, esithi, “Manje uThixo usesiphile indawo, sesizaphumelela kuleli ilizwe.”
Anachokapo pamenepo nakakumba china. Koma apa sanakanganiranenso ndi munthu. Iye anachitcha Kutakasuka, nati, “Tsopano Yehova watipatsa ife malo otakasukirako ndipo tilemera muno.”
23 Esuka lapho waya eBherishebha.
Kenaka Isake anachoka ku malo kuja kupita ku Beeriseba.
24 Ngalobobusuku uThixo wabonakala kuye wathi, “NginguNkulunkulu kayihlo u-Abhrahama. Ungesabi, ngoba ngilawe; ngizakubusisa ngandise ubunengi bezizukulwane zakho ngenxa yenceku yami u-Abhrahama.”
Usiku umenewo Yehova anadza kwa Isake nati, “Ine ndine Mulungu wa abambo ako Abrahamu. Usachite mantha popeza Ine ndili ndi iwe. Ndidzakudalitsa ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri chifukwa cha mtumiki wanga Abrahamu.”
25 U-Isaka wakha i-Alithari khonapho wamemeza ibizo likaThixo. Wamisa ithente lakhe khonapho, izisebenzi zakhe zemba umthombo khonapho.
Isake anamanga guwa lansembe pamenepo ndipo anapembedza Yehova. Pomwepo anamanga tenti yake, ndipo antchito ake anakumba chitsime.
26 Ngalesosikhathi u-Abhimelekhi weza kuye evela eGerari, elo-Ahuzathi umeluleki wakhe loFikholi umlawuli wamabutho akhe.
Abimeleki pamodzi ndi Ahuzati mlangizi wake ndi Fikolo mkulu wa ankhondo ake anabwera kwa Isake kuchokera ku Gerari.
27 U-Isaka wababuza wathi, “Lilandeni kimi, njengoba lalingizonda laze langixotsha?”
Tsopano Isake anawafunsa kuti, “Bwanji mwabwera kwa ine, popeza munandichitira nkhanza ndi kundithamangitsa?”
28 Bamphendula bathi, “Sabona kamhlophe ukuthi uThixo wayelawe; yikho sasesicabanga ukuthi kumele kube lesivumelwano esibotshiweyo phakathi kwethu lawe. Kasenze isibopho lawe
Iwo anayankha, “Tsopano tadziwa kuti Yehova anali ndi iwe; ndiye taganiza kuti inu ndi ife tichite lumbiro. Ife tichite pangano ndi inu
29 esokuthi kawusoze usihlukuluze, njengoba lathi singazange sikulimaze ngalutho kodwa sakuvalelisa ngokuthula. Khathesi usubusisiwe nguThixo.”
kuti inu simudzatichitira zoyipa monga ifenso sitinakuchitireni nkhondo. Ife tinakuchitirani zabwino zokhazokha, ndipo tinakulolani kuti musamuke kuchoka kwathu mu mtendere. Tsopano Yehova wakudalitsani.”
30 U-Isaka wasebenzela idili, badla banatha.
Tsono Isake anawakonzera phwando, ndipo anadya ndi kumwa.
31 Ekuseni kakhulu ngelanga elilandelayo amadoda wonke enza isifungo omunye komunye. U-Isaka wasebavulela indlela bahamba ngokuthula.
Mmawa wake aliyense analumbira pangano kwa mnzake. Tsono Isake anawalola kuti anyamuke ndipo anamusiya mu mtendere.
32 Ngalolosuku izisebenzi zika-Isaka zabuya zamtshela ngomthombo ezaziwugebhile. Zathi, “Sesiwatholile amanzi!”
Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!”
33 Wawuthi yiShibha, osekuze kube namuhla idolobho kuthiwa yiBherishebha.
Iye chitsimecho anachitcha Pangano. Nʼchifukwa chake mzindawu umatchedwa Beeriseba mpaka lero.
34 Kwathi u-Esawu eseleminyaka yobudala engamatshumi amane, wathatha uJudithi indodakazi kaBheri umHithi njalo loBhasemathi indodakazi ka-Eloni umHithi.
Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti.
35 Baletha ukukhathazeka kakhulu ku-Isaka loRabheka.
Akazi awiriwa anasandutsa Isake ndi Rebeka kukhala ndi moyo wa madandawulo nthawi zonse.

< UGenesisi 26 >