< UHezekheli 4 >
1 “Khathesi-ke, ndodana yomuntu, thatha umcephe webumba uwubeke phambi kwakho, udwebe kuwo idolobho laseJerusalema.
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 Dweba ukuvinjezelwa kwalo: Misa izindawo zokuvinjezelwa kwalo, yakha umthezuko ngaphezu kwalo, misa inkamba zokulihlasela uphinde ulihonqolozele ngezigodo zokubhidliza.
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 Emva kwalokho thatha umganu wensimbi, uwubeke unjengomduli wensimbi phakathi kwakho lomuzi ube usuphendulela ubuso bakho kuwo. Wena ukhangele ngakuwo umuzi, umuzi ube ngovinjezelweyo, wena ube ngumvimbezeli. Lokhu kuzakuba yisibonakaliso endlini ka-Israyeli.
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 Emva kwalokho lala ngomhlubulo wenxele, ubeke isono sendlu ka-Israyeli phezu kwakho. Kumele uthwale isono sabo okwalezonsuku ulele ngomhlubulo wakho.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5 Sengikumisele inani linye lezinsuku njengeminyaka yezono zabo. Ngakho izono zendlu ka-Israyeli uzazithwala okwensuku ezingamakhulu amathathu lamatshumi ayisificamunwemunye.
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 Emva kokuba usuqede lokhu, lala phansi futhi, khathesi kube ngomhlubulo wakho wokunene, uthwale isono sendlu kaJuda. Ngikumisele insuku ezingamatshumi amane, usuku olulodwa lumele umnyaka munye ngamunye.
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 Phendulela ubuso bakho ekuvinjezelweni kweJerusalema kuthi izingalo zakho zingembeswanga uphrofithe kubi ngeJerusalema.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 Ngizakubopha ngentambo ukuze ungatshibiliki usuka kwelinye icele usiya kwelinye uze uqede insuku zokuvinjezelwa kwakho.
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 Thatha ingqoloyi lebhali, indumba lelentili, inyawuthi lophoko; ukubeke embizeni yokugcinela ukusebenzise ekwenzeni ukudla kwakho. Kumele ukudle phakathi kwensuku ezingamakhulu amathathu lamatshumi ayisificamunwemunye ulele ngomhlubulo wakho.
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 Linganisa amashekeli angamatshumi amabili okudla ozakudla usuku ngalunye njalo ukudle ngezikhathi ezimisiweyo.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 Njalo linganisa okukodwa kwesithupha kwehini lamanzi uwanathe ngezikhathi ezimisiweyo.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 Dlana ukudla njengalapho usidla ikhekhe lebhali, ukupheke abantu bekhangele, inkuni zakho kube ngamalongwe abantu.”
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 UThixo wathi, “Ngokunjalo abantu bako-Israyeli bazakudla ukudla okungcolileyo phakathi kwezizwe engizabaxotshela kuzo.”
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 Lapho-ke mina ngathi, “Akunjalo, Thixo Wobukhosi. Angikaze ngizingcolise. Kusukela ebutsheni bami kuze kube khathesi angikaze ngidle loba yini etholakale ifile kumbe edlithizwe yizinyamazana. Akulanyama engcolileyo eseyake yangena emlonyeni wami.”
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 Wasesithi, “Kulungile. Ngizakuvumela ukuba upheke isinkwa sakho ngamalongwe enkomo esikhundleni samalongwe abantu.”
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 Waphinda wathi kimi, “Ndodana yomuntu, ngizavala ukungeniswa kokudla eJerusalema. Abantu bazakudla ukudla kokwabelwa benqineka, banathe lamanzi okwabelwa bengelathemba,
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 ngoba ukudla lamanzi kuzakuba yingcosana. Bazakwethuka lapho bebonana, njalo bazacikizeka ngenxa yezono zabo.”
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”