< UHezekheli 38 >
1 Ilizwi likaThixo lafika kimi lisithi:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Ndodana yomuntu, khangelisa ubuso bakho bumelane loGogi, owaselizweni laseMagogi, inkosana enkulu yaseMesheki kanye laseThubhali; phrofetha kubi ngaye
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 uthi: ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Ngimelana lawe, wena Gogi, nkosana enkulu yaseMesheki kanye laseThubhali.
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Ngizakutshibilikisa, ngifake amawuka emihlathini yakho ngikukhuphe lebutho lakho lonke, amabhiza akho, abagadi bamabhiza bakho behlome bephelele, lexuku elikhulukazi lilamahawu amancane lamakhulu, bonke benyikinya izinkemba zabo.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 IPhezhiya, leKhushi kanye lePhuthi bazakuba belabo, bonke belamahawu lezingowane,
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 njalo leGomeri lamabutho ayo wonke, kanye leBhethi Thogarima ivela khatshana enyakatho lamabutho ayo wonke, izizwe ezinengi ezilawe.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Lunga; zilungisele, wena kanye lamaxuku wonke abuthene emaceleni akho wonke, uwalawule.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Emva kwensuku ezinengi uzabizelwa empini. Eminyakeni ezayo uzahlasela ilizwe eselisindile empini, elilabantu balo ababuthwa ezizweni ezinengi basiwa ezintabeni zako-Israyeli ezaziphundlekile okwesikhathi eside. Babekhutshiwe ezizweni, khathesi bonke bahlezi ekuvikelekeni.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Wena lamabutho akho wonke kanye lezizwe ezinengi ezilawe lizakuya khonale, liqhubeka njengesiphepho; lizakuba njengeyezi lisibekele ilizwe.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Lokhu yikho okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Ngalolosuku kuzafika imicabango engqondweni yakho njalo uzaceba isu elibi.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Uzakuthi, “Ngizahlasela ilizwe elilemizi engelamithangala; ngizahlasela abantu abalokuthula abanganakaneli lutho, bonke abahlezi bengelamithangala njalo bengelamasango lemigoqo.
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Ngizaphanga njalo ngithumbe ngiphinde ngiguqulele isandla sami ekumeleni amanxiwa asahlaliswa abantu lasebantwini abaqoqwa ezizweni, abalezifuyo ezinengi lempahla, abahlala enkabeni yelizwe.”
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 IShebha leDedani kanye labathengisi bonke baseThashishi lemizi yalo yonke bazakuthi kuwe, “Lande ukuzaphanga na? Uqoqe amaxuku akho ukuba uthumbe, uthathe isiliva legolide, uthathe izifuyo kanye lempahla njalo uthumbe impango enengi na?”’
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Ngakho, ndodana yomuntu, phrofetha uthi kuGogi: ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Ngalolosuku, lapho abantu bami u-Israyeli sebehlala ekuvikelweni, kawuyikukubona na?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 Uzakuza uvela endaweni yakho khatshana le enyakatho, wena kanye lezizwe ezinengi ezilawe, zonke zigade amabhiza, ixuku elikhulukazi, ibutho elilamandla.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Uzaqhubeka umelana labantu bami u-Israyeli njengeyezi elisibekele ilizwe. Ensukwini ezizayo, wena Gogi, ngizakwenza umelane lelizwe lami, ukuze izizwe zingazi lapho sengizibonakalisa ngingcwele ngawe phambi kwazo.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Kanti kawusuwe yini engakhuluma ngawe ensukwini zakudala ngezinceku zami abaphrofethi bako-Israyeli na? Ngalesosikhathi baphrofetha iminyaka eminengi ukuthi ngangizakwenza umelane labo.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Nanku okuzakwenzakala ngalolosuku: Lapho uGogi esehlasela ilizwe lako-Israyeli ulaka lwami oluvuthayo luzavuka, kutsho uThixo Wobukhosi.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Ngokutshiseka kwami langolaka lwami oluvuthayo ngithi ngalesosikhathi kuzakuba lokuzamazama komhlaba okukhulu elizweni lako-Israyeli.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Inhlanzi zasolwandle, izinyoni zasemoyeni, izinyamazana zeganga, zonke izidalwa ezihamba phansi, labantu bonke abasemhlabeni kuzathuthumela ngokuba khona kwami. Izintaba zizagenqulwa, amawa azabhidlika njalo lemiduli yonke izawela phansi.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Ngizalaya inkemba imelane loGogi kuzozonke izintaba zami, kutsho uThixo Wobukhosi. Inkemba yomuntu ngamunye izamelana lomfowabo.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 Ngizamahlulela ngesifo langokuchithwa kwegazi; ngizathululela phansi izihlambi zezulu, isiqhotho lesolufa etshisayo phezu kwakhe laphezu kwamabutho akhe kanye laphezu kwezizwe ezinengi ezilaye.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Ngalokho ngizabonakalisa ubukhulu bami lobungcwele bami, njalo ngizakwenza ngazakale phambi kwezizwe ezinengi. Lapho-ke bazakwazi ukuthi mina nginguThixo.’”
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”