< U-Eksodusi 2 >

1 Kwasekusithi eyinye indoda esizweni sakoLevi yathatha owesifazane ongumLevi,
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 wazithwala wabeletha indodana. Wabona ukuthi umntwana wayemuhle kakhulu, wasemfihla okwezinyanga ezintathu.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 Kodwa kwathi lapho sekusehlula ukuthi amfihle, wenza isitsha semizi, wasibhada ngodaka lengcino. Wafaka umntwana phakathi kwaso wayasibeka okhunjini lomfula uNayili phakathi kwemihlanga.
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 Udadewabo wema bucwala ukuba abone okwenzakala kuye.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 Indodakazi kaFaro yehlela emfuleni ukuyageza, amantombazana ayikhangelayo ayehamba okhunjini lomfula. Yasisibona isitsha phakathi kwemihlanga yathuma incekukazi yayo ukuyasithatha.
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 Yasivula yambona umntwana. Wayekhala, yasimzwela usizi yathi, “Lo ngomunye wabantwana bamaHebheru.”
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 Udadewabo wasesithi endodakazini kaFaro, “Ngingayakudingela omunye wabesifazane bamaHebheru ukuthi akondlele umntwana na?”
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 Yasisithi, “Yebo, hamba.” Intombazana yasuka yayabiza unina womntwana.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 Indodakazi kaFaro yathi kuye, “Mthathe lumntwana ungondlele yena, ngizakupha isondlo.” Ngakho owesifazane wamthatha umntwana wamondla.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 Esekhulile umntwana, wamthatha wamusa endodakazini kaFaro wasesiba ngumntanayo. Yasimutha ibizo yathi nguMosi ngoba yathi, “Ngamkhupha emanzini.”
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 Ngelinye ilanga, uMosi esekhulile, waya lapho okwakusebenzela khona abantu bakibo, wabona ukuthi babethwele nzima kanjani. Wabona umGibhithe etshaya umHebheru, omunye wabantu bakibo.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 Wathi thala ngapha langapha wabona kungelamuntu, wasebulala umGibhithe wamfihla etshebetshebeni.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 Ngelanga elilandelayo waphuma njalo wabona amaHebheru amabili esilwa. Wasebuza lo owayephambanisile wathi, “Kungani utshaya owakini ongumHebheru na?”
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 Indoda leyo yathi, “Ngubani okwenze waba ngumbusi lomahluleli wethu? Usucabanga ukungibulala na njengoba ubulele umGibhithe?” Ngalokho uMosi wesaba wacabanga ukuthi, “Engxenye engikwenzileyo sekusazakala.”
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 Kwathi uFaro ekuzwa lokho, wazama ukubulala uMosi, kodwa uMosi wabalekela eMidiyani, lapho afika khona wahlala phansi eduze komthombo.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 Umphristi waseMidiyani wayelamadodakazi ayisikhombisa, afika ezokukha amanzi lokukhelela imikolo ukuze anathise izimvu zikayise.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 Kwafika abelusi abathile bawaxotsha, kodwa uMosi wasukuma wawalamulela wanathisa izimvu zawo.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 Kwathi izintombi sezibuyele kuyise eRuweli wazibuza esithi, “Kungani lamhla liphangisile ukuphenduka?”
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 Zaphendula zathi, “KulomGibhithe osilamulele kubelusi. Uze wasikhelela amanzi wanathisa lezimvu zethu.”
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 Wawabuza amadodakazi akhe wathi, “Ungaphi? Limtshiyeleni? Mbizeni ukuze azothola okokudla.”
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 UMosi wavuma ukuzehlala lale indoda, eyamnika indodakazi yayo uZiphora ukuthi abe ngumkakhe.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 UZiphora wazala indodana, uMosi wayitha ibizo wathi nguGeshomu ngoba esithi, “Sengibe ngumuntu wezizweni endaweni yabezizweni.”
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 Emva kwesikhathi eside, inkosi yaseGibhithe yafa. Abako-Israyeli bakhala babubula ebugqilini babo, kwasekusithi ukukhala kwabo becela usizo ngenxa yobugqili ababekubo kwafinyelela kuNkulunkulu.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 UNkulunkulu wakuzwa ukububula kwabo wasekhumbula isivumelwano asenza lo-Abhrahama, lo-Isaka loJakhobe.
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 Ngakho uNkulunkulu wakhangela abako-Israyeli, wakhathazeka ngabo.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

< U-Eksodusi 2 >