< U-Esta 1 >
1 Lokhu yikho okwenzakala ngesikhathi sika-Ahasuweru, owayebusa izifunda ezingaphezu kwekhulu elilamatshumi amabili lasikhombisa kusukela e-Indiya kuze kuyefika eTopiya.
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 Ngalesosikhathi inkosi u-Ahasuweru wayebusa esesigodlweni saseSusa,
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 kwathi ngomnyaka wesithathu wokubusa kwakhe, wenzela izikhulu zakhe kanye leziphathamandla zakhe idili elikhulu. Abakhokheli bebutho basePhezhiya labaseMediya, amakhosana, kanye lezikhulu zezifunda zonke zazikhona.
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 Okwensuku ezilikhulu lamatshumi ayisificaminwembili watshengisa ubukhulu benotho yombuso wakhe kanye lobucwazicwazi lobukhosi bombuso wakhe.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 Kwathi lezonsuku seziphelile, inkosi yenza idili elikhulu elabakhona okwensuku eziyisikhombisa, endaweni ehonqolozelweyo esigodlweni senkosi, lisenzelwa bonke abantu abaziwayo labantukazana ababesesigodlweni saseSusa.
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 Egumeni kwakulezilengiso ezimhlophe leziluhlaza okwesibhakabhaka, zibotshelwe emasongweni esiliva ngentambo zelineni elimhlophe lelembu eliyibubende ensikeni zamatshe aqinileyo. Kwakulemibheda yegolide lesiliva phezu kwephansi elaligandelwe ngamatshe aligugu, abomvu, aluhlaza, amhlophe lamnyama lamanye adulayo.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 Iwayini lalinathelwa ezinkezweni zegolide, inye ngayinye yehlukene kwezinye, njalo iwayini lesikhosini lalilinengi, kutshengisa ukukhululeka kwesandla senkosi.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 Ngokulaya kwenkosi, isethekeli sinye ngasinye sasikhululekile ukuthi sinathe ngokwentando yaso, ngoba inkosi yayilaye zonke iziphathamandla ezazisipha iwayini ukuthi ziphe umuntu wonke njengokufisa kwakhe.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 INdlovukazi uVashithi layo yenzela abesifazane ababesesigodlweni seNkosi u-Ahasuweru idili elikhulu.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 Ngelanga lesikhombisa, inkosi u-Ahasuweru isidakiwe ngenxa yewayini, yalaya abathenwa abayisikhombisa ababeyisebenzela, uMehumani, uBhizitha, uHaribhona, uBhigitha, u-Abhagitha, uZethari loKharikhasi,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
11 ukuthi balethe kuyo iNdlovukazi uVashithi ethwele umqhele wakhe wobukhosi ukuze abukise ubuhle bakhe ebantwini kanye lezikhulwini, ngoba wayemuhle kakhulu.
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Kodwa kwathi abathenwa beyitshela ngokulaya kwenkosi, iNdlovukazi uVashithi yala ukuya. Ngakho inkosi yathukuthela yavutha ngolaka.
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 Njengoba kwakuyinjwayelo ukuthi inkosi icebisane lezingcitshi ezindabeni eziphathelene lemithetho kanye lokwahlulela, yakhuluma lamadoda ahlakaniphileyo ayezwisisa ngomumo walezozikhathi
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 njalo ayeseduzane kakhulu lenkosi kwakunguKharishena, uShethari, u-Adimatha, uThashishi, uMeresi, uMarisena loMemukhani, izikhulu eziyisikhombisa zasePhezhiya laseMediya ezazilemvumo yokuya enkosini njalo zilezikhundla eziphakemeyo embusweni.
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 Yasibuza yathi, “Umthetho uthi kwenziweni eNdlovukazini uVashithi? Phela kayilalelanga umlayo wenkosi u-Ahasuweru awuthumele kuyo ngabathenwa.”
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 UMemukhani wasephendula phambi kwenkosi kanye lezikhulu zayo wathi, “INdlovukazi uVashithi yonile, hatshi enkosini kuphela, kodwa lasezikhulwini zonke kanye labantu bonke bezabelo zonke zeNkosi u-Ahasuweru.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Phela isenzo seNdlovukazi sizakwazakala kuwo wonke amakhosikazi, abesedelela omkawo esithi, ‘Inkosi u-Ahasuweru yalaya iNdlovukazi uVashithi ukuthi ilethwe phambi kwayo, kodwa yala ukuza.’
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 Lamhlanje amakhosikazi aphakemeyo asePhezhiya kanye laseMediya asizwileyo isenzo seNdlovukazi azaphendula izikhulu zenkosi zonke ngendlela efananayo. Kuzakuba khona ukungahloniphi kanye lengxabangxoza.
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Ngakho-ke, nxa kulungile enkosini, kakube lomthetho ozaphuma esigodlweni njalo ulotshwe emithethweni yelizwe lePhezhiya leMediya, ongeke uguqulwe njalo, ukuthi uVashithi akumelanga aphinde angene lapho okulenkosi u-Ahasuweru. Njalo inkosi kayiphe isikhundla sayo sobundlovukazi komunye ongcono kulayo.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 Kuzakuthi nxa umthetho wenkosi umenyezelwa kuwo wonke umbuso wayo omkhulu, abesifazane bonke bazahlonipha omkabo kusukela komncane kusiya komkhulu.”
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 Inkosi kanye lezikhulu zayo bathokoza ngalokhu kucebisa, inkosi yasisenza khona lokho uMemukhani akucebisayo.
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 Yathumela izincwadi kuzozonke izabelo zombuso, kuleso laleso sabelo incwadi yaso ngolimi olukhulunywa kuso, kwamenyezelwa ngendimi zazo ukuthi yileyo laleyo ndoda kumele ibuse umuzi wayo.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.