< UmTshumayeli 3 >
1 Zonke izinto zilesikhathi sazo, konke okwenziwayo ngaphansi kwelanga kulesibanga sakho:
Chinthu chilichonse chili ndi nthawi yake, ndi nyengo yake yomwe anayika Mulungu:
2 isikhathi sokuzalwa lesikhathi sokufa, isikhathi sokuhlanyela lesikhathi sokusiphuna,
Nthawi yobadwa ndi nthawi yomwalira, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola.
3 isikhathi sokubulala lesikhathi sokuphilisa, isikhathi sokubhidliza lesikhathi sokwakha,
Nthawi yakupha ndi nthawi yochiritsa, nthawi yogwetsa ndi nthawi yomanga.
4 isikhathi sokukhala lesikhathi sokuhleka, isikhathi sokulila lesikhathi sokugida,
Nthawi yomva chisoni ndi nthawi yosangalala, nthawi yolira maliro ndi nthawi yovina.
5 isikhathi sokuchithiza amatshe lesikhathi sokuwabutha, isikhathi sokugona lesikhathi sokunina,
Nthawi yotaya miyala ndi nthawi yokundika miyala, nthawi yokumbatirana ndi nthawi yoleka kukumbatirana.
6 isikhathi sokudinga lesikhathi sokukhalala, isikhathi sokugcina lesikhathi sokulahla,
Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna, nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.
7 isikhathi sokudabula lesikhathi sokuthunga, isikhathi sokuthula lesikhathi sokukhuluma,
Nthawi yongʼamba ndi nthawi yosoka, nthawi yokhala chete ndi nthawi yoyankhula.
8 isikhathi sokuthanda lesikhathi sokuzonda, isikhathi sempi lesikhathi sokuthula.
Nthawi yokondana ndi nthawi yodana, nthawi ya nkhondo ndi nthawi ya mtendere.
9 Umuntu osebenzayo uzuzani na ngokusadalala kwakhe?
Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa?
10 Sengiwubonile umthwalo uNkulunkulu awethese abantu.
Ine ndinaona chipsinjo chimene Mulungu anayika pa anthu.
11 Yonke into uyenze yabanhle ngesikhathi sayo. Wamupha umuntu iphakade enhliziyweni yakhe; kodwa abantu bangeke bafinyelele kulokho uNkulunkulu asakwenzayo kwasekuqaleni kusiya ekupheleni.
Iye anapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthawi yake. Anayika nzeru zamuyaya mʼmitima ya anthu; komabe anthuwo sangathe kuzindikira zomwe Mulungu wachita kuyambira pa chiyambi mpaka chimaliziro.
12 Ngiyakwazi ukuthi kakukho okungcono ebantwini kulokuthi bajabule njalo benze okuhle besaphila.
Ine ndikudziwa kuti palibenso kanthu kabwino kwa anthu kopambana kusangalala ndi kuchita zabwino pamene ali ndi moyo.
13 Ukuthi wonke umuntu adle, anathe asuthiseke ekusebenzeni kwakhe gadalala, lokhu kuyisipho sikaNkulunkulu.
Ndi mphatso ya Mulungu kwa munthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ndi ntchito zake zolemetsa.
14 Ngiyazi yonke into eyenziwa nguNkulunkulu izakuba khona kokuphela; akulalutho olungengezwa kukho loba kususwe kukho. UNkulunkulu uyenza lokho ukuze abantu bamkhonze.
Ndikudziwa kuti chilichonse chimene Mulungu amachita chidzakhala mpaka muyaya; palibe zimene zingawonjezedwe kapena kuchotsedwa. Mulungu amazichita kuti anthu azimuopa.
15 Loba yini ekhona seyake yaba khona, kulalokho okuzakuba khona sekwaba khona ngaphambili; njalo uNkulunkulu uzakubalisa okwedlulayo.
Chilichonse chimene chilipo chinalipo kale, ndipo chimene chidzakhalapo chinalipo poyamba; Mulungu amabwezanso zakale zimene zinapita kuti zichitikenso.
16 Njalo ngabona okunye ngaphansi kwelanga: endaweni yokwahlulela, ububi babukhona, endaweni yokulungisa, ububi babukhona.
Ndipo ndinaona chinthu chinanso pansi pano: ku malo achiweruzo, kuyipa mtima kuli komweko, ku malo achilungamo, kuyipa mtima kuli komweko.
17 Ngacabanga ngenhliziyo yami, “UNkulunkulu uzabehlulela bonke abalungileyo lababi, ngoba sizaba khona isikhathi sezenzakalo zonke, isikhathi sawo wonke umsebenzi.”
Ndinalingalira mu mtima mwanga kuti; “Mulungu adzaweruza olungama pamodzi ndi oyipa omwe, pakuti anayika nthawi yochitikira chinthu chilichonse, nthawi ya ntchito iliyonse.”
18 Ngacabanga njalo ngathi, “UNkulunkulu uyabahlola abantu ukuze babone ukuthi banjengezinyamazana.
Ndinalingaliranso kuti, “Kunena za anthu, Mulungu amawayesa ndi cholinga choti awaonetse kuti iwo ali ngati nyama.
19 Isiphetho somuntu siyafana lesezinyamazana; isiphetho sinye sibalindele bonke: njengoba lokhu kuyafa, kanjalo lokunye kuyafa. Konke kokubili kulomphefumulo munye; umuntu kangcono kulenyamazana. Konke kuyize.
Zimene zimachitikira munthu, zomwezonso zimachitikira nyama; chinthu chimodzi chomwecho chimachitikira onse: Monga munthu amafa momwemonso nyama imafa. Zonsezi zimapuma mpweya umodzimodzi omwewo; munthu saposa nyama. Zonsezi ndi zopandapake.
20 Konke kuya ndawo yinye; konke kuvela othulini, yikho konke kubuyela othulini.
Zonse zimapita kumodzimodzi; zonsezi zimachokera ku fumbi, ndipo zimabwereranso ku fumbi komweko.
21 Ngubani owaziyo ingabe umphefumulo womuntu uyakhwela uye phezulu kuthi owenyamazana wehlele phansi phakathi emhlabathini?”
Kodi ndani amene amadziwa ngati mzimu wa munthu umakwera kumwamba, ndipo mzimu wa nyama umatsikira kunsi kwa dziko?”
22 Yikho ngabona ukuthi kakukho okungcono emuntwini ngaphandle kokuthi akholise umsebenzi wakhe ngoba leso yiso isabelo sakhe. Ngoba kambe ngubani ongamenza ukuthi abone lokho okuzakwenzakala yena esedlule?
Kotero ndinaona kuti palibe chinthu chabwino kwa munthu kuposa kuti munthu azisangalala ndi ntchito yake, pakuti ichi ndiye chake chenicheni. Pakuti ndani amene angamubweretse kuti adzaone zimene zidzamuchitikira iye akadzamwalira?