< UDutheronomi 34 >

1 UMosi wasekhwela eNtabeni yaseNebho evelela emagcekeni eMowabi esiya phezu kwePhisiga, ngaphetsheya malungana leJerikho. Kukhonale uThixo amtshengisa khona ilizwe lonke, kusukela eGiliyadi kusiya kwelikaDani,
Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
2 lonke elikaNafithali, ilizwe lika-Efrayimi lelikaManase, lonke ilizwe likaJuda kusiyafika olwandle olungentshonalanga,
Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
3 iNegebi kanye lomhlaba wonke osuka eSigodini seJerikho, iDolobho laMalala, kusiya kude khonale eZowari.
Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
4 Ngakho uThixo wathi kuye, “Leli yilo ilizwe engathembisa ngesifungo u-Abhrahama, u-Isaka loJakhobe, lapho engathi khona, ‘Ngizalinika izizukulwane zenu.’ Ngikuvumele ukuthi ulibone ngawakho amehlo, kodwa awusoze uchaphele kulo.”
Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
5 Ngakho uMosi inceku kaThixo wafela khonapho kwelamaMowabi, njengokwakutshiwo nguThixo.
Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
6 Wamngcwaba eMowabi, esigodini esikhangelene leBhethi-Pheyori, kodwa kuze kube lamuhla lokhu kakho loyedwa olaziyo ingcwaba lakhe.
Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
7 UMosi wayeseleminyaka elikhulu lamatshumi amabili ekufeni kwakhe, ikanti amehlo akhe ayesabona kuhle njalo engakaphelelwa ngamandla.
Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
8 Abako-Israyeli bamlilela uMosi emagcekeni aseMowabi okwensuku ezingamatshumi amathathu, kwaze kwedlula insuku zokukhala lokulila.
Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
9 UJoshuwa indodana kaNuni wayegcwele umoya wokuhlakanipha ngoba uMosi wayembeke izandla. Ngakho abako-Israyeli bamlalela njalo benza lokho uThixo ayekulaye uMosi.
Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
10 Kusukela lapho, kakukabi lomunye njalo umphrofethi ko-Israyeli onjengoMosi, owayesaziwa nguThixo ubuso ngobuso,
Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
11 owenza zonke lezozimanga lezibonakaliso ayethunywe nguThixo ukuba ayezenza eGibhithe, kuFaro lakuzo zonke izikhulu zakhe lakulo lonke ilizwe lakhe.
Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
12 Ngoba kakho oyake atshengisele amandla amakhulu kangako loba ukwenza izenzo ezesabekayo uMosi azenzayo emehlweni abo bonke abako-Israyeli.
Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.

< UDutheronomi 34 >