< UDutheronomi 32 >

1 “Lalelani, we mazulu, ngizakhuluma, zwana, we mhlaba, amazwi omlomo wami.
Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 Akuthi imfundiso yami inethe njengezulu kuthi amazwi ami ehle njengamazolo, njengemifefezo etshanini obutsha, njengezulu elinengi phezu kwamahlumela.
Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 Ngizaliphakamisa ibizo likaThixo. Yebo dumisani ubukhulu bukaNkulunkulu wethu!
Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 UliDwala, imisebenzi yakhe iphelele, njalo zonke izindlela zakhe zilungile. UNkulunkulu othembekileyo ongenzi okubi, uqotho njalo ulungile yena.
Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 Sebenze okubi phambi kwakhe; balihlazo kabase bantwabakhe, kodwa isizukulwane esixhwalileyo lesingaqondanga.
Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 Yiyonale na indlela yokubonga kwenu uThixo, lina ziwula zabantu abangelakuhlakanipha? KasuYihlo, uMdali wenu, owalenzayo njalo owalibumbayo na?
Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Khumbulani insuku zakudala; likhumbule izizukulwane zasendulo. Buza uyihlo yena uzakutshela, abadala benu, njalo bazakuchasisela.
Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Kwathi oPhezukonke esephe izizwe ilifa lazo, eselwahlukanisile uluntu, walufakela imingcele, kusiya ngenani lamadodana ka-Israyeli.
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Ngoba isabelo sikaThixo ngabantu bakhe, uJakhobe yisabelo sakhe esikhethiweyo.
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Wamfica elizweni eliyinkangala, indawo engatheli lutho njalo elodlame. Wamvikela, wamonga; wamsingatha njengegugu lakhe,
Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 njengokhozi lunyakazisa isidleke salo, beselundiza phezu kwamachwane alo, lwelule amaphiko alo ukuwagola, luwathwale ngamaphiko alo.
ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Nguye yedwa uThixo owamkhokhelayo; kungekho unkulunkulu wezizweni owayelaye.
Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Wamkhweza engqongeni yelizwe wamondla ngezithelo zeganga. Wamondla ngoluju olwaluvela edwaleni, langamafutha aphuma ezingoxweni zeliwa,
Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 lezankefu langochago oluvela emihlambini yenkomo leyezimvu; lamazinyane anonisiweyo ezimvu lembuzi, lenqama zekhethelo zaseBhashani, kanye lengqoloyi elezinhlamvu ezinhle. Wanatha igazi eliphuphumayo lesithelo samavini.
pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 UJeshuruni wazimuka watshakala; esesuthi ukudla, wakhuluphala waba butshelezi. Wamlahla uNkulunkulu owamdalayo waliphika iDwala uMsindisi wakhe.
Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Bambangela ubukhwele ngabonkulunkulu babo bezizweni bamthukuthelisa ngezithombe zabo ezinengekayo.
Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Benza imihlatshelo kuwo amadimoni, wona angasiNkulunkulu, onkulunkulu ababengazange babazi, onkulunkulu ababesanda kuvela, onkulunkulu ababengakhonzwa ngoyihlo.
Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Walihlamukela iDwala, elinguyihlo; wakhohlwa uNkulunkulu owakuzalayo.
Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
19 UThixo wakubona lokhu wabafulathela ngoba wathukutheliswa ngamadodana lamadodakazi akhe.
Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
20 ‘Ngizabufihla ubuso bami kubo,’ watsho uThixo, ‘ngize ngibone ukuthi bazaphetha ngani; ngoba bayisizukulwana esixhwalileyo abantwana abangathembekanga.
Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
21 Bangenza ngaba lobukhwele ngalokho okwakungasinkulunkulu njalo bangithukuthelisa ngezithombe zabo ezingasizi lutho. Ngizabavusela umhawu ngesizwe esingesibantu balutho; ngibazondise ngesizwe esingazwisisiyo.
Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
22 Ngoba umlilo usulunyathiswe yikuthukuthela kwami, wona otshisa ujule uze uyethinta ukufa ngaphansi. Uzahangula udle umhlaba kanye lesivuno sawo uthungele lezinsika zezintaba. (Sheol h7585)
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
23 Ngizabehlisela izigigaba, imitshoko yami iphelele phezu kwabo.
“Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
24 Ngizabathumela inkengane eqeda amandla, izifo ezibhubhisayo lomkhuhlane otshabalalisayo; ngizabathumela amazinyo abukhali ezinyamazana zeganga, ubuthi bezinhlangwana ezihuquzelayo emhlabathini.
Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
25 Ezindleleni inkemba izabaswelisa abantwana, emizini kuzabusa uchuku. Amadodana lamadodakazi azabhujiswa aphele, abantwana abancinyane kanye lamadoda alenwele ezimhlophe.
Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
26 Ngithe ngizabachitha ngisuse imbali yabo bakhohlakale emhlabeni,
Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
27 kodwa ngesaba ukweyisa kwesitha, funa isitha singezwisisi besesisithi, “Isandla sethu sinqobile, njalo uThixo kakwenzanga konke lokhu.”’
koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
28 Bayisizwe esingelangqondo, akukho ukuqedisisa kubo.
Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
29 Ngabe kodwa bahlakaniphile njalo bezwisise lokhu, babe lokuqedisisa ukuthi sizakuba yini isiphetho sabo!
Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
30 Kungenzeka njani ukuthi umuntu oyedwa axotshane lenkulungwane, loba ababili basukele izinkulungwane ezilitshumi zibaleke na, ngaphandle kokuthi iDwala labo nxa labathengisa; langaphandle kokuthi uThixo wabo esebahlanekele?
Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
31 Ngoba elabo idwala alinjengelethu iDwala, njengoba lezitha zethu zivuma.
Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
32 Iwayini labo livela esivinini saseSodoma lasemasimini aseGomora. Amagrebisi abo agcwele itshefu, lamaxha awo amunyu.
Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
33 Iwayini labo liyibuthi bezinyoka, ubuhlungu obubulalayo bezinhlangwana.
Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
34 ‘Kambe lokhu angikugodlanga na ngakugcikela eziphaleni zami na?
“Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
35 Ukuphindisela ngokwami; ngizabuyisela. Ngesikhathi esifaneleyo unyawo lwabo luzatshelela; usuku lwabo lokubhujiswa luseduze, ukuchitheka kwabo kubalanda ngesiqubu.’
Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
36 UThixo uzakwahlulela abantu bakhe, abe lozwelo ezincekwini zakhe lapho esebona amandla abo ephela njalo kakho ozasala, isigqili loba okhululekileyo.
Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
37 Uzakuthi: ‘Kanti bangaphi onkulunkulu babo, lelodwala ababephephela kulo,
Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
38 onkulunkulu abadla amafutha emihlatshelo yabo njalo banatha iwayini elingumnikelo wokunathwayo kwabo? Kabaphakame balincedise! Kabaliphe umthunzi wokuphephela!
milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
39 Angithi liyazibonela ukuthi Mina ngiNguye! Kakho omunye unkulunkulu ngaphandle kwami. Ngiyabhubhisa njalo ngiyaphilisa. Ngilimazile njalo ngizelapha, kakho ongaphunyuka esandleni sami.
“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
40 Ngiphakamisela isandla sami ezulwini ngithi: Njengoba ngeqiniso ngiphila nini lanini,
Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 nxa ngilola inkemba yami ephazimayo lesandla sami siyibamba ekwehluleleni, ngizaphindisela kuzozonke izitha zami, ngiphindisele kulabo abangizondayo.
pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
42 Imitshoko yami izagava igazi, kanti inkemba izakudla enyameni: igazi lalabo ababulawayo labathunjwayo, amakhanda alabo abangabakhokheli bezitha.’
Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
43 Jabulani, lina zizwe, kanye labantu bakhe, ngoba uzaphindisela igazi lezinceku zakhe, uzaphindisela ezitheni zakhe, njalo enzele ilizwe lakhe labantu bakhe indlela yokubuyisana.”
Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 UMosi weza loJoshuwa indodana kaNuni wethula wonke amazwi engoma le abantu bonke besizwa.
Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
45 UMosi wathi eqeda ukuwethula lamazwi phambi kwabo bonke abako-Israyeli,
Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
46 wathi kubo, “Alondolozeni ezinhliziyweni zenu wonke lamazwi engiwethule phambi kwenu ngesifungo lamuhla, ukuze libe lakho ukubalaya abantwabenu ukuba bawalalele ngonanzelelo amazwi alo umthetho.
iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
47 Akusimazwi alula nje kini, ayikuphila kwenu. Ngala amazwi lizaphila isikhathi eside elizweni eselingena kulo lichapha uJodani ukuba lilithathe libe ngelenu.”
Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
48 Ngalolosuku uThixo watshela uMosi wathi,
Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
49 “Khwela uye okhahlamba lwezintaba zase-Abharimi eNtabeni yaseNebho kwelamaMowabi, ngaphetsheya kweJerikho, ukuze ubone iKhenani, ilizwe engilinika abako-Israyeli ukuba balithathe libe ngelabo.
“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
50 Phezu kwaleyontaba okhwele phezu kwayo uzakufa umbelwe uye kubokhokho bakho njengoba u-Aroni laye wafela entabeni yaseHori wembelwa kwabakibo.
Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
51 Lokhu kungenxa yokuthi lina lobabili lalahla ithemba lenu kimi phambi kwabako-Israyeli emachibini aseMeribha Khadeshi, eNkangala yaseZini langenxa yokuthi alizange lime ngobungcwele bami phambi kwabako-Israyeli.
Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
52 Ngenxa yalokho, ilizwe uzalibonela kude, awusoze ungene elizweni esengilinika abako-Israyeli ukuba bangene kulo.”
Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

< UDutheronomi 32 >