< UDutheronomi 26 >

1 “Nxa usungenile elizweni uThixo uNkulunkulu wakho akunika lona njengelifa njalo usulithethe wahlala kulo
Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
2 thatha ezinye zezithelo zakuqala zazo, zonke izilimo zomhlabathi welizwe uThixo uNkulunkulu wakho akunika lona uzifake esitsheni. Uhambe uye endaweni leyo uThixo uNkulunkulu wakho azayikhetha njengendawo yokuhlala yeBizo lakhe
mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
3 uthi kumphristi osesikhundleni ngalesosikhathi, ‘Ngiyamemezela lamuhla kuThixo uNkulunkulu wakho ukuthi sengifikile elizweni uThixo afunga kubokhokho bethu ukuthi uzasinika lona.’
ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
4 Umphristi uzakwamukela isitsha esisezandleni zakho asibeke phansi phambi kwe-alithari likaThixo uNkulunkulu wakho.
Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
5 Ngakho uzakutsho phambi kukaThixo uNkulunkulu wakho uthi: ‘Ubaba wayeluzulani lomʼAramu, wehla waya eGibhithe elabantu abalutshwana bafika bahlala khona baze baba yisizwe esikhulu kakhulu, esilamandla njalo esilabantu abanengi kakhulu.
Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
6 Kodwa amaGibhithe asiphatha ngochuku, asihlupha, asisebenzisa nzima.
Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
7 Ngakho sakhala kuThixo, uNkulunkulu wabokhokho bethu, uThixo walizwa ilizwi lethu njalo wabona lokuhlupheka kwethu, ukutshikatshika kwethu kanye lokuncindezelwa kwethu.
Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
8 Ngenxa yalokho uThixo wasikhupha elizweni laseGibhithe ngesandla esilamandla langengalo eyeluliweyo, ngezenzo ezesabekayo langezibonakaliso kanye lezimangaliso.
Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
9 Wasiletha kulindawo njalo wasinika lelilizwe, ilizwe eligeleza uchago loluju;
Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
10 khathesi sengiletha izithelo zakuqala zomhlabathi lowo, Oh Thixo, onginike wona.’ Uzabeka isitsha phambi kukaThixo uNkulunkulu wakho umkhothamele.
Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
11 Ngakho wena labaLevi kanye labezizweni abahlala phakathi kwenu lizathokoza ezintweni zonke ezinhle uThixo uNkulunkulu wakho akunike zona wena kanye labendlu yakho.
Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
12 Kuzakuthi lapho usuqedile ukwahlukanisa okwetshumi kwaso sonke isivuno sakho ngomnyaka wesithathu, okungumnyaka wokwetshumi, wena uzakunika umLevi, owezizweni, intandane kanye lomfelokazi, ukuze badle basuthe emadolobheni akho.
Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
13 Tshono futhi kuThixo uNkulunkulu wakho uthi: ‘Sengikhuphile isabelo esingcwele endlini yami ngasinika umLevi, owezizweni, intandane lomfelokazi, njengokulaya kwakho. Kangeqanga imilayo yakho kumbe ukukhohlwa eminye yayo.
Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
14 Angizange ngidle lutho lwesabelo esingcwele ngesikhathi sokulila, kumbe ukususa okunye kwakho ngesikhathi ngingongcolileyo, loba ukunikela ingxenye yakho kwabafileyo. Ngikulalele Thixo Nkulunkulu wami; ngenzile konke ongilaye khona.
Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
15 Khangela phansi usezulwini, indawo yakho yokuhlala engcwele, ubusise abantu bakho bako-Israyeli kanye lelizwe osinike lona njengesithembiso owasenza ngesifungo kubokhokho bethu, ilizwe eligeleza uchago loluju.’”
Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
16 “UThixo uNkulunkulu wakho uyakulaya lamuhla ukuba ulandele izimiso kanye lemithetho le; uyigcine ngonanzelelo olukhulu ngenhliziyo yakho yonke kanye langomphefumulo wakho wonke.
Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
17 Lamuhla usuvume obala ukuthi uThixo unguNkulunkulu wakho lokuthi uzahamba ezindleleni zakhe, ukuthi uzagcina izimiso zakhe, imilayo, lemithetho yakhe, lokuthi uzamlalela.
Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
18 Futhi uThixo ukuvumile lamuhla ukuthi lina lingabantu bakhe, liyisabelo sakhe esiligugu njengokuthembisa kwakhe njalo kumele ligcine yonke imilayo yakhe.
Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
19 Umemezele ukuthi uzaliphakamisa ngodumo, ngokwaziwa langenhlonipho phezu kwezizwe zonke azidalayo lokuthi lizakuba ngabantu abangcwele kuThixo uNkulunkulu wenu njengokuthembisa kwakhe.”
Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.

< UDutheronomi 26 >