< UDutheronomi 11 >

1 “Thandani uThixo uNkulunkulu wenu lilondoloze okwakhe, izimiso, imithetho lemilayo yakhe ngazozonke izikhathi.
Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
2 Khumbulani lamuhla ukuthi abantwabenu akusibo ababubonayo njalo babazi ubukhulu bukaThixo uNkulunkulu wenu; ubukhosi bakhe, isandla sakhe esilamandla, lengalo yakhe eyelulekileyo;
Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
3 izibonakaliso azenzayo kanye lakho konke akwenzayo phakathi kwelizwe leGibhithe, ezenza kuFaro iNkosi yeGibhithe laselizweni lakhe lonke;
zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
4 lalokho akwenza kubutho leGibhithe, lasemabhizeni lezinqola zawo, ukuthi wakunqoba njani konke lokhu ngamanzi oLwandle oluBomvu mhla bexotshana lani, kanye lokuthi uThixo wabachitha baphela du.
zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
5 Akusibantwabenu ababona alenzela khona enkangala laze lazafika lapha,
Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
6 kanye lalokho akwenza kuDathani lo-Abhiramu, amadodana ka-Eliyabi wako-Rubheni. Lapho umhlaba owavuleka khona phambi kwabako-Israyeli wabaginya bonke kanye lezimuli zabo, lamathente abo lakho konke okuphilayo okwakungokwabo.
ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
7 Kodwa-ke kwakungawenu amehlo abona zonke lezizinto ezazenziwe nguThixo.
Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
8 Yikho-ke gcinani lilalele yonke imilayo engilinika yona lamuhla, ukuze lizuze amandla okuchapha iJodani liyelithumba lelolizwe,
Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
9 njalo lihlale kulo isikhathi eside ilizwe uThixo alinika okhokho benu lezizukulwane zenu, ilizwe eligeleza uchago loluju.
ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
10 Lelolizwe elizangena kulo lilithumbe alifanani lelizwe laseGibhithe, lapho elivela khona, lapho elalihlanyela inhlanyelo yenu lithwala amanzi nzima lithelela njengesivandeni semibhida.
Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
11 Kodwa ilizwe elilichaphela uJodani ukuze lilithumbe libe ngelenu yilizwe lezintaba lezihotsha ezinatha zigcwale ngamanzi ezulu.
Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
12 Yilizwe uThixo uNkulunkulu wenu alikhathalelayo, amehlo kaThixo wenu aphezu kwalo kusukela ekuqaleni komnyaka kuze kube sekupheleni kwawo.
Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
13 Ngakho lingalalela ngokwethembeka imilayo yami engilinika yona lamuhla, ukuthanda uThixo uNkulunkulu wenu njalo limkhonze ngenhliziyo zenu zonke, langemiphefumulo yenu yonke,
Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
14 ngalokho ngizanisa izulu emhlabeni wenu ngesikhathi salo, ekwindla kanye lasentwasa, ukuze libe lenala yamabele njalo livune, iwayini elitsha kanye lamafutha.
pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
15 Ngizamilisa utshani egangeni obuzadliwa zinkomo zenu, lina lizakudla lisuthe.
Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
16 Qaphelani linanzelele ukuthi aliyikuhugeka lihlamuke likhonze abanye onkulunkulu libakhothamele.
Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
17 Kungaba njalo ulaka lukaThixo luzavutha kini, njalo uzavala amazulu akhe ukuze kungabi lezulu elizakuna kuthi umhlaba wenu ungatheli izithelo, kuthi lina libhubhe masinyane elizweni elihle uThixo alinika lona.
Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
18 Gcinani amazwi ami la ezinhliziyweni lasengqondweni zenu, abopheleni njengezimpawu ezandleni zenu, liwabophele lemabunzini enu.
Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
19 Afundiseni abantwabenu, lixoxe ngawo nxa lihlezi emakhaya enu kanye lalapho lihamba endleleni, lapho lilala lanxa livuka.
Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
20 Abhaleni emigubazini yezindlu zenu kanye lasemasangweni enu,
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
21 ukuze kuthi insuku zenu kanye lezabantwabenu zande elizweni uThixo afunga ukulinika okhokho benu, kuze kube laphakade.
kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
22 Nxa lingamhlonipha lilandele imilayo yami le engilinika yona ukuba liyilandele, ukuthanda uThixo uNkulunkulu wenu, ukuhamba ngezindlela zakhe libambelele kuye ngokuqinileyo,
Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
23 ngalokho uThixo uzazixotsha zonke izizwe phambi kwenu njalo lani lizazemuka izizwe ezinkulu kulani, njalo ezilamandla kulani.
Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
24 Yonke indawo elizanyathela kuyo izakuba ngeyenu: umhlaba wenu uzaqhela ukusuka enkangala usiya eLebhanoni, kusuka emfuleni iYufrathe kusiya olwandle olusentshonalanga.
Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
25 Kakho ozamelana lani. UThixo uNkulunkulu wenu, njengokulithembisa kwakhe, uzaletha ukuthuthumela ngani lokulesaba elizweni lonke, ngaphi langaphi elihamba khona.
Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
26 Khangelani, lamuhla ngifaka phambi kwenu isibusiso lesithuko,
Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
27 isibusiso nxa lilalela imilayo kaThixo uNkulunkulu wenu engilinika yona lamuhla;
dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
28 isithuko nxa lingalaleli imilayo kaThixo uNkulunkulu wenu njalo libe selitshiya indlela engilikhomba yona ngokulandela abanye onkulunkulu elingabaziyo.
Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
29 Nxa uThixo uNkulunkulu wenu eselifikisile elizweni eselingena kulo ukuba lilithumbe, kalibomemezela liseNtabeni iGerizimu lezozibusiso, kuthi liseNtabeni ye-Ebhali limemezele izithuko.
Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
30 Njengoba lisazi, izintaba zingaphetsheya kweJodani, entshonalanga yomgwaqo okhangele entshonalanga, eduzane lezihlahla ezinkulu zaseMore, elizweni lalawo maKhenani ahlala e-Arabha eduzane kweGiligali.
Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
31 Seliseduze ukuchapha iJodani ukuba lingene lithumbe lelolizwe uThixo uNkulunkulu wenu alinika lona. Kuzakuthi nxa selilithethe selihlala khona,
Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
32 libe leqiniso lokuthi liyalalela zonke izimiso lemithetho engilibekela yona lamuhla.”
mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

< UDutheronomi 11 >