< UDanyeli 5 >

1 Inkosi uBhelishazari wenzela izikhulu zakhe ezizinkulungwane idili elikhulu, wanatha lazo iwayini.
Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
2 Kwathi uBhelishazari enatha iwayini lakhe walaya ukuthi kulethwe izitsha zegolide lezesiliva ezazithethwe nguyise uNebhukhadineza ethempelini eJerusalema, efuna ukuthi inkosi, lezikhulu zayo, labafazi bayo kanye labafazi bayo beceleni banathele kuzo.
Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
3 Yikho baziletha izitsha zegolide ezazithethwe ethempelini likaNkulunkulu eJerusalema, kwasekusithi inkosi lezikhulu zayo kanye labafazi bayo beceleni banathela kuzo.
Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
4 Bathi belinatha iwayini babelokhu bedumisa onkulunkulu begolide labesiliva, labethusi, labensimbi, labezigodo labamatshe.
Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
5 Masinyane nje kwavela iminwe yesandla somuntu yaloba emdulini eduzane loluthi lwesibane esigodlweni. Inkosi yasibukela isandla siloba.
Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
6 Ubuso bayo bahloba, yethuka amadolo ayo aze atshayana, imilenze yathamba yathi wohlo phansi.
Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
7 Inkosi yamemeza yathi kakubizwe izangoma lezingcazi zezinkanyezi kanye lezanuse yasisithi kuwo la amadoda ayizihlakaniphi zaseBhabhiloni, “Loba ngubani ongabala umbhalo lo angitshele ukuthi utshoni uzagqokiswa eziyibubende agqiziswe iketane legolide entanyeni yakhe, njalo uzaphiwa isikhundla sesithathu sokuba ngumbusi kulelilizwe.”
Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
8 Zasezingena zonke izihlakaniphi. Kodwa zehluleka ukuwubala umbhalo lokutshela inkosi ukuthi utshoni.
Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
9 Ngakho inkosi uBhelishazari yathuthumela okwedlulayo, ubuso bayo bahloba. Izikhulu zayo zadideka.
Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
10 Indlovukazi yathi isizwa amazwi enkosi lezikhulu zayo yeza yangena endlini yedili. Yathi, “Oh nkosi, mana njalo. Ungethuki! Ungaze wahloba kanjalo!
Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
11 Kulomuntu embusweni wakho olomoya wabonkulunkulu abangcwele phakathi kwakhe. Ngesikhathi sikayihlo watshengisa ukuqonda, lokukhalipha lenhlakanipho okufana lokwabonkulunkulu. Uyihlo, inkosi uNebhukhadineza yambeka ukuba yinduna yabomasalamusi, lezangoma, lezingcazi zezinkanyezi lezanuse.
Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
12 Indoda le, uDanyeli, inkosi eyayimbiza ngokuthi nguBhelitheshazari, wabonakala elengqondo evukileyo, lolwazi lokuzwisisa, njalo elamandla okuhumutsha amaphupho, lokuchaza amalibho kanye lokuhlahlula izinkinga ezinzima. Mbize uDanyeli, uzakutshela ukuthi umbhalo utshoni.”
Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
13 Ngakho uDanyeli walethwa phambi kwenkosi, inkosi yathi kuye, “Wena unguye uDanyeli na, omunye wabathunjwa abalethwa ngubaba inkosi bevela koJuda?
Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
14 Sengizwile ukuthi umoya wabonkulunkulu uphakathi kwakho lokuthi ulokuqonda, lokukhalipha lenhlakanipho eyinqaba.
Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
15 Izihlakaniphi lezangoma zilethwe kimi ukuthi zingibalele umbhalo lo, zingitshele ukuthi utshoni, kodwa zehlulekile ukuwuchaza.
Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
16 Manje sengizwile ukuthi wena ulamandla okutsho ingcazelo lokuhlahlula izinkinga ezinzima. Aluba ungawubala umbhalo lo uphinde ungitshele ukuthi utshoni, uzagqokiswa eziyibubende, ugqiziswe leketane legolide entanyeni yakho, uphinde ubekwe esikhundleni sokuba ngowesithathu ebukhulwini bombuso lo.”
Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
17 UDanyeli wasephendula inkosi wathi, “Ungazigcinela lezozipho zakho, uphe leyomivuzo yakho omunye umuntu. Loba kunjalo ngizayibalela inkosi umbhalo lowo ngiyitshele ukuthi utshoni.
Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
18 Yebo kambe nkosi, uNkulunkulu oPhezukonke wanika uyihlo uNebhukhadineza ubukhosi lobukhulu lodumo kanye lenkazimulo.
“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
19 Ngenxa yesikhundla esiphezulu amnika sona, bonke abantu kanye lezizwe zonke labantu bendimi zonke babemqhuqha, bemesaba. Labo inkosi eyafuna ukubabulala, yababulala; labo eyafuna ukubaxolela, yabaxolela; labo eyafuna ukubakhweza ezikhundleni yabakhweza; kwathi labo eyafuna ukubayangisa, yabayangisa.
Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
20 Kodwa kwathi lapho inhliziyo yayo isilobuqholo, isilukhuni ngokuzigqaja yethulwa esihlalweni sayo sobukhosi yaphucwa udumo lwayo.
Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
21 Yaxotshwa ebantwini yaphiwa ingqondo yenyamazana; yahlala labobabhemi beganga, yadla utshani njengezinkomo; lomzimba wayo wagxanxwa ngamazolo omkhathi yaze yavuma ukuthi uNkulunkulu oPhezukonke nguye uThixo phezu kwemibuso yabantu, abeke phezu kwayo loba nguphi umbusi amthandayo.
Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
22 Kodwa wena ndodana yayo, awu Bhelishazari, kawuzithobanga, lokuba ukwazi konke lokhu.
“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
23 Endaweni yalokho, uzimisele ukumelana loThixo wezulu. Wathi kakuthathwe izitsha zethempeli layo zilethwe kuwe, kwasekusithi wena lezikhulu zakho, labafazi bakho kanye labafazi bakho beceleni lanathela iwayini kuzo. Wadumisa onkulunkulu besiliva legolide, abethusi, lensimbi, lezigodo lamatshe, abangaboniyo, labangezwayo labangaqedisisiyo. Kodwa kawumhloniphanga uNkulunkulu ophethe ukuphila kwakho kanye lezindlela zakho zonke esandleni sakhe.
Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
24 Kungakho ethumele lesosandla esalobe lumbhalo.
Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
25 Nanku umbhalo obulotshiwe: mene, mene, thekheli, pharisini.
“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
26 Nanku okutshiwo ngamagama la: Mene: Nkulunkulu usezibalile insuku zokubusa kwakho, usekuqedile.
“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
27 Thekheli: Usulinganisiwe esikalini wafunyanwa ulula.
Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 Pharisini: Umbuso wakho usuhlukaniswe phakathi, wabelwa amaMede lamaPhezhiya.”
Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
29 Kwathi ngomlayo kaBhelishazari uDanyeli wagqokiswa eziyibubende, wagqiziswa iketane legolide entanyeni yakhe, kwamenyezelwa ukuthi usengumbusi wesikhundla sobuthathu elizweni.
Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
30 Ngabona lobobusuku uBhelishazari, inkosi yamaBhabhiloni wabulawa,
Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
31 kwathi uDariyu umuMede wabuthatha ubukhosi eleminyaka engamatshumi ayisithupha lambili.
ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

< UDanyeli 5 >