< 2 USamuyeli 11 >
1 Kwathi entwasa, ngesikhathi amakhosi ayesiyakulwa ngaso impi, uDavida wathuma uJowabi elabantu benkosi lebutho lonke lako-Israyeli. Baqothula ama-Amoni basebevimbezela iRabha. Kodwa uDavida wasala eJerusalema.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 Ngelinye ilanga kusihlwa uDavida wavuka embhedeni wakhe wahambahamba phezu kophahla lwesigodlo. Esephahleni wabona owesifazane egeza. Owesifazane lowo wayemuhle kakhulu,
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 uDavida wasethuma umuntu ukuyabuza ngaye. Umuntu lowo wathi, “Kanti lo kasuBhathishebha, indodakazi ka-Eliyami umka-Uriya umHithi na?”
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 UDavida wathuma izithunywa ukuyamthatha. Weza kuye, wembatha laye. (Owesifazane lo wayezihlambulule ekungcoleni kwakhe.) Emva kwalokho wabuyela ekhaya.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 Owesifazane lowo wathatha isisu, wasethumela ilizwi kuDavida, esithi, “Sengilesisu.”
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Ngakho uDavida wathumela ilizwi leli kuJowabi elithi: “Ngilethela u-Uriya umHithi.” UJowabi wamthumela kuDavida.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 U-Uriya esefikile kuye, uDavida wambuza ukuthi uJowabi wayenjani, amabutho ayenjani kanye lokuthi impi yayiqhubeka njani.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 UDavida wasesithi ku-Uriya, “Yehlela endlini yakho ugeze inyawo zakho.” Ngakho u-Uriya wasuka esigodlweni, walandelwa yisipho esavela enkosini esasala sithunyelwa kuye.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 Kodwa u-Uriya walala entubeni yesigodlo lezinceku zonke zenkosi yakhe akaze aya endlini yakhe.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 Kwathi uDavida esetsheliwe ukuthi, “U-Uriya kayanga ekhaya,” wambuza wathi, “Angithi usanda kufika nje uvela khatshana? Kungani ungayanga ekhaya?”
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 U-Uriya wathi kuDavida, “Ibhokisi lesivumelwano sikaThixo lo-Israyeli loJuda kuhlezi emathenteni, inkosi yami uJowabi kanye labantu benkosi yami bamise egangeni. Pho ngingaya kanjani endlini ukuyakudla, lokunatha ngilale lomkami futhi na? Ngeqiniso elinjengoba uphila, mina angiyikwenza into enjalo!”
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 UDavida wasesithi kuye, “Hlala lapha elinye ilanga futhi, kusasa ngizakubuyisela emuva.” Ngakho u-Uriya wahlala eJerusalema lolosuku kanye lolwalandelayo.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 Esecelwe nguDavida, wadla wanatha laye, uDavida wasemdakisa. Kodwa kusihlwa u-Uriya waphuma wayalala ecansini lakhe phakathi kwezinceku zenkosi yakhe; akayanga ekhaya.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 Ekuseni uDavida walobela uJowabi incwadi wayiphathisa u-Uriya.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 Kuyo wayelobe ukuthi, “U-Uriya mbeke kuviyo eliphambili lapho impi evutha khona kakhulu. Lapho-ke khumukani kuye ukuze acakazelwe phansi afe.”
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 Ngakho kwathi uJowabi idolobho eselivimbezele, wabeka u-Uriya lapho ayesazi khona ukuthi yikho okwakulabavikeli abalamandla kakhulu.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 Kwathi abantu bakulelodolobho sebephumile ukuba balwe loJowabi, abanye babantu ebuthweni likaDavida bafa; u-Uriya umHithi laye futhi wafa.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 UJowabi wathumela uDavida umbiko opheleleyo ngempi.
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 Walaya isithunywa wathi: “Lapho usuqedile ukwethulela inkosi umbiko wempi,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 ulaka lwenkosi lungavutha, ibe isibuza isithi, ‘Kungani lisondele eduzane kangaka ledolobho ukuba lilwe? Kalazanga yini ukuthi kade bengatshoka imitshoko besemdulini?
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 Ngubani obulele u-Abhimelekhi indodana kaJerubhi-Bheshethi na? Owesifazane obephezu komduli kamjikijelanga ngembokodo, wayafela eThebhezi na? Kungani lisondele eduzane kangaka lomduli?’ Ingakubuza lokhu, uthi kuyo, ‘Lenceku yakho u-Uriya umHithi ifile.’”
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 Isithunywa sasuka sahamba, kwathi sesifikile samtshela uDavida konke uJowabi ayesithume ukuba siyekutsho.
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 Isithunywa sathi kuDavida, “Abantu basikhulele, baphuma bazasihlasela etshatshalazini, kodwa sibadudulele emuva entubeni yedolobho.
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 Lapho-ke abemitshoko batshoke izinceku zakho besemdulini, kwathi abanye abantu benkosi bafa. Lenceku yakho, u-Uriya umHithi ifile.”
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 UDavida watshela isithunywa wathi, “Yitsho lokhu kuJowabi: ‘Ungakhathazwa yilokhu; inkemba idla omunye njengoba isidla omunye. Qinisa ukuhlasela idolobho, ulichithe.’ Yitsho lokhu ukuba umise isibindi uJowabi.”
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 Kwathi umka-Uriya esezwile ukuthi umkakhe usefile, wamlilela.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 Kwathi isikhathi sokulila sesiphelile, uDavida wamletha endlini yakhe, wasesiba ngumkakhe wamzalela indodana. Kodwa into eyenziwa nguDavida yathukuthelisa uThixo.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.