< 2 Amakhosi 1 >

1 Ngemva kokufa kuka-Ahabi, amaMowabi ahlamukela u-Israyeli.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 U-Ahaziya wayewele embotsheni yendlu yakhe engaphezulu eSamariya walimala. Wathumela izithunywa, wathi kuzo, “Hambani liyebuza kuBhali-Zebhubhi, unkulunkulu wase-Ekroni, ukuthi kambe ngizasila yini kulokhu kulimala na.”
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Kodwa ingilosi kaThixo yathi ku-Elija umThishibi, “Suka uyehlangabeza izithunywa zenkosi yaseSamariya uyezibuza ukuthi, ‘Kambe yikuthi akuselaNkulunkulu ko-Israyeli na ukuze uyehlahlula kuBhali-Zebhubhi, unkulunkulu wase-Ekroni?’
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Ngakho uThixo uthi: ‘Awuyikusuka kulowombheda ogulela kuwo. Ngempela uzakufa!’”
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Ekubuyeleni kwezithunywa enkosini, yazibuza yathi, “Kungani selibuyile na?”
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Izithunywa zaphendula zathi, “Kulendoda esihlangabezileyo yathi kithi, ‘Buyelani enkosini elithumileyo liyeyitshela ukuthi, “Ilizwi likaThixo lithi: Kungenxa yokuthi akulaNkulunkulu yini ko-Israyeli okubangele ukuthi uthumele abantu ukuyahlahlula kuBhali-Zebhubhi, unkulunkulu we-Ekroni na? Ngakho awuyikuvuka kulowombheda olele kuwo. Ngempela uzakufa!”’”
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Inkosi yabuza izithunywa yathi, “Ngumuntu onjani lowo olihlangabezileyo waselitshela lokhu?”
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 Izithunywa zaphendula zathi, “Yindoda ebigqoke isigqoko soboya ekhalweni ibophe ngozwezwe.” Inkosi yathi, “Lowo ngu-Elija umThishibi.”
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Inkosi yasithumela ku-Elija induna yebutho labantu bayo abangamatshumi amahlanu. Induna yebutho yakhwela yaya ku-Elija, owayehlezi phezu koqaqa, yafika yathi kuye, “Muntu kaNkulunkulu, inkosi ithi, ‘Yehla!’”
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 U-Elija ephendula induna yebutho wathi, “Nxa ngingumuntu kaNkulunkulu, kakwehle umlilo ovela ezulwini ukuqothule wena kanye labantu bakho abangamatshumi amahlanu!” Lakanye wehla umlilo uvela ezulwini wayiqothula induna yebutho kanye labantu bayo.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Ngokubona lokho inkosi yathuma ku-Elija eyinye induna yebutho lamanye amadoda angamatshumi amahlanu. Induna yathi ku-Elija, “Muntu kaNkulunkulu, inkosi ithi, ‘Yehla khathesi.’”
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 U-Elija waphendula wathi, “Nxa ngingumuntu kaNkulunkulu, kakwehle umlilo ovela ezulwini ukuqothule wena kanye labantu bakho!” Ngakho umlilo kaNkulunkulu wehla uvela ezulwini waqothula izinduna zamabutho ezakuqala zombili kanye labo bonke abantu bayo abangamatshumi amahlanu.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Ngakho inkosi yathuma induna yebutho yesithathu labantu bayo abangamatshumi amahlanu. Induna yebutho yesithathu yakhwela yafika yaguqa ngamadolo phambi kuka-Elija yamncenga yathi, “Muntu kaNkulunkulu, akube lesihawu ngempilo yami leyamadoda la angamatshumi amahlanu, thina sizinceku zakho!
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Angithi uyabona, umlilo wehle uvela ezulwini waqothula izinduna zamabutho lamadoda angamatshumi amahlanu induna nganye. Kodwa manje akunakekele impilo yami!”
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 Ingilosi kaThixo yathi ku-Elija, “Yehla kanye layo induna; ungayesabi.” Ngakho u-Elija wasukuma wehla kanye lenduna waya enkosini.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 Wasesithi enkosini, “Ilizwi likaThixo lithi: Kungenxa yokuthi akulaNkulunkulu yini ko-Israyeli ukuze uthume izithunywa ukuthi ziyohlahlula kuBhali-Zebhubhi, unkulunkulu we-Ekroni na? Ngenxa yesenzo sakho lesi, awuyikuvuka kulowombheda olele kuwo. Ngempela uzakufa!”
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 Lakanye wafa, njengelizwi likaThixo elakhulunywa ngu-Elija. Njengoba u-Ahaziya wayengelandodana, ubukhosi bakhe bathathwa nguJoramu owaba yinkosi ngomnyaka wesibili wokubusa kukaJehoramu indodana kaJehoshafathi inkosi yakoJuda.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Konke okwembali yokubusa kuka-Ahaziya, kanye lakwenzayo, akulotshwanga yini egwalweni lwembali yamakhosi ako-Israyeli na?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< 2 Amakhosi 1 >