< 2 Amakhosi 20 >

1 Ngalezonsuku uHezekhiya wagula, eselengela ekufeni. Umphrofethi u-Isaya indodana ka-Amozi waya kuye wathi: “Nanku okutshiwo nguThixo: Lungisa indlu yakho, ngoba uzakufa; awuyikusila.”
Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
2 UHezekhiya waphendula ubuso bakhe wakhangela emdulini wakhuleka kuThixo esithi,
Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
3 “Khumbula, Thixo, ukuthi ngihambe phambi kwakho ngokuthembeka langokuzinikela ngenhliziyo yami yonke, njalo ngenze okuhle emehlweni akho.” UHezekhiya wakhala kabuhlungu.
“Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
4 U-Isaya engakasuki egumeni elingaphakathi, kwafika ilizwi likaThixo kuye lisithi:
Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
5 “Buyela uyetshela uHezekhiya, umkhokheli wabantu bami uthi, ‘Nanku okutshiwo nguThixo, uNkulunkulu kayihlo uDavida. Uthi: Ngiwuzwile umkhuleko wakho njalo ngizibonile lezinyembezi zakho; ngizakusilisa. Ngosuku lwesithathu kusukela khathesi uzakhwela uye ethempelini likaThixo.
“Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
6 Ngizakwengezelela iminyaka elitshumi lanhlanu empilweni yakho. Ngizakukhulula wena kanye ledolobho leli ezandleni zenkosi yase-Asiriya. Ngizavikela idolobho leli ngizenzela mina njalo ngisenzela inceku yami uDavida.’”
Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
7 U-Isaya wathi: “Lungisani isigaqa semikhiwa.” Bakwenza lokho basebethoba ngaso ithumba, wasesila.
Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
8 UHezekhiya wayebuze u-Isaya wathi, “Kuyini okuzakuba yisibonakaliso sokuthi uThixo uzangisilisa kanye lokuthi ngizakhwela ngiye phezulu ethempelini leNkosi ngosuku lwesithathu kusukela khathesi na?”
Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
9 U-Isaya waphendula wathi, “Nansi isibonakaliso sikaThixo kuwe, esokuthi uThixo uzakwenza akuthembisayo. Kambe isithunzi sizakuya phambili amanyathelo alitshumi kumbe sizabuyela emuva amanyathelo alitshumi na?”
Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
10 “UHezekhiya wathi kulula ukuba isithunzi siye phambili amanyathelo alitshumi, kodwa kasiyi emuva amanyathelo alitshumi.”
Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
11 Ngakho umphrofethi u-Isaya wacela kuThixo, uThixo wenza ukuthi isithunzi sibuyele emuva okwezinyathelo ezilitshumi esasehle ngawo ezikhwelelweni zika-Ahazi.
Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
12 Ngalesosikhathi uMerodakhi-Bhaladani indodana kaBhaladani inkosi yaseBhabhiloni wabhalela uHezekhiya izincwadi wamthumela lesipho ngoba wayezwile ngokugula kukaHezekhiya.
Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
13 UHezekhiya wazamukela izithunywa wazitshengisa konke okwakusendlini yakhe yokugcinela impahla, isiliva, igolide, iziyoliso kanye lamafutha acengekileyo, izikhali zakhe lakho konke okwakukhona enothweni yakhe. Akulalutho esigodlweni sakhe loba embusweni wakhe wonke uHezekhiya angazitshengisanga lona.
Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
14 Ngakho u-Isaya umphrofethi waya kuHezekhiya inkosi wambuza wathi, “Atheni amadoda lawana njalo avela ngaphi?” UHezekhiya waphendula wathi: “Avela elizweni elikhatshana. Avele eBhabhiloni.”
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
15 Umphrofethi wabuza wathi: “Aboneni esigodlweni sakho?” UHezekhiya wathi, “Abone konke okusesigodlweni sami. Akulalutho phakathi kwempahla zami eziligugu engingawatshengisanga khona.”
Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
16 Ngakho u-Isaya wasesithi kuHezekhiya, “Zwana ilizwi likaThixo lithi:
Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
17 Isikhathi sizafika sibili lapho konke okusesigodlweni sakho lakho konke oyihlo abakugcinayo kusiyafika lolosuku, kuzathwalelwa eBhabhiloni. Akuyikusala lutho, kutsho uThixo.
Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
18 Njalo abanye besizukulwane sakho, abenyama legazi lakho, abazazalwa nguwe, bazathathwa bayekuba ngabathenwa esigodlweni senkosi yaseBhabhiloni.”
Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
19 UHezekhiya waphendula wathi: “Ilizwi likaThixo olikhulumileyo lilungile.” Ngoba wayenakana esithi: “Kambe kakuyikuba lokuthula lokuvikeleka ekuphileni kwami na?”
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
20 Ezinye izehlakalo zombuso kaHezekhiya, konke ukuphumelela kwakhe lokwakha kwakhe ichibi kanye lomgelo owaletha amanzi phakathi komuzi, akulotshwanga yini egwalweni lwembali yamakhosi akoJuda na?
Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
21 UHezekhiya waya ekuphumuleni kubokhokho bakhe. Indodana yakhe uManase yathatha ubukhosi.
Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Amakhosi 20 >