< 2 Amakhosi 14 >
1 Ngomnyaka wesibili kaJowashi indodana kaJehowahazi inkosi yako-Israyeli, u-Amaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda waqalisa ukubusa.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu eqalisa ukubusa, njalo wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amabili lasificamunwemunye. Unina kwakunguJehowadani, owayevela eJerusalema.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Yena wenza okulungileyo phambi kukaThixo, kodwa kwakungafanani lokukayise uDavida. Kukho konke ayekwenza walandela inyathelo likayise uJowashi.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Kodwa izindawo eziphakemeyo zokukhonzela azizange zisuswe; abantu baqhubeka benikela imihlatshelo lokutshisa impepha kulezondawo.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Kuthe umbuso usuqinile ezandleni zakhe, wabulala izikhulu ezazibulele uyise owayeyinkosi.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Kodwa kasabulalanga amadodana alabo ababulala uyise inkosi, njengokulotshiweyo eNcwadini yoMthetho kaMosi lapho uThixo alaya khona wathi: “Abazali abayikufela abantwababo, loba abantwana bafele abazali babo; ngulowo lalowo uzafela isono sakhe.”
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Nguye owanqoba ama-Edomi azinkulungwane ezilitshumi, eSigodini seTswayi waze wathumba iSela empini, wayibiza ngokuthi yiJokitheli, okulibizo layo kuze kube lalamuhla.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Ngakho u-Amaziya wathumela izithunywa kuJowashi indodana kaJehowahazi, indodana kaJehu, inkosi yako-Israyeli emqopha esithi, “Woza, uqondane lami ubuso ngobuso.”
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Kodwa uJowashi inkosi yako-Israyeli waphendula u-Amaziya inkosi yakoJuda wathi, “Isihlahlana sameva saseLebhanoni sathumela umsedari eLebhanoni ilizwi sathi, ‘Yendisela indodakazi yakho endodaneni yami.’ Kwavela isilo eLabhanoni eseza safika sagxobagxoba isihlahlana sameva ngamasondo aso.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Ngempela uyinqobile i-Edomi ngakho khathesi usuziqhenya. Ziqhenye ekunqobeni kwakho, kodwa uhlale ekhaya! Kungani uzibizela uhlupho uzibangela ukulwa kwakho njalo lokukaJuda na?”
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Loba kunjalo, u-Amaziya, kazange alalele, ngakho uJowashi inkosi yako-Israyeli wahlasela. Yena waqondana lo-Amaziya inkosi yakoJuda bakhangelana ubuso ngobuso eBhethi-Shemeshi koJuda.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 UJuda wachithwa ngu-Israyeli, kwathi amadoda wonke abalekela emizini yawo.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 UJowashi inkosi yako-Israyeli wathumba u-Amaziya inkosi yakoJuda, indodana kaJowashi, eyindodana ka-Ahaziya, eBhethi-Shemeshi. Ngakho uJowashi wasesiya eJerusalema wayadiliza umduli weJerusalema kusukela esangweni lika-Efrayimi kusiya eSangweni leJiko, isibanga esingaba yizingalo ezingamakhulu ayisithupha ubude.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 Wathatha lonke igolide lesiliva lazozonke ezinye impahla ezatholakala zisethempelini likaThixo lasezindlini zenotho esigodlweni waphinda wathumba labantu wahamba labo eSamariya.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Mayelana lezinye izehlakalo zombuso kaJowashi, lakho konke lokuphumelela kwakhe, lempi ayilwa lo-Amaziya inkosi yakoJuda, lokhu akulotshwanga yini egwalweni lwembali yamakhosi ako-Israyeli na?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 UJowashi waphumula laboyise, njalo wembelwa eSamariya lamakhosi ako-Israyeli. UJerobhowamu indodana yakhe wabusa esikhundleni sakhe.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 U-Amaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda waphila okweminyaka elitshumi lemihlanu ngemva kokufa kukaJowashi indodana kaJehowahazi inkosi yako-Israyeli.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Mayelana lezinye izehlakalo zombuso ka-Amaziya azilotshwanga na egwalweni lwembali yamakhosi akoJuda?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Bamenzela icebo eJerusalema, wasebalekela eLakhishi, kodwa bathumela amadoda amlandela ayambulalela khonale.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Bamthwala ngebhiza bamletha eJerusalema lapha angcwatshwa khona labokhokho bakhe, eMzini kaDavida.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Ngakho abantu bonke koJuda bathatha u-Azariya, owayeleminyaka elitshumi lesikhombisa yokuzalwa bamgcoba ubukhosi bukayise u-Amaziya.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Nguye owakha kutsha i-Elathi walibuyisela koJuda ngemva kokuphumula kukayise labokhokho bakhe.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Ngomnyaka wetshumi lanhlanu ka-Amaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda, uJerobhowamu indodana kaJowashi inkosi yako-Israyeli waba yinkosi eSamariya, njalo wabusa okweminyaka engamatshumi amane lanye.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Wenza ububi phambi kukaThixo njalo kazange atshiye lasinye sezono zikaJerobhowamu indodana kaNebhathi, lezo abangela u-Israyeli ukuthi azenze.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Nguye owabuyisela imingcele yako-Israyeli kusukela eLebho Hamathi kusiya eLwandle lwase-Arabha, njengelizwi likaThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, alikhuluma ngenceku yakhe uJona indodana ka-Amithayi, umphrofethi owayevela eGathi-Heferi.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 UThixo wayekubonile ukuthi kwakubuhlungu kanganani kubo bonke abako-Israyeli, izigqili loba ababekhululekile, ukuhlupheka ababekukho; kungekho labani owayengabasiza.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 Kanti njengoba uThixo wayengatshongo ukuthi uzakwesula ibizo lika-Israyeli ngaphansi kwamazulu, wabahlenga ngesandla sikaJerobhowamu indodana kaJowashi.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Mayelana lezinye izehlakalo zombuso kaJerobhowamu, konke akwenzayo, kanye lokuphumelela kwakhe empini, lokuthi wathumba njani wabuyisela embusweni ka-Israyeli iDamaseko leHamathi, ayengawe Juda, akulotshwanga yini egwalweni lwembali yamakhosi ako-Israyeli na?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 UJerobhowamu waphumula laboyise, amakhosi ako-Israyeli. UZakhariya indodana yakhe wabusa esikhundleni sakhe.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.