< 2 Imilando 20 >
1 Ngemva kwalokho amaMowabi lama-Amoni kanye labanye bamaMewuni baphuma impi ukuba bayehlasela uJehoshafathi.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Amanye amadoda aya kuJehoshafathi afika athi kuye, “Kulempi enkulu ezayo ukuzakuhlasela evela ngase-Edomi, ngaphetsheya kolwandle. IsiseHazazoni Thamari” (okuyikuthi, Eni-Gedi).
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Ngokwethuka, uJehoshafathi wazimisela ukumdinga uThixo, wamemezela ukuba akuzilwe ukudla kulolonke elakoJuda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Abantu bakoJuda baqoqana bahlangana bezodinga usizo kuThixo, lakanye baphuma kuyo yonke imizi yakoJuda.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Ngakho uJehoshafathi wema phambi kwebandla lakoJuda lelaseJerusalema ethempelini likaThixo phambi kweguma elitsha
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 wathi, “Oh Thixo, Nkulunkulu wabokhokho, kakusuwe yini uNkulunkulu osezulwini? Ubusa phezu kwemibuso yezizwe zonke. Amandla asesandleni sakho, njalo kakho ongamelana lawe.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 Oh Nkulunkulu wethu, awubaxotshanga ababekuleli lizwe phambi kwabantu bakho bako-Israyeli wabanika ukuba libe ngelabo nini lanini abesizukulwane sika-Abhrahama umngane wakho na?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Sebehlale kulo njalo sebakhe indawo yokukhonzela yeBizo lakho, besithi,
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 ‘Nxa sisehlelwa zinhlupheko, loba yinkemba yokwahlulela, loba yizifo loba yindlala, sizakuma ngobukhona bakho phambi kwalelithempeli elileBizo lakho sikhale kuwe ekuhlukuluzweni kwethu, wena uzasizwa njalo usisindise.’
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Kodwa khathesi nanka amadoda ama-Amoni lamaMowabi labeNtabeni yaseSeyiri, abelizwe owalela u-Israyeli ukuba alinqobe ekuphumeni kwakhe eGibhithe; okwabangela ukuthi babatshiye abaze bababhubhisa.
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Khangela ukuthi khathesi baphindisela ngokunganani ngokusemuka isipho owasipha sona ukuba sibe yilifa lethu.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Oh Nkulunkulu wethu, awuyikubahlulela na? Ngoba asilamandla okumelana lebutho elikhulu kangaka elisihlaselayo. Asikwazi esingakwenza, kodwa amehlo ethu aphezu kwakho.”
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Wonke amadoda akoJuda, labomkabo labantwabawo lensane, bema lapho phambi kukaThixo.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 UMoya kaThixo wehlela kuJahaziyeli indodana kaZakhariya, indodana kaBhenaya, indodana kaJeyiyeli, indodana kaMathaniya, umLevi oyisizukulwane sika-Asafi, emi phambi kwebandla.
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Wasesithi: “Lalela, wena Nkosi Jehoshafathi labo bonke abahlala koJuda labaseJerusalema! Nanku okutshiwo nguThixo kini: ‘Lingesabi njalo lingadediswa yibukhulu bebutho laleyompi. Ngoba ukulwa akusikwenu, kodwa ngokukaNkulunkulu.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Kusasa hambani liyejamelana labo. Bona bazakhwela ngokhalo lwaseZizi, lina lizabathola ekucineni kodonga eNkangala yaseJeruweli.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Aliyikuyilwa limpi. Lunganini ezindaweni; lime ngesibindi lizabona ukuhlenga kukaThixo azalenzela khona, Oh lina bakaJuda lani beJerusalema. Lingesabi, lingadangali. Phumani kusasa liyehlasela, uThixo uzakuba lani.’”
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 UJehoshafathi wakhothama ubuso buphansi kanti njalo bonke abakoJuda labaseJerusalema bawela phansi ngobuso bemkhonza uThixo.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Ngakho abanye abaLevi bamaKhohathi, lamaKhora bema bamdumisa uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, ngelizwi eliphakemeyo okuphezulu.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Kwathi ekuseni kakhulu basuka baya eNkangala yaseThekhowa. Bathi besuka lapho, uJehoshafathi waphakama wathi, “Lalelani kimi, bantu bakoJuda lani baseJerusalema! Thembelani kuThixo uNkulunkulu wenu uzaliphathisa; likholwe abaphrofethi bakhe, lizaphumelela.”
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Ngemva kokubuza abantu, uJehoshafathi wakhetha amadoda okuhlabelela uThixo lokumdumisa ngenxa yenkazimulo yobungcwele bakhe bekhokhele amabutho, besithi: “Mbongeni uThixo, ngoba uthando lwakhe lumi nininini.”
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Bathi beqalisa ukuhlabelela njalo bedumisa, uThixo wabeka abantu bokucathamela abase-Amoni labase-Mowabi labaseNtabeni iSeyiri ababedinga ukuhlasela uJuda, behlulwa.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Amadoda ako-Amoni lawamaMowabi avukela amadoda ayevela eNtabeni yaseSeyiri ukuba bawabulale bawatshabalalise. Ngemva kokuba sebeqedile ukubulala abaseSeyiri, banceda ngokubulalana bodwa.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Amadoda akoJuda athe efika endaweni emalungana lenkangala bakhangela lapho okwakulebutho elikhulu khona babona ngezidumbu zelekene phansi, kungekho loyedwa owayebalekile.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Ngakho uJehoshafathi lamanye amadoda bahamba bayabutha impango, njalo phakathi kwayo bafumana impahla zokusebenzisa lezembatho lezinye njalo impahla eziligugu ukwedlula lezo ababengazithwala. Impango yayinengi kwaze kwathatha insuku ezintathu beyithutha.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Ngosuku lwesine babuthana eSigodini saseBherakha, lapho abadumisela khona uThixo. Kungenxa yalokho yonale indawo yabizwa ngokuthi iSigodi saseBherakha kuze kube lamuhla.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Ngakho wonke amadoda akoJuda lawaseJerusalema abuyela ngokuthokoza eJerusalema, bekhokhelwa nguJehoshafathi ngoba uThixo wayebenzele lokho okwakubajabulisile phezu kwezitha zabo.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Bangena eJerusalema baya ethempelini likaThixo betshaya imihubhe lemiqangala lamacilongo.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Ukwesaba uNkulunkulu kwehlela phezu kwayo yonke imibuso emazweni besizwa ngokulwa kukaThixo esilwa lezitha zika-Israyeli.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Lakanye umbuso kaJehoshafathi waba lokuthula, ngoba uNkulunkulu wakhe wayemnike ukuphumula inxa zonke.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Ngakho uJehoshafathi wabusa koJuda. Waba yinkosi yakoJuda eleminyaka engamatshumi amathathu lanhlanu, wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amabili lanhlanu. Unina wayengu-Azubha indodakazi kaShilihi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Wahamba ngezindlela zikayise u-Asa njalo kazange aphambuke kuzo; wenza okulungileyo phambi kukaThixo.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Izindawo zokukhonzela kazisuswanga njalo abantu babelokhu bengazimiselanga ngezinhliziyo zabo ngokupheleleyo kuNkulunkulu waboyise.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Ezinye izehlakalo ngombuso kaJehoshafathi kusukela ekuqaleni kusiya ekucineni, zilotshiwe embalini kaJehu, indodana kaHanani, yona elotshwe egwalweni lwamakhosi ako-Israyeli.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Ngokuqhubeka kwezikhathi, uJehoshafathi inkosi yakoJuda waba lesibopho asenza lo-Ahaziya inkosi yako-Israyeli, owayelecala lokwenza okubi.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Wavumelana laye ukuba bakhe imikhumbi yokuthwala impahla zokuthengiselana. Ngemva kokuba isiyakhiwe e-Eziyoni-Gebheri,
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 u-Eliyezari indodana kaDodavahu waseMaresha wakhuluma isiphrofethi esilahla uJehoshafathi, esithi, “Ngenxa yokuthi wenza isibopho lo-Ahaziya, uThixo uzadiliza lokho okwenzileyo.” Imikhumbi yabhidlika ayaze yenelisa ukungena olwandle isiyathengisa.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.