< 1 Amakhosi 9 >

1 USolomoni eseqedile ukwakha ithempeli likaThixo lesigodlo sobukhosi, esenelisile konke ayezimisele ukukwenza,
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna,
2 UThixo wabonakala kuye ngokwesibili, njengoba wayebonakele kuye eGibhiyoni.
Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni.
3 UThixo wathi kuye: “Sengiwuzwile umkhuleko wakho lesikhalazo osenzileyo phambi kwami; sengilenze labangcwele lelithempeli olakhileyo wena ngokufaka iBizo lami kulo lanininini. Amehlo ami kanye lenhliziyo yami kuzakuba phezu kwalo ngezikhathi zonke.
Yehova ananena kwa iye kuti: “Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
4 Wena, ungahamba phambi kwami ngobuqotho benhliziyo langokuqonda njengoba uyihlo uDavida akwenza, wenze konke engikulaya ngakho ugcine izimiso zami lemithetho yami,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
5 ngizaqinisa isihlalo sakho sobukhosi phezu kuka-Israyeli kuze kube nininini, njengoba ngathembisa uyihlo uDavida lapho ngathi, ‘Awuyikwehluleka ukuzuza indoda esihlalweni sobukhosi ko-Israyeli.’
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
6 Kodwa nxa wena kanye lamadodana akho lingifulathela lingagcini imithetho lezimiso zami engilinike khona beselisuka liye kwabanye onkulunkulu libakhonze,
“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
7 ngizamthathela u-Israyeli umhlaba engangimnike wona ngilikhalale leli ithempeli esengilingcwelisile ngeBizo lami. U-Israyeli uzadelelwa abe yinhlekisa ebantwini bonke.
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
8 Lelithempeli lizakuba yinqumbi yamatshe. Bonke abedlula lapha bazakwenyanya bahleke ulunya bathi, ‘Kanti kungani uThixo enze into enje kulelilizwe lakulelithempeli na?’
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
9 Abantu bazaphendula bathi, ‘Kungenxa yokuthi sebedele uThixo uNkulunkulu wabo, owakhipha oyise eGibhithe, ngoba sebesuke banamathela kwabanye onkulunkulu, babakhonza njalo babasebenzela yikho-nje uThixo esebehlisele incithakalo yonke le.’”
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
10 Ekupheleni kweminyaka engamatshumi amabili, lapho uSolomoni akha khona lezizindlu ezimbili, ithempeli likaThixo kanye lesigodlo sobukhosi,
Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu,
11 iNkosi uSolomoni wanikela amadolobho angamatshumi amabili aweGalile kuHiramu inkosi yaseThire, ngoba uHiramu wayemnike zonke izigodo zesihlahla somsedari lezephayini legolide ayekufuna.
Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna.
12 Kodwa uHiramu wathi esesuka eThire esiyabona amadolobho ayewaphiwe nguSolomoni, kazange ajabule ngawo.
Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo.
13 Wambuza wathi, “Ngamadolobho bani la onginike wona, mfowethu?” njalo wayewabiza ngokuthi yilizwe leKhabhuli, okulibizo alokhu ebizwa ngalo lalamuhla.
Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino.
14 Kunjalo-nje uHiramu wayethumele uSolomoni igolide elalingamathalenta alikhulu elilamatshumi amabili.
Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
15 Nansi imbali yokubanjwa ngamandla kwabantu yiNkosi uSolomoni ukwakha ithempeli likaThixo, ukwakhiwa kwesigodlo sakhe, ledundulu elithiwa yiMilo, lomduli weJerusalema kanye leHazori, iMegido kanye leGezeri.
Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri.
16 (UFaro inkosi yaseGibhithe wayehlasele wathumba iGezeri. Wayeyithungele ngomlilo wayitshisa. Wayebulele amaKhenani ayehlala khona, yona wasekhunga ngayo indodakazi yakhe, umkaSolomoni.
(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni.
17 USolomoni waseyakha kutsha iGezeri.) Wakha iBhethi-Horoni esezansi,
Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi,
18 leBhalathi, kanye leThamari enkangala, phakathi kwelizwe lakhe,
Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo,
19 kanye lamadolobho ayeyiziphala lemizi yezinqola zakhe zempi kanye lamabhiza akhe lakho konke nje ayengafisa ukukwakha eJerusalema leLebhanoni kanye lakulo lonke ilizwe ayelibusa.
pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
20 Kubo bonke abantu abasalayo bama-Amori, amaHithi, amaPherizi, amaHivi lamaJebusi (lababantu babengasibo ama-Israyeli)
Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli).
21 okutsho ukuthi, izizukulwane zabo ezasalayo ama-Israyeli angazibulalanga aziqeda, laba uSolomoni wababamba isibhalo sokwenza umsebenzi wakhe wobugqili, njengoba kunjalo lalamuhla lokhu.
Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino.
22 Kodwa uSolomoni kabenzanga izigqili abako-Israyeli; babengamadoda okumlwela, iziphathamandla zikahulumende, izikhulu zakhe, izinduna, kanye labalawuli bezinqola zakhe zempi labatshayeli bazo.
Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake.
23 Njalo babeyizikhulu zokukhokhela imisebenzi eqakathekileyo kaSolomoni, izikhulu ezingamakhulu amahlanu lamatshumi amahlanu ezazikhangela amadoda ayesenza umsebenzi.
Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
24 Ngemva kokufika kwendodakazi kaFaro esigodlweni eyayisakhelwe nguSolomoni isuka eMzini kaDavida, wakha njalo idundulu elithiwa yiMilo.
Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
25 Kathathu ngomnyaka uSolomoni wanikela umnikelo wokutshiswa lomnikelo wobudlelwano e-alithareni ayelakhele uThixo, etshisa impepha phambi kukaThixo kanye lemihlatshelo. Ngalokho wagcwalisa imilandu yezimiso zethempeli.
Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
26 INkosi uSolomoni wakha njalo imikhumbi e-Eziyoni-Gebheri, eseduzane le-Elathi ngase-Edomi, ekhunjini loLwandle oluBomvu.
Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
27 Kunjalo-nje uHiramu wathumela abantu bakhe, abagwedli ababelwazi ulwandle ukuba bayesebenza emikhunjini labakaSolomoni.
Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni.
28 Bagwedla baya e-Ofiri baphenduka legolide elilesisindo samathalenta angamakhulu amane lamatshumi amabili, bayalethula enkosini uSolomoni.
Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

< 1 Amakhosi 9 >