< 1 Amakhosi 20 >

1 UBheni-Hadadi inkosi yama-Aramu waqoqa ibutho lakhe lonke. Wayephelekezelwa ngamakhosi angamatshumi amathathu lamabili ngezinqola zawo zempi lamabhiza, wasuka wayahanqa iSamariya wayihlasela.
Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
2 Wathuma izithunywa edolobheni ku-Ahabi inkosi yako-Israyeli, esithi, “Nanku okutshiwo nguBheni-Hadadi:
Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
3 Isiliva legolide lakho ngokwami, abafazi benu abahle kakhulu labantwana ngabami.”
“Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
4 Inkosi yako-Israyeli yaphendula yathi, “Kunjalo nkosi mbusi wami. Mina lakho konke engilakho ngokwakho.”
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
5 Izithunywa zaphenduka njalo zisithi, “UBheni-Hadadi uthi: ‘Ngathumela ngathi ngifuna isiliva legolide lakho, abafazi labantwabakho.
Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
6 Kodwa ngasolesi isikhathi kusasa ngizathumela izikhulu zami ukuzakhuthuza isigodlo sakho lezindlu zezikhulu zakho. Zizabutha yonke into eligugu kuwe zikuthathele.’”
Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
7 Inkosi yako-Israyeli yasibiza bonke abadala belizwe yathi kubo, “Ake libone lindoda edinga uhlupho! Ithe isithi ifuna abafazi bami labantwabami, isiliva legolide lami, angizange ngale.”
Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
8 Abadala kanye labantu bonke bathi, “Ungalaleli njalo ungamniki lokho akufunayo.”
Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
9 Yasitshela izithunywa zikaBheni-Hadadi ukuthi, “Tshelani inkosi umbusi wami ukuthi, ‘Inceku yakho izagcwalisa isicelo sakuqala kodwa lesi hayi ayenelisi.’” Zasuka izithunywa zabuyisela impendulo kuBheni-Hadadi.
Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
10 Ngakho uBheni-Hadadi wakhupha ilizwi njalo lisiya ku-Ahabi, wathi: “Kabangihlanekele onkulunkulu, loba kungaba lobunzima obunganani, nxa kuzasala ubhuqu olulingana ukufunjathwa ngamadoda wonke aseSamariya.”
Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
11 Inkosi yako-Israyeli yaphendula yathi, “Mtsheleni lithi: ‘Lowo ohloma ngezempi angabokloloda njengongahlomanga.’”
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
12 UBheni-Hadadi wemukela lelilizwi ezinathela lamanye amakhosi emathenteni awo, wahle walawula amabutho akhe esithi: “Hlomelani ukuhlasela.” Basebelungisela ukuhlasela idolobho.
Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
13 Kusenjalo kweza umphrofethi ku-Ahabi inkosi yako-Israyeli owafika wabika esithi, “Nanku okutshiwo nguThixo: ‘Uyalibona na ibutho elikhulu kangaka? Ngizalinikela ezandleni zakho lamuhla nje, ukuze wazi ukuba nginguThixo.’”
Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
14 U-Ahabi wabuza wathi, “Kodwa ngubani ozakwenza lokhu?” Umphrofethi waphendula wathi, “Nanku okutshiwo nguThixo: ‘Lokhu kuzakwenziwa ngabalawuli bamabutho ezabelweni abayintanga yabatsha.’” Yena wabuza njalo ukuthi, “Pho ngubani ozayiqalisa impi?” Umphrofethi wamphendula wathi, “Nguwe.”
Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
15 Ngakho u-Ahabi wamema abalawuli bamabutho abentanga yabatsha ezabelweni, abangamakhulu amabili lamatshumi amathathu lambili. Waseqoqa labo bonke abanye abako-Israyeli abazinkulungwane eziyisikhombisa ndawonye.
Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
16 Basuka emini enkulu ngesikhathi uBheni-Hadadi lamakhosi angamatshumi amathathu lambili ayezomhlomulela belokhu besazinathela bedakwa emathenteni abo.
Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
17 Abalawuli bezabelweni bentanga yabatsha basuka kuqala. UBheni-Hadadi wayethumele inhloli, ezabika ukuthi, “Kulamadoda ezayo evela eSamariya.”
Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
18 Yena wathi, “Nxa esiza ngokuthula, athumbeni ephila; nxa ezohlasela, athumbeni ephila.”
Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
19 Abalawuli bamabutho ezabelweni abentanga yabatsha baphuma edolobheni belandelwa libutho
Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
20 njalo ngamunye wabo wabulala lowo ayeqondene laye. Ebona lokhu, ama-Aramu abaleka, ama-Israyeli axotshana lawo. Kodwa uBheni-Hadadi inkosi yama-Aramu wabaleka ngebhiza lamanye amabutho ayesilwa ngamabhiza.
Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
21 Inkosi yako-Israyeli yaqhubeka yakhulela abamabhiza kanye labezinqola zempi yatshaya yabhuqa ama-Aramu amanengi kakhulu.
Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
22 Ngemva kwalokho, umphrofethi waya enkosini yako-Israyeli wafika wathi, “Hloma uphelele ubone ukuthi ungenzani, ngoba entwasa inkosi yama-Aramu iyeza izokuhlasela futhi.”
Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
23 Kusenjalo, izikhulu zenkosi yase-Aramu zayicebisa zathi, “Onkulunkulu babo ngonkulunkulu bezintabeni. Yikho besikhulele. Kodwa singalwela emagcekeni, ngempela sizabakhulela.
Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
24 Wena yenza kanje: Susa wonke amakhosi ekulawuleni kwawo ufake abanye abalawuli esikhundleni sawo.
Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
25 Njalo kumele uqoqe amanye amabutho anjengala anqotshwayo, kulingane amabhiza kanye lezinqola zempi ukuze silwele emagcekeni labako-Israyeli. Ngalokho akulakuthandabuza ukuthi sizabe silamandla kulabo.” Wavumelana labo wenza njengokutsho kwabo.
Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
26 Ngesikhathi sentwasa uBheni-Hadadi waqoqa ama-Aramu wasesiya e-Afekhi ukuze alwe labako-Israyeli.
Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
27 Ama-Israyeli ayeseqoqene, anikwa lemiphako, asuka ayawahlangabeza. Ama-Israyeli amisa maqondana lawo kungathi yimihlanjana yembuzi emibili, kanti ama-Aramu ayegcwele indawana yonke.
Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
28 Umphrofethi kaNkulunkulu wasesiya enkosini yako-Israyeli wafika wathi, “Nanku okutshiwo nguThixo: ‘Njengoba ama-Aramu esithi uThixo ngunkulunkulu wezintaba hatshi uNkulunkulu wezigodi, ngizanikela wonke amabutho awo amanengi kangaka ezandleni zakho, ukuze wazi ukuthi mina nginguThixo.’”
Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
29 Bajamelana okwensuku eziyisikhombisa, kwathi ngosuku lwesikhombisa bahlaselana. Ama-Israyeli abulala abazinkulungwane ezilikhulu phakathi kwamabutho ama-Aramu ahamba ngezinyawo ngosuku olulodwa.
Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
30 Amanye amabutho abalekela edolobheni lase-Afekhi, lapho adilikelwa khona ngumduli owabulala izinkulungwane ezingamatshumi amabili lesikhombisa. Kwathi uBheni-Hadadi wabalekela edolobheni lapho afika wacatsha endlini ephakathi.
Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
31 Izikhulu zakhe zathi kuye, “Khangela, sesizwile ukuthi amakhosi ako-Israyeli ngamakhosi alomusa. Asihambeni enkosini yako-Israyeli sembethe amasaka okhalweni njalo sibophe amakhanda ngentambo. Mhlawumbe izakuxolela ingakubulali.”
Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
32 Basuka bethandele amasaka ezinkalweni zabo, bebophe amakhanda ngentambo, baya enkosini yako-Israyeli bafika bathi, “Inceku yakho uBheni-Hadadi ithi, ‘Ngicela ungiyekele ngiphile.’” Inkosi yathi, “Ulokhu esaphila? Ngumfowethu lowo.”
Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
33 Amadoda lawo abona lokhu kukhomba ubuhle alithathela phezulu lelilizwi athi, “Ye, umfowenu uBheni-Hadadi!” Inkosi yathi, “Hambani liyemthatha.” Lakanye uBheni-Hadadi uthe efika, u-Ahabi wathi kakhwele enqoleni yakhe yempi.
Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
34 UBheni-Hadadi wazibika esithi, “Ngizabuyisela wonke amadolobho athunjwa ngubaba kuyihlo. Ungazilungisela izindawo zokuthengiselana eDamaseko, njengoba ubaba laye wayelazo eSamariya.” U-Ahabi wathi, “Ngesivumelwano ngizakukhulula.” Wasesenza isivumelwano laye wamkhulula.
Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
35 Ngelizwi likaThixo omunye wamadodana abaphrofethi wathi komunye, “Ake ungitshaye ngesikhali sakho,” kodwa wala.
Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
36 Ngakho umphrofethi wasesithi, “Njengoba ungalalelanga ilizwi likaThixo, uzakuthi usuka kimi ubulawe yisilwane.” Ngemva kokusuka kwakhe, wafunyanwa yisilwane sambulala.
Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
37 Umphrofethi wafumana enye njalo indoda wathi kuyo, “Ake ungigwaze.” Yamgwaza leyondoda yamlimaza.
Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
38 Umphrofethi wasuka wayamelela inkosi endleleni. Wazifihla ubuso bakhe ngeqhiye.
Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
39 Kuthe inkosi isedlula khonapho, umphrofethi wayimemeza esithi, “Inceku yakho ibe iphakathi kwempi etshisayo, kwathi omunye weza kimi lothunjiweyo wathi, ‘Linda lumuntu. Nxa engabaleka, uzamfela wena, loba uhlawule ngethalenta lesiliva.’
Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
40 Kuthe inceku yakho isaphathekile lapha lalaphaya, umuntu lowo wanyamalala.” Inkosi yako-Israyeli yathi, “Leso yiso isigwebo sakho. Usuvele wasiqamba wena ngokwakho.”
Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
41 Umphrofethi waphanga wembula ubuso bakhe, inkosi yako-Israyeli yabona ukuthi ngomunye wabaphrofethi.
Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
42 Wathi enkosini, “Nanku okutshiwo nguThixo: ‘Usukhulule umuntu ebengithe kumele afe. Kutsho ukuthi usuzamfela wena, labantu bakho bazafela abantu bakhe.’”
Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
43 Ngokuhlulukelwa langokuzonda, inkosi yako-Israyeli yasuka yabuyela esigodlweni sayo eSamariya.
Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.

< 1 Amakhosi 20 >