< Romans 14 >

1 Kintu kun biswas te komjur ase, tai logote eku bisar kotha nadiyi kene, taike grohon koribi.
Mulandire amene ndi ofowoka mʼchikhulupiriro, osatsutsana naye pa maganizo ake.
2 Biswas thaka ekjon to sob khabo pare, kintu komjur thaka ekjon to khali pata-sata he khai.
Chikhulupiriro cha munthu wina chimamulola kudya china chilichonse koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake ndi chofowoka, amangodya zamasamba zokha.
3 Etu karone kun pora sob khai, tai pora ekjon kun eku nakhai taike ninda koribo nadibi; aru jun manu nakhai tai bhi kha ekjon ke bisar na koribi. Kelemane Isor pora taike grohon kori loise.
Munthu amene amadya chilichonse sayenera kunyoza amene satero, ndipo munthu amene samadya chilichonse asaweruze munthu amene amatero, pakuti Mulungu anamulandira.
4 Apuni kun ase dusra laga nokor ke bisar kori bole to? Tai nijor laga malik age te he tai khara korithake, nohoile giri thake. Kintu taike uthai dibo kelemane, Probhu pora taike khara kori dibole pare.
Kodi ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wamwini? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza popeza kuti Mbuye wake angathe kumukhozetsa.
5 Ekjon pora din ekta to dusra din pora bhal eneka bhabona kore, kintu kunba pora sob din to eke eneka bhabona kore. Sob manu pora nijor monte he thik biswas koribo lage.
Munthu wina amayesa tsiku limodzi lopatulika kuposa lina. Munthu wina amayesa masiku onse ofanana. Aliyense akhale otsimikiza mʼmaganizo ake.
6 Kun pora din alag ulaikene mani ase, tai Probhu laga naam te mani loi ase; aru jun manu khai ase, Isor ke dhanyavad diya nisena, Probhu laga naam te khai ase. Jun manu nakhai, Isor ke dhanyavad diya nisena Probhu laga naam te nakhabi.
Iye amene amaganiza kuti tsiku limodzi ndi lopambana, amatero kwa Ambuye. Iye amene amadya nyama, amadya mwa Ambuye pakuti amayamika Mulungu. Ndipo iye amene sadya, amatero kwa Ambuye ndi kuyamika Mulungu.
7 Kelemane amikhan kun bhi nijor nimite jinda nathake, nohoile nijor karone namore.
Pakuti palibe wina wa ife amene amakhala moyo pa yekha ndiponso palibe wina wa ife amene amafa pa yekha.
8 Jodi amikhan jinda thakile, Probhu nimite ase, aru jodi morile bhi, Probhu nimite he mori ase. Etu nimite, jodi amikhan jinda thakilebi morile bhi Probhu nimite he ase.
Ngati ife tikhala ndi moyo, ife tikhala ndi moyo kwa Ambuye. Ndipo ngati ife tifa, tifa kwa Ambuye. Choncho, ngati tikhala ndi moyo kapena kufa, ndife ake a Ambuye.
9 Etu nimite he Khrista mori jaise aru jinda hoise, titia he Tai jinda thaka khan aru mori kene thaka khan sob laga Probhu hobo.
Pa chifukwa ichi, Khristu anafa ndi kuukanso kotero kuti Iye akhale ndi Ambuye wa akufa ndi amoyo.
10 Kintu apuni kele bhai khan uporte bisar kori ase? Aru apuni kele bhai khan ke ninda kori ase? Kelemane amikhan sob Isor pora bisar korate khara koribo.
Tsono nʼchifukwa chiyani iwe ukuweruza mʼbale wako? Kapena nʼchifukwa chiyani ukumunyoza mʼbale wako? Pakuti ife tonse tidzayima pa mpando wakuweruza wa Mulungu.
11 Kelemane eneka likha ase, Probhu he koise, “Moi jinda thaka tak,” sob Moi age te athukaribo, Aru sob manu nijor jiba pora Isor ke shikar koribo.”
Kwalembedwa, akutero Ambuye, “Pamene Ine ndili ndi moyo, aliyense adzandigwadira ndipo lilime lililonse lidzavomereza Mulungu.”
12 Etu karone amikhan sob nijor laga kaam Isor logot te janai dibo.
Choncho tsopano, aliyense wa ife adzafotokoza yekha kwa Mulungu.
13 Etu karone etiya pora amikhan ekjon he ekjon laga bisar nakoribo, kintu tai laga bhai laga theng nalagibo nimite, nohoile bhal laga rasta bondh nakoribo nimite monte rakhibo.
Motero, tiyeni tisiye kuweruzana wina ndi mnzake. Mʼmalo mwake, tsimikizani mʼmaganizo anu kuti musayike chokhumudwitsa kapena chotchinga mʼnjira ya mʼbale wanu.
14 Moi jani ase aru Probhu Jisu naam te thik jani loise, sapha nohua jinis eku bhi nai, kintu kun pora nohoi eneka bhabona kore tai nimite sapha nohoi.
Monga mmodzi amene ndili mwa Ambuye Yesu, ndine wotsimikiza mtima kuti palibe chakudya chimene pachokha ndi chodetsedwa. Koma ngati wina atenga china chake kukhala chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa.
15 Kelemane apuni ki khai ase, etu pora bhai laga mon jokhom kori dile, apuni morom te nathake. Apuni ki khai ase etu pora Khrista kun karone morise Taike nosto na koribi.
Ngati mʼbale wako akuvutika chifukwa cha chimene umadya, iwe sukuchitanso mwachikondi. Usamuwononge mʼbale wako amene Khristu anamufera chifukwa cha chakudya chakocho.
16 Etu karone ki bhal ase eneka apuni pora mani loi ase, etu biya nisena kobole nadibi.
Musalole kuti chimene muchiyesa chabwino achinene ngati choyipa.
17 Kelemane Isor laga rajyo to kha luwa nimite nohoi, kintu Pobitro Atma te dharmikta, aru shanti aru khushi nimite ase.
Pakuti Ufumu wa Mulungu si nkhani yakudya ndi kumwa, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.
18 Kun pora Khrista ke eneka pora sewa kore Isor ke bhi aru manu ke bhi khushi kore.
Nʼchifukwa chake aliyense amene atumikira Khristu mʼnjira iyi akondweretsa Mulungu ndi kuvomerezedwa ndi anthu.
19 Etu karone, ki shanti ase aru ki pora mili kene ekjon-ekjon ke banabo pare etu bisaribi.
Tsono tiyeni tiyesetse kuchita zimene zidzabweretsa mtendere ndi kulimbikitsana mwachikondi.
20 Kha luwa nimite Isor laga kaam nosto na koribi. Sob jinis to hosa bhi sapha ase, kintu ekjon laga kha luwa pora jodi kunba theng lagi bole dise koile, titia etu to galti ase.
Musawononge ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Chakudya chonse ndi choyera, koma munthu amalakwa ngati adya chilichonse chimene chimakhumudwitsa wina.
21 Jodi mangso aru angur ros kha nimite bhai ekjon ke theng lagikena, aru tai paap kori jai nohoile komjur hoijai, tinehoile eitu khan nakhaile he bhal hobo.
Nʼkwabwino kusadya kapena kumwa vinyo kapena kuchita chilichonse chimene chidzachititsa mʼbale wako kugwa.
22 Apuni laga ki biswas ase, apuni majote he rakhibi. Kun he nijor pora mani luwa sob te nijorke galti nabhabi, etu manu asishit ase.
Tsono zimene ukukhulupirira pa zinthu izi zikhale pakati pa iwe ndi Mulungu. Wodala munthu amene sadzitsutsa yekha pa zimene amazivomereza.
23 Kintu kunba pora jodi duita mon kori biya bhabona pora khai koile, etu nijorke ninda kori ase, kelemane etu to biswas pora nohoi. Aru ki biswas te nohoi, etu sob to paap ase.
Koma munthu amene akukayika atsutsidwa ngati adya, chifukwa kudya kwake si kwa chikhulupiriro; ndipo chilichonse chosachokera mʼchikhulupiriro ndi tchimo.

< Romans 14 >