< Waiata 65 >

1 Ki te tino kaiwhakatangi. He himene, he waiata na Rawiri. E taria ana koe, e te Atua, e te whakamoemiti i Hiona: a ka whakamana te kupu taurangi ki a koe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 E te kaiwhakarongo inoi, e haere nga kikokiko katoa ki a koe.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 E kaha ake ana i ahau nga kino: a matou mahi tutu, mau ena e hipoki.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Ka hari te tangata e whiriwhiria e koe, e meatia e koe kia tata atu ki a koe, kia noho i roto i ou marae: ka makona matou i te pai o tou whare, o tou temepara tapu.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 He mea whakawehi, he tapu, tau utu kupu ki a matou, e te Atua o to matou whakaoranga, e te okiokinga o nga pito katoa o te whenua, o te hunga hoki i tawhiti i runga o te moana;
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 E whakau nei i nga maunga, he kaha hoki nona; tona whitiki nei he kaha.
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 E whakamarie nei i te haruru o nga moana, i te haruru o o ratou ngaru, i te ngangau hoki o nga iwi.
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Ka wehi ano ki au tohu te hunga e noho ana i nga pito rawa: hari ana i a koe nga putake o te ata, o te ahiahi.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 E tirotirohia ana e koe te whenua, e whakamakukuria ana, e whakamomonatia nuitia ana e koe; ki tonu te awa o te Atua i te wai: oti rawa ake te whakapai e koe, kua rite mai i a koe he witi mo aua wahi.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Makuku rawa i a koe ona moa, pe ana i a koe ona tupuke: e whakangawaritia ana e koe ki nga ua: e manaakitia ana e koe tona pihinga ake.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 E karaunatia ana e koe te tau ki tou pai; e maturuturu ana hoki te momonatanga o ou ara.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 E maturuturu ana ki nga wahi kai o te koraha: a whitikiria ana nga pukepuke ki te koa.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 He hipi te kakahu o nga wahi kai; ngaro ana nga raorao i te witi; hamama ana ratou i te hari, waiata ana.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Waiata 65 >