< Tauanga 29 >

1 Hei te whitu o nga marama, hei te ra tuatahi o te marama he huihuinga tapu mo koutou; kaua tetahi mahi a te kaimahi e mahia: hei ra whakatangi tetere tena ma koutou.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Me tuku ano he tahunga tinana hei kakara reka ki a Ihowa; kia kotahi puru, hei te kuao, kia kotahi hipi toa, kia whitu nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 A hei te paraoa pai i konatunatua ki te hinu te whakahere totokore, kia toru nga whakatekau mo te puru, kia rua hoki nga whakatekau mo te hipi toa,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Me te whakatekau mo te reme kotahi, o nga reme e whitu;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara, hei whakamarie mo koutou:
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Ko te tahunga tinana ano o te marama, me tona whakahere totokore, ko t tahunga tinana tuturu, me tona whakahere totokore, me nga ringihanga o era, kia rite ki nga ritenga o te pera, hei kakara reka, hei whakahere ahi ki a Ihowa.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 A i te tekau o nga ra o tenei marama, o te whitu, he huihuinga tapu mo koutou: me whakapouri o koutou wairua: kaua tetahi mahi e mahia:
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Engari me tapae he tahunga tinana ki a Ihowa hei kakara reka; kia kotahi puru, hei te kuao, kia kotahi hipi toa, kia whitu nga reme toa tau tahi; hei nga mea kohakore nga mea ma koutou:
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Hei te paraoa pai ano hoki i konatunatua ki te hinu te whakahere totokore mo era, kia toru nga whakatekau mo te puru, kia rua hoki nga whakatekau mo te hipi toa kotahi,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Hei te whakatekau mo te reme, puta noa i nga reme e whitu:
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Kia kotahi koati toa hei whakahere hara; me te whakahere hara hei whakamarie, te tahunga tinana tuturu, me tona whakahere totokore, me nga ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 A hei te tahi tekau ma rima o nga ra o te whitu o nga marama he huihuinga tapu mo koutou; kaua tetahi mahi a te kaimahi e mahia, a kia whitu nga ra e mea hakari ai koutou ki a Ihowa:
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Me tapae ano he tahunga tinana, he whakahere ahi, hei kakara reka ki a Ihowa: kia kotahi tekau ma toru nga puru, hei te kuao, kia rua nga hipi toa, kia kotahi tekau ma wha nga reme toa tau tahi, hei nga mea kohakore:
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Hei te paraoa pai ano i konatunatua ki te hinu te whakahere totokore; kia toru nga whakatekau ki te puru, o nga puru kotahi tekau ma toru, kia rua nga whakatekau ki te hipi toa, ara o nga hipi toa e rua,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Me te whakatekau ki te reme, o nga reme kotahi tekau ma wha:
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Me tetahi koati toa, hei whakahere hara; me te tahunga tinana tuturu ano, me tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Me tuku hoki i te rua o nga ra nga puru kotahi tekau ma rua, hei te kuao, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 A, ko nga whakahere totokore o aua mea, me nga ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi, o nga reme, kia rite ki te maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Kia kotahi koati toa ano hei whakahere hara; tera atu ano te tahunga tinana tuturu me tona whakahere totokore, me nga ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 A, hei te toru o nga ra, kia kotahi tekau ma tahi nga puru, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore;
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 A, ko nga whakahere totokore, me nga ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Kia kotahi koati toa hei whakahere hara; me te whakahere hara tuturu ano, me tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 A i te wha o nga ra kia kotahi tekau nga puru, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Na, ko nga whakahere totokore me nga ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara; me te tahunga tinana tuturu ano, me tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 A i te rima o nga ra kia iwa nga puru, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 A, ko nga whakahere totokore, me nga ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara; tera ano te tahunga tinana tuturu, me tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 A i te ono o nga ra kia waru nga puru, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 A, ko nga whakahere totokore, me nga ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara: tera ano te tahunga tinana tuturu, tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 A, i te whitu o nga ra, kia whitu nga puru, kia rua nga hipi toa, kia tekau ma wha nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 A, ko nga whakahere totokore, me o ratou ringihanga, ara o nga puru, o nga hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara; tera ano te tahunga tinana tuturu, tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Hei te waru o nga ra he huihuinga nui ma koutou: kaua tetahi mahi a te kaimahi e mahia.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Engari me tapae he tahunga tinana, he whakahere ahi, he kakara reka ki a Ihowa; kia kotahi puru, kia kotahi hipi toa, kia whitu nga reme toa tau tahi, he mea kohakore:
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 A, ko nga whakahere totokore, me o ratou ringihanga, ara o te puru, o te hipi toa, o nga reme, kia rite ki to ratou maha, kia rite ki te ritenga:
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Kia kotahi koati toa ano hoki hei whakahere hara; tena ano te tahunga tinana tuturu, me tona whakahere totokore, me tona ringihanga.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Ko enei a koutou e mea ai ki a Ihowa i a koutou hakari nunui, haunga a koutou ki taurangi, me a koutou tahunga tinana, me a koutou whakahere totokore, a koutou ringihanga, me a koutou whakahere mo te pai.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Na ka korerotia e Mohi ki nga tama a Iharaira nga mea katoa i whakahau ai a Ihowa ki a Mohi.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Tauanga 29 >