< Ehekiera 35 >

1 I puta mai ano te kupu a Ihowa ki ahau, i mea,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 E te tama a te tangata, anga atu tou mata ki Maunga Heira, poropititia te he mo reira,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 Mea atu hoki ki a ia, Ko te kupu tenei a te Ariki, a Ihowa; Nana, hei hoariri ahau mou, e Maunga Heira, a ka totoro atu toku ringa ki a koe, ka ururua rawa koe i ahau, ka meinga hoki hei miharotanga.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Ko ou pa ka tuhea i ahau, a hei ururua koe, a ka mohio koe ko Ihowa ahau.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 No te mea he mauahara mau tonu tou, a kua tukua e koe nga tama a Iharaira ki te kaha o te hoari i te wa o to ratou aitua, i te wa o te he i te mutunga.
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 Mo reira, e ora ana ahau, e ai ta te Ariki, ta Ihowa, ka mahia koe e ahau hei mea mo te toto, ka whaia ano koe e te toto; kihai na koe i kino ki te toto, na ka whaia koe e te toto.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Heoi ka meinga e ahau a Maunga Heira hei matakitakinga, hei ururua; a ka hatepea atu e ahau te tangata e tika ana na reira, te tangata ano e hoki mai ana.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 A ka whakakiia e ahau ona maunga ki ona tupapaku: a, ko te hunga e patua ki te hoari, ka hinga ki ou pukepuke, ki ou awaawa, ki ou rerenga wai katoa.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Ka ururua koe i ahau a ake ake; e kore ano ou pa e nohoia, a ka mohio koutou ko Ihowa ahau.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Na, kua mea na koe, Ko enei iwi e rua, ko enei whenua e rua moku, mo tatou tonu hoki; i te mea kei reira nei ano a Ihowa;
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 Mo reira, e ora ana ahau, e ai ta te Ariki, ta Ihowa, ko taku mahi ka rite ki tou riri, ki tou hae, i hae ai koe i a koe i mauahara ra ki a ratou; a ka whakakitea atu ahau ki a ratou, ina rite i ahau te whakawa mou.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Na ka mohio koe ko Ihowa ahau, a kua rangona e ahau au kohukohu katoa i korerotia e koe mo nga maunga o Iharaira, i a koe i ki ra, Kua ururua, kua homai hei kai ma tatou.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 A kua whakakake mai o koutou mangai ki ahau, kua whakamaha i a koutou kupu moku: kua rongo ahau.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Ko te kupu tenei a te Ariki, a Ihowa; A te wa e koa ai te whenua katoa, ka ururua koe i ahau.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 I koa na koe ki te kainga o te whare o Iharaira, kua ururua na, ka pena ano ahau ki a koe: ka ururua koe, e Maunga Heira, e Eroma katoa, ae ra, katoa; a ka mohio ratou ko Ihowa ahau.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ehekiera 35 >