< Zakaria 9 >
1 Fetse; miatrek’ an-tane’ i Hadrake mpitofa e Damesèke, ty tsara’ Iehovà; (mitolik’ am’ Iehovà ty fihaino’ ondatio naho ze hene’ fifokoa’Israele; )
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
2 naho amy Kamate mpiefetse ama’ey; naho amy Tsore vaho amy Tsidone, amy t’ie mahihitse.
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 Toe namboatse rova fatratse t’i Tsore le nampitoabotse volafoty hoe deboke naho volamena ki’e hoe fotak’ an-damoke.
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Inao t’ie hampikoahe’ i Talè, havatambia’e mb’ an-driak’ añe ty haozara’e; vaho ho forototoe’ ty afo.
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
5 Hahaisake zay ty Askelone vaho hiria-kolitse, hangirifiry ka t’i Azà, naho i Ekrone ty amy fitamà’e nilesay; hihomake ty mpanjaka’ i Azà le tsy ho amam-pimoneñe ty Askelone.
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 Anak’ amontoñe ty hitoboke e Ashdode, vaho haitoako ty fisengea’ o nte-Pilistio.
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 Hafahako am-bava’e ao ty lio’e naho an-tsifim-pamotsi’e ao o raha mampangorìñeo; fa o sehanga’eo ty ho an’ Andrianañaharen-tika, ie ty hanoeñe mpiaolo e Iehodà ao, vaho hanahake ty nte-Iebose t’i Ekrone.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 Hitobe am-piarikatoha’ i kivohokoy raho ty amo lahindefoñeo, ty amy miary eo naho mibalike vaho tsy hisoroha’ ty mpamorekeke ka, fa ho jilove’ o masokoo henane zao.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
9 Mandià taroba ry anak’ampela’ i Tsione, mipoñafa ry anak’ ampela’ Ierosalaime; Hehe te mitotsak’ ama’o ty Mpanjaka’o, Vantan-dre, reketse fandrombahañe, mirèke, miningitse borìke, ambone’ ty fola-bao, ana’ty borìke vave’e.
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Le hapitsoko amy Efraime ty sarete, naho am’ Ierosalaime ty soavala, naho ho pozaheko o fàlen-kotakotakeo; ie hitsara fampilongoañe amo kilakila’ ondatio, vaho hitakatse an-driake ey pak’ an-driak’ añe i fifehea’ey, naho boak’amy Sakay añe pak’ añ’ olo-ty tane toy.
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 Le ihe, ty amy lio’ i fañina ama’oiy, hampiavoteko boak’ an-koboñe tsy aman-drano ao o azo an-drohio.
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Mimpolia mb’an-drova fatratse mb’ eo, ry mpirohy mitamàñeo; anito ty ho koiheko te hondroheko in-droe o azoo.
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Ampivohoreko hoe te faleko t’Iehodà, atsafeko amy faley ty Efraime; naho ho troboeko o ana’oo ry Tsione, hatreatré’e o ana’oo ry Iavane, ie hampanahafeko amy fibaram-panalolahiy.
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
14 Ho oniñe ambone’ iereo eo t’Iehovà, naho hihiririñe hoe helatse i ana-pale’ey; ho tiofe’ Iehovà, Talè i antsivay, vaho hijoñe an-tangololahi’ i atimoy.
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 Ie harova’ Iehovà’ i Màroy; le hampibotseke iereo handialia o vato-piletseo; hìnoñe iereo naho hiroharoha hoe an-divay; hatsafeñe hoe an-tsoakazo, kotsa hoe an-kotso’ i kitreliy eo.
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
16 Handrombake iareo amy andro zay t’Iehovà Andrianañahare’ iareo ho lia-rai’ ondati’eo, ho vatosoan-tsabaka’e, mimilemiletse an-tane’e eo.
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Akore ty hafanjàka naho hatsomerentsere’ iareo! Hampiraorao o ajalahio ty ampemba naho o somondrarao ty divai-vao.
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.