< Romana 6 >

1 Aa vaho hanao ty hoe hao tika: Antao hitolom-pandilatse hampitomambao ty hasoa!
Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe?
2 Sondo’e! Akore t’ie nihomake an-kakeo ro mbe ho veloñ’ ama’e?
Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo?
3 He tsy fohi’ areo te itikañ’ iaby nilipotse am’ Iesoà Norizañey ro nilipotse amy havilasi’ey.
Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake?
4 Aa le nitrao-pilenteke ama’e tika amy lipotsey mb’an-kavilasy ao, soa te, hambañe ami’te nampitroare’ ty engen-dRae an-kavilasy i Norizañey, ty hañaveloan-tika an-kavelom-bao.
Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.
5 Aa naho nampireketeñe ama’e tika an-kavilasy manahake aze, le ho mpiamy fivañonan-ko velo’ey ka tika,
Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake.
6 ie fohiñe te naradorado mindre ama’e i vatan-tika hambo’ey, hañitoañe i sandriñe lifo-kakeoy, soa tsy hondevozen-tahiñe ka,
Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo
7 amy te votsotse an-kakeo ze fa nihomake.
chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.
8 Aa kanao niharo vilasy amy Norizañey tika, le atokisan-tika te hindrezañe an-kaveloñe ka,
Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye.
9 fohiñe te natroatse amy havilasiy i Norizañey tsy ho vilasy ka, amy te tsy anaña’ i havilasiy lily.
Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye.
10 I havilasy nivetraha’ey, le nivetraha’e ty amo hakeoo indraike nahaheneke; fe i haveloñe iveloma’ey, ro iveloma’e aman’ Añahare.
Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.
11 Iantofo arè te nihomake an-kakeo nahareo, fe veloñe aman’ Añahare am’ Iesoà Norizañey.
Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu.
12 Aa le ko atolotse ho fehèn-kakeo o sandri’ areo ho momokeo, hivohots’ amo hadrao’eo.
Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa.
13 Le ko atolo’ areo an-tahiñe o fangefange’ areoo ho harao-katsivokarañe, fe manolora vatañe aman’ Añahare hoe nivelomeñe an-kavilasy; vaho o fangefange’ areoo ho haraon-kavantañañe aman’ Añahare,
Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo.
14 amy te tsy hanan-dily ama’ areo o hakeoo, amy t’ie tsy ambane’ ty fimanemanean-dily, fa ambanem-patarihañe.
Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
15 Akore arè? Handilatse hao tika amy te tsy fehèm-pepètse fa ambanem-patarihañe? Aiy, sondo’e!
Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi!
16 Tsy fohi’ areo hao te, ze anolora’ areo sandriñe ho mpitoro’e hivohora’o, le ondevo’ i vohorañey?—ke amo tahiñeo minday mb’am-pikoromahañe, he am-pivohorañe minday havantañañe.
Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake.
17 Ty fatarihan’ Añahare, inahareo nondevozen-kakeo fe mivohotse añ’arofo amo ventem-pañòhañe nitaroñañeo,
Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira.
18 le fa hinaha an-kakeo vaho mpitoron-kavantañañe.
Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.
19 Anoeko an-dreha’ ondaty ty amy haifoifo’ o sandri’ areoo: Fa hambañe amy te nafoe’areo hondevozen-kakeo naho tahiñe o fangefangeo hañonjonañe ty hatsivokarañe; t’ie hibanabana o fangefangeo hito­ron-kavañonañe mb’am-piavahañe henane zao.
Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima.
20 Ie nitoron-kakeo taolo, le nihaha amy havantañañey.
Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo.
21 Aa le inoñe ty nivokareñe amo raha man­ala­tse anahareo henaneo? kanao ampigadoñe’e an-kamomohañe.
Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa!
22 Aa ie hinaha an-kakeo naho mivohotse aman’ Añahare henaneo, ro mahazo ty hasoa i fiavahañey ie mamokatse haveloñe tsy modo. ­ (aiōnios g166)
Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
23 Fihomahañe ty valen-kakeo, fe haveloñe nainai’e ro fatarihan’ Añahare amy Talèntika Iesoà Norizañey. (aiōnios g166)
Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios g166)

< Romana 6 >