< Salamo 98 >
1 Takasio sabo vao t’Iehovà fa nahafonitse raha fanjaka; nahazoa’e fandrebahañe i fità’e havanay naho i sira’e masiñey.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 Fa nampahafohine’ Iehovà i fandrombaha’ey; naboa’e ampahaisaha’ o kilakila ‘ndatio ty havantaña’e.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 Nitiahi’e ty fiferenaiña’e naho ty figahiña’e amy anjomba’ Israeley, fonga nahaoniñe ty fandrombahan’ Andrianañaharentika ze olon-tane.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Mipoñafa am’ Iehovà, ry tane toy iaby, Mirañorañoa an-drebeke, eka mandrengea an-tsabo.
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Sabò t’Iehovà arahen-jejo-bory, i jejo-boriy mañara-takasy;
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 Reke-trompetra naho fivolañ’ antsiva— mipozaha an-drebek’ añatrefa’ Iehovà Mpanjaka.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Hitroñe ami’ty halifora’e i riakey, ty voatse toy vaho o mpimoneñe ama’eo.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Hitehateha-taña o sorotombakeo, le hitrao-pisabo an-kaehake o vohitseo,
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 añatrefa’ Iehovà eo fa homb’eo re hizaka ty tane toy. ho zakae’e an-kavantañañe ty voatse toy, naho an-kahiti’e ondatio.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.